< Yesaya 59 >

1 Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa, kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
Khangela isandla seNkosi kasifinyezwanga ukuthi singasindisi, lendlebe yayo kayinzima ukuthi ingezwa.
2 Koma zoyipa zanu zakulekanitsani ndi Mulungu wanu; ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu, kotero Iye sadzamva.
Kodwa iziphambeko zenu zehlukanisile phakathi kwenu loNkulunkulu wenu, lezono zenu zibusithile ubuso bakhe kini, ukuthi angezwa.
3 Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi. Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu. Pakamwa panu payankhula zabodza, ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
Ngoba izandla zenu zingcoliswe ngegazi, leminwe yenu ngenkohlakalo; indebe zenu zikhulume amanga, lolimi lwenu lungunguna ububi.
4 Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama, palibe amene akupita ku mlandu moona mtima. Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza; amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
Kakho omemeza ngokulunga, njalo kakho olabhela ngeqiniso; bathemba okuyize, bakhulume amanga; bamitha ububi, bazale isiphambeko.
5 Iwo amayikira mazira a mamba ndipo amaluka ukonde wakangawude. Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa, ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
Bachamusela amaqanda enhlangwana, beluke ubulembu besayobe; odla okwamaqanda awo uyafa; lelichotshoziweyo liqhamuka lilibululu.
6 Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala; ndipo chimene apangacho sangachifunde. Ntchito zawo ndi zoyipa, ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
Ubulembu babo kabuyikuba yizembatho, njalo kabayikuzembesa ngemisebenzi yabo. Imisebenzi yabo yimisebenzi yobubi, lesenzo sodlakela sisezandleni zabo.
7 Amathamangira kukachita zoyipa; sachedwa kupha anthu osalakwa. Maganizo awo ndi maganizo oyipa; kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
Inyawo zabo zigijimela ebubini; baphangisa ukuchitha igazi elingelacala; imicabango yabo yimicabango yobubi; ukubhubhisa lokuchitha kusezindleleni zabo.
8 Iwo sadziwa kuchita za mtendere; zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo. Njira zawo zonse nʼzokhotakhota; aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
Indlela yokuthula kabayazi; njalo kakulasahlulelo emikhondweni yabo; bazenzela izindlela zabo ezimazombazombe; loba ngubani ohamba kuzo kayikwazi ukuthula.
9 Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira; ndipo chipulumutso sichitifikira. Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha; tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
Ngakho-ke isahlulelo sikhatshana lathi, lokulunga kakusifinyeleli. Silindela ukukhanya, kodwa khangela, ubumnyama; silindela ukukhazimula, kodwa sihamba emnyameni omkhulu.
10 Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona, kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso. Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku; timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
Siphumputha umduli njengeziphofu, siphumputhe kwangathi kasilamehlo; sikhubeke emini enkulu kwangathi kukusihlwa, sisendaweni ezichithekileyo njengabafileyo.
11 Tonse timabangula ngati zimbalangondo: Timalira modandaula ngati nkhunda. Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza. Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
Sonke siyabhonga njengamabhere, silile lokulila njengamajuba; silindela isahlulelo, kodwa kasikho; losindiso, kodwa lukhatshana lathi.
12 Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu, ndipo machimo athu akutsutsana nafe. Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse ndipo tikuvomereza machimo athu:
Ngoba iziphambeko zethu zandile phambi kwakho, lezono zethu zifakaza zimelene lathi; ngoba iziphambeko zethu zilathi, lobubi bethu siyabazi;
13 Tawukira ndi kumukana Yehova. Tafulatira Mulungu wathu, pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova, ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
ukuphambuka, lokuqambela iNkosi amanga, lokusuka ekulandeleni uNkulunkulu wethu, ukukhuluma incindezelo lokuhlamuka, ukukhulelwa lokukhuluma amazwi amanga aphuma enhliziyweni.
14 Motero kuweruza kolungama kwalekeka ndipo choonadi chili kutali ndi ife; kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu, ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
Ngakho isahlulelo sibuyiselwa emuva, lokulunga kumi khatshana; ngoba iqiniso liyakhubeka esitaladeni, lobuqotho kabulakungena.
15 Choonadi sichikupezeka kumeneko, ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto. Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa kuti panalibe chiweruzo cholungama.
Yebo, iqiniso liyasilela, lowehlukana lobubi uzenza impango. INkosi yasikubona, njalo kwaba kubi emehlweni ayo ukuthi kakulasahlulelo.
16 Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe, Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera; Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza, ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
Yasibona ukuthi kwakungelamuntu, yamangala kakhulu ukuthi kwakungelamlamuli; ngakho ingalo yayo yaletha usindiso kuye, lokulunga kwayo khona kwamsekela.
17 Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa, ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso; anavala kulipsira ngati chovala ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
Ngoba yembatha ukulunga njengebhatshi lensimbi, lengowane yosindiso ekhanda layo; yembatha izembatho zempindiselo njengesembatho, yazembesa ukutshiseka njengejazi.
18 Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake molingana ndi zimene anachita, adzaonetsa ukali kwa adani ake ndi kubwezera chilango odana naye. Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
Njengokwezenzo, ngokunjalo izaphindisela, ulaka kwabamelana layo, umvuzo ezitheni zayo; ezihlengeni uzabuyisela umvuzo.
19 Choncho akadzabwera ngati madzi oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho. Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
Ngokunjalo bazalesaba ibizo leNkosi kusukela entshonalanga, lodumo lwayo kusukela lapho okuphuma khona ilanga. Lapho isitha sizangena njengomfula, uMoya weNkosi uzaphakamisa isiboniso esimelene laso.
20 “Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,” akutero Yehova.
LoMhlengi uzafika eZiyoni, lakulabo abaphenduka eziphambekweni koJakobe, itsho iNkosi.
21 Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,” akutero Yehova.
Mina-ke, lesi yisivumelwano sami labo, itsho iNkosi: UMoya wami ophezu kwakho, lamazwi ami engiwafake emlonyeni wakho, kawayikusuka emlonyeni wakho, lemlonyeni wenzalo yakho, lemlonyeni wenzalo yenzalo yakho, itsho iNkosi, kusukela khathesi kuze kube phakade.

< Yesaya 59 >