< Yesaya 6 >

1 Chaka chimene mfumu Uziya anamwalira, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando waufumu, wautali ndi wokwezedwa, ndipo mkanjo wawo unali wautali; kotero kuti unadzaza mʼNyumba ya Yehova.
Ngomnyaka inkosi u-Uziya eyafa ngawo, ngabona uThixo ehlezi esihlalweni sobukhosi esiphezulu esiphakemeyo, injobo yesembatho sakhe igcwele ithempeli.
2 Pamwamba pawo panayimirira Aserafi, aliyense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi: awiri anaphimba nkhope zawo, awiri anaphimba mapazi awo, ndipo awiri ankawulukira.
Ngaphezu kwakhe kwakulamaserafimu, elinye lelinye lilempiko eziyisithupha. Ayegubuzele ubuso bawo ngezimpiko ezimbili, egubuzele inyawo zawo ngezimbili, ephapha ngezimbili.
3 Ndipo Aserafiwo amafuwulirana kuti “Woyera, woyera, woyera Yehova Wamphamvuzonse. Dziko lonse lapansi ladzaza ndi ulemerero wake.”
Elinye lamemezela kwelinye lisithi: “Ungcwele, ungcwele, ungcwele uThixo uSomandla, umhlaba wonke ugcwele inkazimulo yakhe.”
4 Chifukwa cha kufuwulako maziko a zitseko ndi ziwundo anagwedezeka ndipo mʼNyumba ya Yehova munadzaza utsi.
Ekuzwakaleni kwamazwi awo imigubazi lombundu kwanyikinyeka, kwathi ithempeli lagcwala intuthu.
5 Tsono ine ndinafuwula kuti, “Tsoka langa ine! Ndatayika! Pakuti ndine munthu wapakamwa poyipa, ndipo ndimakhala pakati pa anthu a pakamwa poyipa, ndipo ndi maso anga ndaona mfumu Yehova Wamphamvuzonse.”
Mina ngakhala ngathi, “Maye mina! Sengibhujisiwe! Ngoba ngingumuntu olezindebe ezingcolileyo, njalo ngihlala phakathi kwabantu abalezindebe ezingcolileyo, lamehlo ami asebone iNkosi, uThixo uSomandla.”
6 Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja anawulukira kwa ine ali ndi khala lamoto mʼdzanja lake, khala limene analichotsa ndi mbaniro pa guwa lansembe.
Lapho-ke elinye lamaserafimu laphaphela kimi liphethe ilahle elivuthayo esandleni salo elalilithethe ngodlawu e-alithareni.
7 Ndipo anandikhudza pakamwa panga ndi khala lamotolo nati, “Taona ndakhudza pa milomo yako ndi khalali; kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.”
Lathinta umlomo wami ngalo lathi, “Khangela, lokhu sekuthinte izindebe zakho; icala lakho selisusiwe, njalo lesono sakho sesihlawulelwe.”
8 Kenaka ndinamva mawu a Ambuye akuti, “Kodi ndidzatuma yani? Ndipo ndani adzapite mʼmalo mwathu?” Ndipo ine ndinati, “Ndilipo. Tumeni!”
Ngasengisizwa ilizwi leNkosi lisithi, “Ngizathuma bani na? Ngubani na ozasihambela?” Mina ngathi, “Ngilapha. Ngithuma!”
9 Yehova anati, “Pita ndipo ukawawuze anthu awa: “‘Kumva muzimva, koma osamvetsetsa; kupenya muzipenya koma osaona kanthu.’
Yasisithi, “Hamba uyetshela abantu uthi: ‘Zwanini kokuphela, kodwa lingaqedisisi; libone kokuphela, kodwa lingabonisisi.’
10 Tsono anthu amenewa uwaphe mtima; uwagonthetse makutu, ndipo uwatseke mʼmaso. Mwina angaone ndi maso awo, angamve ndi makutu awo, angamvetse ndi mitima yawo, kenaka ndi kutembenuka mtima ndi kuchiritsidwa.”
Yenza inhliziyo yalababantu ibe lukhuni; wenze indlebe zabo zibe buthundu, uvale amehlo abo. Hlezi babone ngamehlo abo, bezwe ngezindlebe zabo, baqedisise ngezinhliziyo zabo, baphenduke basiliswe.”
11 Pamenepo ine ndinati, “Zimenezo ndi mpaka liti Inu Ambuye?” Ndipo Iyeyo anandiyankha kuti, “Mpaka mizinda itasanduka mabwinja nʼkusowa wokhalamo, mpaka nyumba zitasowa anthu okhalamo, mpaka dziko litasanduka chipululu ndithu,
Ngasengisithi, “Koze kube nini, Nkosi?” Yona yaphendula yathi: “Amadolobho aze achitheke njalo kungaselabantu kuwo, izindlu zize zisale zingaselabantu, lamasimu ephundleke abhuquzeka,
12 mpaka Yehova atasamutsira aliyense kutali, dziko nʼkusiyidwa kwathunthu.
uThixo aze axotshele umuntu wonke khatshana njalo ilizwe lidelwe ngokupheleleyo.
13 Ndipo ngakhale chigawo chakhumi cha anthu chitatsala mʼdziko, nachonso chidzawonongedwa. Koma monga momwe mitengo ya muwanga ndi thundu imasiyira chitsa pamene ayidula, chonchonso mbewu yoyera idzatsalira ngati chitsa chotsala mʼdziko.”
Lanxa ingxenye eyodwa etshumini isala elizweni izachithwa futhi. Kodwa njengezihlahla zetherebhinti lemi-okhi zitshiya izidindi lapho seziganyulwe, ngokunjalo inhlanyelo engcwele izakuba yisidindi elizweni.”

< Yesaya 6 >