< Yesaya 59 >

1 Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa, kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
Adiera bad Jehova Nyasaye ok chiek ma ok dores joge, bende ite ok odino ma ok dowinj wach.
2 Koma zoyipa zanu zakulekanitsani ndi Mulungu wanu; ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu, kotero Iye sadzamva.
To richou ema osepogou gi Nyasachu; richou ema omiyo osepandonu wangʼe mondo kik owinju.
3 Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi. Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu. Pakamwa panu payankhula zabodza, ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
Nimar lwetu otimo remo, kendo usemulo richo. Dhou osewacho miriambo kendo leu osehulo gik mamono.
4 Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama, palibe amene akupita ku mlandu moona mtima. Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza; amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
Onge ngʼama dwaro tim makare; kata manyo bura miyalo gadiera. Gigeno mana kuom weche manono kendo giwacho miriambo, gimako ich mar chandruok kendo ginywolo mana richo.
5 Iwo amayikira mazira a mamba ndipo amaluka ukonde wakangawude. Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa, ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
Gibutno e tong thuonde, kendo gichweyo mbuyi mar otiengʼ-otiengʼ. Ngʼato angʼata mochamo tongʼ-gi biro tho kendo kamoro oto to nyathi fu ema wuokie.
6 Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala; ndipo chimene apangacho sangachifunde. Ntchito zawo ndi zoyipa, ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
Mbui margi ok nyal twangʼ-go nanga, bende ok ginyal umore giwegi gi gik ma giloso. Timbegi gin timbe richo; kendo timbe mag mahundu ni e lwetgi.
7 Amathamangira kukachita zoyipa; sachedwa kupha anthu osalakwa. Maganizo awo ndi maganizo oyipa; kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
Tiendegi reto kadhi timo richo; giyot ahinya mondo gichwer remo maonge ketho. Paro manie chunygi gin paro maricho kendo kamoro amora ma gidhiyoe; masira gi chandruok ema dongʼie.
8 Iwo sadziwa kuchita za mtendere; zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo. Njira zawo zonse nʼzokhotakhota; aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
Ok gingʼeyo yo makelo kwe, onge tim makare e yoregi. Giseloko yorego obedo yore mogondore ogondore, kendo ngʼato angʼata mawuotho e yorego ok noyud kwe.
9 Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira; ndipo chipulumutso sichitifikira. Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha; tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
Omiyo ngʼado bura makare koro bor kodwa, kendo tim makare ok chop irwa. Wagombo ler, to mudho ema waneno; kendo wadwaro mondo piny oru, to mudho mandiwa ema wawuothoe.
10 Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona, kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso. Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku; timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
Wamulo kor udi mana ka muofni, kendo wamulo kuonde ma wawuothe, mana ka joma onge wengegi. Wachwanyore godiechiengʼ, mana ka gima en otieno kendo wachalo joma otho e kind joma rateke.
11 Tonse timabangula ngati zimbalangondo: Timalira modandaula ngati nkhunda. Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza. Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
Walak mana ka ondiegi kendo wadengo malit mana ka akuru. Wadwaro ngʼado bura makare to ok wayud kata achiel, kendo wamanyo ngʼama reswa to obor kodwa.
12 Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu, ndipo machimo athu akutsutsana nafe. Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse ndipo tikuvomereza machimo athu:
Nimar timbewa mamono opongʼo wangʼi kendo richowa elore e lela. Timbewa marichogo osiko kodwa kendo wayie timbewa mamonogo, ma gin:
13 Tawukira ndi kumukana Yehova. Tafulatira Mulungu wathu, pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova, ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
ngʼanyo kendo ketho e nyim Jehova Nyasaye, loko ngʼewa ne Nyasachwa, chano timo tulo kendo paro weche mag miriambo ka chunywa opongʼ kod wuond.
14 Motero kuweruza kolungama kwalekeka ndipo choonadi chili kutali ndi ife; kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu, ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
Omiyo ngʼado bura makare ogol oko kendo tim makare ni mabor kodwa, adiera onge e yore matindo kendo tim makare ni kuma bor.
15 Choonadi sichikupezeka kumeneko, ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto. Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa kuti panalibe chiweruzo cholungama.
Adiera ok nyal yudi, kendo ngʼat motangʼ ne richo chuny ji ojokgo. Jehova Nyasaye norangogi kendo nokecho nikech ngʼado bura makare onge kuomgi.
16 Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe, Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera; Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza, ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
Ne oneno kaonge ngʼato kata achiel, kendo nobwok ni onge kata ngʼato madikony; omiyo bade owuon nokelone en owuon warruok kendo timne makare ema norite.
17 Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa, ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso; anavala kulipsira ngati chovala ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
Norwakore tim makare ka law akor mar nyinyo, kendo ne orwako warruok ka ogut lweny; bende ne orwako chulo kuor ka ngʼama rwako law, kendo nobolo mirima mager kuome ka law abola.
18 Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake molingana ndi zimene anachita, adzaonetsa ukali kwa adani ake ndi kubwezera chilango odana naye. Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
Obiro chulo ngʼato ka ngʼato mana moromore gi timbene, obiro kumo wasike duto gi mirima mager kendo obiro kumo joma odakie dho nembe.
19 Choncho akadzabwera ngati madzi oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho. Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
Koa yo podho chiengʼ, ji noluor nying Jehova Nyasaye, kendo koa yo wuok chiengʼ, oganda nomiye duongʼ. Nimar nobi ka pi mongingore ma much Jehova Nyasaye osekudho.
20 “Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,” akutero Yehova.
Jehova Nyasaye wacho niya, “Jalno makelo Resruok nobi Sayun, mondo ores nyikwa Jakobo moseweyo richogi.”
21 Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,” akutero Yehova.
Jehova Nyasaye wacho niya, “Akwongʼora ni ma e singruokna kodgi. Roho mara man kuomu kod wechena ma aseketo e dhou nosik kodu chakre kawuono nyaka tiengʼ mabiro bangʼu koa kuom nyikwau kadhi nyaka kuom nyithindgi, wach ok nowuogi e dhog-gi ndalo duto nyaka chiengʼ,” Jehova Nyasaye ema owacho.

< Yesaya 59 >