< Yesaya 59 >

1 Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa, kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
Еда не может рука Господня спасти? Или отягчил есть слух Свой, еже не услышати?
2 Koma zoyipa zanu zakulekanitsani ndi Mulungu wanu; ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu, kotero Iye sadzamva.
Но греси ваши разлучают между вами и между Богом, и грех ради ваших отврати лице Свое от вас еже не помиловати.
3 Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi. Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu. Pakamwa panu payankhula zabodza, ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
Руце бо ваши осквернене кровию, и персты ваши во гресех, устне же ваши возглаголаша беззаконие, и язык ваш неправде поучается.
4 Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama, palibe amene akupita ku mlandu moona mtima. Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza; amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
Никтоже глаголет правды, ниже есть суд истинен: уповают на суетная и глаголют тщетная, яко зачинают труд и раждают беззаконие.
5 Iwo amayikira mazira a mamba ndipo amaluka ukonde wakangawude. Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa, ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
Яица аспидска разбиша и постав паучинный ткут, и хотяй от яиц их ясти, разбив запорток (его), обрете и в нем василиска.
6 Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala; ndipo chimene apangacho sangachifunde. Ntchito zawo ndi zoyipa, ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
Постав их не будет на ризу, и не одеждутся от дел своих: дела бо их дела беззакония.
7 Amathamangira kukachita zoyipa; sachedwa kupha anthu osalakwa. Maganizo awo ndi maganizo oyipa; kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
Нозе же их на зло текут, скори пролияти кровь, и мысли их мысли о убийствах: сокрушение и бедность во путех их,
8 Iwo sadziwa kuchita za mtendere; zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo. Njira zawo zonse nʼzokhotakhota; aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
и пути мирнаго не познаша, и несть суда во путех их: стези во их развращены, по нихже ходят и не ведят мира.
9 Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira; ndipo chipulumutso sichitifikira. Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha; tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
Того ради отступи от них суд, и не постигнет их правда: ждущым им света, бысть им тма, ждуще зари во мраце ходиша.
10 Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona, kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso. Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku; timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
Осяжут яко слепии стену, яко суще без очес осязати будут, и падутся в полудни яко в полунощи, яко умирающе возстенут
11 Tonse timabangula ngati zimbalangondo: Timalira modandaula ngati nkhunda. Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza. Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
яко медведь, и яко голубь вкупе пойдут. Ждахом суда, и несть, спасение далече отступи от нас.
12 Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu, ndipo machimo athu akutsutsana nafe. Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse ndipo tikuvomereza machimo athu:
Много бо беззаконие наше пред Тобою, и греси наши противу сташа нам: беззакония бо наша в нас, и неправды нашя уразумехом:
13 Tawukira ndi kumukana Yehova. Tafulatira Mulungu wathu, pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova, ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
нечествовахом и солгахом и отступихом от последования Бога нашего: глаголахом неправду и не покорихомся, во утробе зачахом и поучихомся от сердца нашего словесем неправедным:
14 Motero kuweruza kolungama kwalekeka ndipo choonadi chili kutali ndi ife; kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu, ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
и оставихом созади суд, и правда далече отступи от нас: яко изнеможе во путех их истина, и правым (путем) не возмогоша прейти:
15 Choonadi sichikupezeka kumeneko, ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto. Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa kuti panalibe chiweruzo cholungama.
и истина взяся, и преставиша ум свой еже смыслити. И виде Господь и негодова, яко не бяше суда:
16 Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe, Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera; Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza, ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
и виде, и не бяше мужа, и помысли, и не бяше избавляющаго: и мсти им мышцею Своею, и помилованием утверди.
17 Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa, ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso; anavala kulipsira ngati chovala ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
И одеяся правдою яко щитом, и возложи шлем спасения на главу, и облечеся в ризу отмщения, и одеждею Своею:
18 Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake molingana ndi zimene anachita, adzaonetsa ukali kwa adani ake ndi kubwezera chilango odana naye. Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
яко воздаваяй воздаяние укоризну супостатом.
19 Choncho akadzabwera ngati madzi oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho. Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
И убоятся, иже от запад, имене Господня, и иже от восток солнца, имене Его славнаго: приидет бо яко река насильная гнев от Господа, приидет со яростию.
20 “Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,” akutero Yehova.
И приидет Сиона ради Избавляяй, и отвратит нечестие от Иакова.
21 Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,” akutero Yehova.
И сей им иже от Мене завет, рече Господь: Дух Мой, иже есть в тебе, и глаголголы, яже Аз дах во уста твоя, не оскудеют от уст твоих и от уст семене твоего: рече бо Господь отныне и во век.

< Yesaya 59 >