< Yesaya 59 >
1 Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa, kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
Aj, neníť ukrácena ruka Hospodinova, aby nemohla zachovati, aniž jest obtíženo ucho jeho, aby nemohlo slyšeti.
2 Koma zoyipa zanu zakulekanitsani ndi Mulungu wanu; ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu, kotero Iye sadzamva.
Ale nepravosti vaše rozloučily vás s Bohem vaším, a hříchové vaši to způsobili, že skryl tvář před vámi, aby neslyšel.
3 Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi. Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu. Pakamwa panu payankhula zabodza, ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
Nebo ruce vaše jsou poškvrněné krví, a prstové vaši nepravostí; rtové vaši mluví lež, jazyk váš vynáší převrácenost.
4 Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama, palibe amene akupita ku mlandu moona mtima. Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza; amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
Není žádného, ješto by se zasadil o spravedlnost, aniž jest kdo, ješto by zastával pravdy. Doufají v marnost, a mluví daremné věci; počínají nátisk, a rodí nepravost.
5 Iwo amayikira mazira a mamba ndipo amaluka ukonde wakangawude. Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa, ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
Vejce bazališková vyseděli, a plátna pavoukového natkali. Kdož by jedl vejce jejich, umře; pakli je roztlačí, vynikne ještěrka.
6 Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala; ndipo chimene apangacho sangachifunde. Ntchito zawo ndi zoyipa, ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
Plátna jejich nehodí se na roucho, aniž se odějí dílem svým; skutkové jejich skutkové nepravosti, a dílo ukrutnosti jest v rukou jejich.
7 Amathamangira kukachita zoyipa; sachedwa kupha anthu osalakwa. Maganizo awo ndi maganizo oyipa; kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
Nohy jejich k zlému běží, a pospíchají k vylévání krve nevinné. Myšlení jejich jsou myšlení nepravá, zpuštění a setření jest na cestách jejich.
8 Iwo sadziwa kuchita za mtendere; zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo. Njira zawo zonse nʼzokhotakhota; aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
Cesty pokoje neznají, a není žádné spravedlnosti v šlepějích jejich. Stezky své převracejí tajně; kdožkoli po nich chodí, nemívá pokoje.
9 Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira; ndipo chipulumutso sichitifikira. Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha; tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
Protož vzdálil se od nás soud, a nedochází nás spravedlnost. Èekáme-li na světlo, aj, tma, pakli na blesk, v mrákotách chodíme.
10 Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona, kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso. Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku; timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
Makáme jako slepí stěnu, a jako bychom žádných očí neměli, šámáme. Urážíme se o poledni jako v soumrak, u veliké hojnosti podobni jsme mrtvým.
11 Tonse timabangula ngati zimbalangondo: Timalira modandaula ngati nkhunda. Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza. Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
Mumleme všickni my jako nedvědi, a jako holubice ustavičně lkáme. Očekáváme na soud, ale není ho, na vysvobození, ale daleké jest od nás.
12 Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu, ndipo machimo athu akutsutsana nafe. Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse ndipo tikuvomereza machimo athu:
Nebo rozmnožena jsou přestoupení naše před tebou, a hříchové naši svědčí proti nám, poněvadž přestoupení naše jsou při nás, i nepravosti naše. Známeť to,
13 Tawukira ndi kumukana Yehova. Tafulatira Mulungu wathu, pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova, ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
Že jsme se zpronevěřili, a lhali Hospodinu, a odvrátili se od následování Boha svého, že jsme mluvili o nátisku a odvrácení, že jsme ukládali a vynášeli z srdce slova lživá,
14 Motero kuweruza kolungama kwalekeka ndipo choonadi chili kutali ndi ife; kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu, ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
Tak že odvrácen jest nazpět soud, a spravedlnost zdaleka stojí; nebo klesla na ulici pravda, a pravost nemá průchodu.
15 Choonadi sichikupezeka kumeneko, ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto. Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa kuti panalibe chiweruzo cholungama.
Nýbrž zhynula pravda, a ten, kdož se uchyluje od zlého, loupeži bývá vydán; což vidí Hospodin, a nelíbí se to jemu, že není žádného soudu.
16 Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe, Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera; Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza, ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
Když tedy viděl, že není žádného muže, až se užasl, že není žádného prostředníka. A protož vysvobození jemu způsobilo rámě jeho, a spravedlnost jeho sama jej zpodepřela.
17 Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa, ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso; anavala kulipsira ngati chovala ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
Nebo oblékl spravedlnost jako pancíř, a lebka spasení na hlavě jeho. Oblékl se v roucho pomsty jako v sukni, a oděl se horlivostí jako pláštěm,
18 Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake molingana ndi zimene anachita, adzaonetsa ukali kwa adani ake ndi kubwezera chilango odana naye. Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
Aby podlé skutků, aby podlé nich odplacel prchlivostí protivníkům svým, odměnu nepřátelům svým, i ostrovům odplatu aby dával.
19 Choncho akadzabwera ngati madzi oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho. Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
I budou se báti na západ jména Hospodinova, a na východu slunce slávy jeho, když se přivalí jako řeka nepřítel, jejž duch Hospodinův preč zažene.
20 “Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,” akutero Yehova.
Neboť přijde k Sionu vykupitel, a k těm, kteříž se odvracují od přestoupení v Jákobovi, praví Hospodin.
21 Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,” akutero Yehova.
Tatoť pak bude smlouva má s nimi, praví Hospodin: Duch můj, kterýž jest v tobě, a slova má, kteráž jsem vložil v ústa tvá, neodejdouť od úst tvých, ani od úst semene tvého, ani od úst potomků semene tvého, praví Hospodin, od tohoto času až na věky.