< Yesaya 6 >

1 Chaka chimene mfumu Uziya anamwalira, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando waufumu, wautali ndi wokwezedwa, ndipo mkanjo wawo unali wautali; kotero kuti unadzaza mʼNyumba ya Yehova.
I KA makahiki i make ai ke alii, o Uzia, ike aku la au i ka Haku, e noho ana ma ka nohoalii kiekie, i hapaiia, a piha ka luakini i kona hua lole.
2 Pamwamba pawo panayimirira Aserafi, aliyense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi: awiri anaphimba nkhope zawo, awiri anaphimba mapazi awo, ndipo awiri ankawulukira.
Ku mai la maluna, ma o na la, na Serapima; he paono, he paono na eheu ia lakou a pau. Me na mea elua ia i uhi ai i kona maka, me na mea elua ia i uhi ai i kona mau wawae, a me na mea elua ia i lele ai.
3 Ndipo Aserafiwo amafuwulirana kuti “Woyera, woyera, woyera Yehova Wamphamvuzonse. Dziko lonse lapansi ladzaza ndi ulemerero wake.”
A hea ae la kekahi i kekahi, Ihiihi, ihiihi, ihiihi no o Iehova o na kaua. Ua piha ka honua i kona nani.
4 Chifukwa cha kufuwulako maziko a zitseko ndi ziwundo anagwedezeka ndipo mʼNyumba ya Yehova munadzaza utsi.
Haalulu na paepaepuka, i ka leo o ka mea nana i hea, a piha iho la ka hale i ka uwahi.
5 Tsono ine ndinafuwula kuti, “Tsoka langa ine! Ndatayika! Pakuti ndine munthu wapakamwa poyipa, ndipo ndimakhala pakati pa anthu a pakamwa poyipa, ndipo ndi maso anga ndaona mfumu Yehova Wamphamvuzonse.”
Alaila, olelo iho la au, Auwe au! ua make au; no ka mea, he kanaka lehelehe haumia au, a ke noho nei au iwaena o ka lahuikanaka lehelehe haumia; no ka mea, na ike ko'u mau maka i ke alii, ia Iehova o na kaua.
6 Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja anawulukira kwa ine ali ndi khala lamoto mʼdzanja lake, khala limene analichotsa ndi mbaniro pa guwa lansembe.
A lele mai la kekahi o na Serapima io'u nei, aia ma kona lima ka pohaku enaena, ana i lawe ai, mai ke kuahu mai, me na upa ahi.
7 Ndipo anandikhudza pakamwa panga ndi khala lamotolo nati, “Taona ndakhudza pa milomo yako ndi khalali; kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.”
A hoopa mai la ma kuu waha, i mai la, Aia hoi, ua hoopa keia ma kou mau lehelehe, ua laweia kou hewa, ua kalaia kou hala.
8 Kenaka ndinamva mawu a Ambuye akuti, “Kodi ndidzatuma yani? Ndipo ndani adzapite mʼmalo mwathu?” Ndipo ine ndinati, “Ndilipo. Tumeni!”
A lohe iho la no hoi au i ka leo o ka Haku, i ka i ana mai, Iawai la wau e hoouna aku ai? A owai ka mea nana e hele no kakou? Alaila, i aku la au, Eia no wau, e hoouna ia'u.
9 Yehova anati, “Pita ndipo ukawawuze anthu awa: “‘Kumva muzimva, koma osamvetsetsa; kupenya muzipenya koma osaona kanthu.’
I mai la ia, O hele, e olelo aku i keia poe kanaka, I ka lohe ana, e lohe no oukou, aole nae e hoomaopopo, I ka ike ana, e ike no, aole nae e akaka ka ike ana.
10 Tsono anthu amenewa uwaphe mtima; uwagonthetse makutu, ndipo uwatseke mʼmaso. Mwina angaone ndi maso awo, angamve ndi makutu awo, angamvetse ndi mitima yawo, kenaka ndi kutembenuka mtima ndi kuchiritsidwa.”
E hoopalaka i ka naau o keia poe kanaka, E hookuli i ko lakou pepeiao, A e hoopaa i ko lakou maka; O ike ko lakou mau maka, A lohe hoi ko lakou mau pepeiao, A hoomaopopo ko lakou naau, A huli lakou, a hoolaia mai lakou.
11 Pamenepo ine ndinati, “Zimenezo ndi mpaka liti Inu Ambuye?” Ndipo Iyeyo anandiyankha kuti, “Mpaka mizinda itasanduka mabwinja nʼkusowa wokhalamo, mpaka nyumba zitasowa anthu okhalamo, mpaka dziko litasanduka chipululu ndithu,
Alaila, i aku la au, E ka Haku, pehea ka loihi? I mai la ia, A neoneo na kulanakauhale, aohe mea noho iloko, A kanaka ole ko lakou hale, A anai loa ia'ku ka aina,
12 mpaka Yehova atasamutsira aliyense kutali, dziko nʼkusiyidwa kwathunthu.
A lawe loihi aku o Iehova i na kanaka, A mahuahua ka olohelohe ana mawaenakonu o ka aina;
13 Ndipo ngakhale chigawo chakhumi cha anthu chitatsala mʼdziko, nachonso chidzawonongedwa. Koma monga momwe mitengo ya muwanga ndi thundu imasiyira chitsa pamene ayidula, chonchonso mbewu yoyera idzatsalira ngati chitsa chotsala mʼdziko.”
Ina i koe kekahi hapaumi o na mea, E anai loa ia'ku no ia. Aka, e like me ka laau hukaa, a me ka oka, I ka wa i kuaia, ua koe no ke kumu; Pela no e lilo ai kekahi mamo hemolele, I kumu hoolaha no lakou.

< Yesaya 6 >