< Yesaya 6 >

1 Chaka chimene mfumu Uziya anamwalira, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando waufumu, wautali ndi wokwezedwa, ndipo mkanjo wawo unali wautali; kotero kuti unadzaza mʼNyumba ya Yehova.
L'année de la mort du roi Ozias, je vis le Seigneur assis sur un trône, haut et élevé, et sa traîne remplissait le temple.
2 Pamwamba pawo panayimirira Aserafi, aliyense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi: awiri anaphimba nkhope zawo, awiri anaphimba mapazi awo, ndipo awiri ankawulukira.
Au-dessus de lui se tenaient les séraphins. Chacun d'eux avait six ailes. De deux ailes, il se couvrait le visage. De deux, il se couvrait les pieds. De deux ailes, il volait.
3 Ndipo Aserafiwo amafuwulirana kuti “Woyera, woyera, woyera Yehova Wamphamvuzonse. Dziko lonse lapansi ladzaza ndi ulemerero wake.”
L`un d`eux appela l`autre, et dit, « Saint, saint, saint, Yahvé des armées! La terre entière est remplie de sa gloire! »
4 Chifukwa cha kufuwulako maziko a zitseko ndi ziwundo anagwedezeka ndipo mʼNyumba ya Yehova munadzaza utsi.
Les fondements des seuils ont tremblé à la voix de celui qui appelait, et la maison s'est remplie de fumée.
5 Tsono ine ndinafuwula kuti, “Tsoka langa ine! Ndatayika! Pakuti ndine munthu wapakamwa poyipa, ndipo ndimakhala pakati pa anthu a pakamwa poyipa, ndipo ndi maso anga ndaona mfumu Yehova Wamphamvuzonse.”
Alors je dis: « Malheur à moi! Car je suis perdu, parce que je suis un homme aux lèvres impures et que j'habite au milieu d'un peuple aux lèvres impures, car mes yeux ont vu le Roi, Yahvé des Armées! »
6 Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja anawulukira kwa ine ali ndi khala lamoto mʼdzanja lake, khala limene analichotsa ndi mbaniro pa guwa lansembe.
Et l'un des séraphins vola vers moi, tenant à la main un charbon vivant qu'il avait pris sur l'autel avec les pinces.
7 Ndipo anandikhudza pakamwa panga ndi khala lamotolo nati, “Taona ndakhudza pa milomo yako ndi khalali; kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.”
Il en toucha ma bouche, et dit: « Voici, ceci a touché tes lèvres; ton iniquité est effacée, et ton péché est pardonné. »
8 Kenaka ndinamva mawu a Ambuye akuti, “Kodi ndidzatuma yani? Ndipo ndani adzapite mʼmalo mwathu?” Ndipo ine ndinati, “Ndilipo. Tumeni!”
J'ai entendu la voix du Seigneur, qui disait: « Qui enverrai-je et qui ira pour nous? » Alors j'ai dit: « Me voici. Envoyez-moi! »
9 Yehova anati, “Pita ndipo ukawawuze anthu awa: “‘Kumva muzimva, koma osamvetsetsa; kupenya muzipenya koma osaona kanthu.’
Il dit: « Va, et dis à ce peuple, Vous entendez en effet, mais ne comprennent pas. Vous voyez en effet, mais ne perçoivent pas.
10 Tsono anthu amenewa uwaphe mtima; uwagonthetse makutu, ndipo uwatseke mʼmaso. Mwina angaone ndi maso awo, angamve ndi makutu awo, angamvetse ndi mitima yawo, kenaka ndi kutembenuka mtima ndi kuchiritsidwa.”
Rends gras le cœur de ce peuple. Rendez leurs oreilles lourdes, et fermez leurs yeux; de peur qu'ils ne voient avec leurs yeux, entendent avec leurs oreilles, comprennent avec leur cœur, et retournez-vous, et soyez guéri. »
11 Pamenepo ine ndinati, “Zimenezo ndi mpaka liti Inu Ambuye?” Ndipo Iyeyo anandiyankha kuti, “Mpaka mizinda itasanduka mabwinja nʼkusowa wokhalamo, mpaka nyumba zitasowa anthu okhalamo, mpaka dziko litasanduka chipululu ndithu,
Alors j'ai dit: « Seigneur, combien de temps? » Il a répondu, « Jusqu'à ce que les villes soient des déchets sans habitant, des maisons sans homme, la terre devient complètement désolée,
12 mpaka Yehova atasamutsira aliyense kutali, dziko nʼkusiyidwa kwathunthu.
et Yahvé a éloigné les hommes, et les lieux abandonnés sont nombreux dans le pays.
13 Ndipo ngakhale chigawo chakhumi cha anthu chitatsala mʼdziko, nachonso chidzawonongedwa. Koma monga momwe mitengo ya muwanga ndi thundu imasiyira chitsa pamene ayidula, chonchonso mbewu yoyera idzatsalira ngati chitsa chotsala mʼdziko.”
S'il lui reste un dixième, qui seront également consommés à leur tour, comme un térébinthe, et comme un chêne dont il reste la souche lorsqu'ils sont abattus, alors la semence sainte est sa souche. »

< Yesaya 6 >