< Yesaya 59 >
1 Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa, kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
Look, Yahweh's hand is not so short that it cannot save; nor his ear so dull, that it cannot hear.
2 Koma zoyipa zanu zakulekanitsani ndi Mulungu wanu; ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu, kotero Iye sadzamva.
Your sinful acts, however, have separated you from your God, and your sins have made him hide his face from you and from hearing you.
3 Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi. Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu. Pakamwa panu payankhula zabodza, ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
For your hands are stained with blood and your fingers with sin. Your lips speak lies and your tongue speaks maliciously.
4 Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama, palibe amene akupita ku mlandu moona mtima. Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza; amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
No one calls in righteousness, and none pleads his case in truth. They trust in empty words, and tell lies; they conceive trouble and give birth to sin.
5 Iwo amayikira mazira a mamba ndipo amaluka ukonde wakangawude. Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa, ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
They hatch eggs of a poisonous snake and weave a spider's web. Whoever eats of their eggs dies, and if an egg is crushed, it hatches into a poisonous snake.
6 Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala; ndipo chimene apangacho sangachifunde. Ntchito zawo ndi zoyipa, ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
Their webs cannot be used for garments, nor can they cover themselves with their works. Their works are works of sin, and deeds of violence are in their hands.
7 Amathamangira kukachita zoyipa; sachedwa kupha anthu osalakwa. Maganizo awo ndi maganizo oyipa; kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
Their feet run to evil, and they run to pour out innocent blood. Their thoughts are thoughts of sin; violence and destruction are their roads.
8 Iwo sadziwa kuchita za mtendere; zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo. Njira zawo zonse nʼzokhotakhota; aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
The way of peace they do not know, and there is no justice in their paths. They have made crooked paths; whoever travels these paths does not know peace.
9 Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira; ndipo chipulumutso sichitifikira. Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha; tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
Therefore justice is far from us, nor does righteousness reach us. We wait for light, but see darkness; we look for brightness, but we walk in darkness.
10 Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona, kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso. Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku; timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
We grope for the wall like the blind, like those who cannot see. We stumble at noonday as in the twilight; among the strong we are like dead men.
11 Tonse timabangula ngati zimbalangondo: Timalira modandaula ngati nkhunda. Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza. Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
We growl like bears and moan like doves; we wait for justice, but there is none; for rescue, but it is far from us.
12 Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu, ndipo machimo athu akutsutsana nafe. Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse ndipo tikuvomereza machimo athu:
For our many transgressions are before you, and our sins testify against us; for our transgressions are with us, and we know our sins.
13 Tawukira ndi kumukana Yehova. Tafulatira Mulungu wathu, pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova, ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
We have rebelled, denying Yahweh and turning away from following our God. We have spoken extortion and turning aside, conceived complaining from the heart and words of lying.
14 Motero kuweruza kolungama kwalekeka ndipo choonadi chili kutali ndi ife; kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu, ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
Justice is driven back, and righteousness stands far off; for truth stumbles in the public square, and right cannot come.
15 Choonadi sichikupezeka kumeneko, ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto. Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa kuti panalibe chiweruzo cholungama.
Trustworthiness has gone away, and he who turns away from evil makes himself a victim. Yahweh saw it and was displeased that there was no justice.
16 Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe, Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera; Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza, ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
He saw that there was no man, and wondered that there was no one to intervene. Therefore his own arm brought salvation for him, and his righteousness sustained him.
17 Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa, ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso; anavala kulipsira ngati chovala ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
He put on righteousness as a breastplate and a helmet of salvation upon his head. He clothed himself with garments of vengeance and wore zeal as a mantle.
18 Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake molingana ndi zimene anachita, adzaonetsa ukali kwa adani ake ndi kubwezera chilango odana naye. Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
He repaid them for what they had done, angry judgment to his adversaries, vengeance to his enemies, to the islands punishment as their reward.
19 Choncho akadzabwera ngati madzi oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho. Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
So they will fear the name of Yahweh from the west, and his glory from the sun's rising; for he will come as a rushing stream, driven by the breath of Yahweh.
20 “Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,” akutero Yehova.
“A redeemer will come to Zion and to those who turn from their rebellious deeds in Jacob—this is Yahweh's declaration.
21 Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,” akutero Yehova.
As for me, this is my covenant with them—says Yahweh—my spirit who is upon you, and my words which I have put in your mouth, will not leave your mouth, or go out of the mouth of your children, or go out of the mouth of your children's children—says Yahweh—from this time and forever.”