< Yesaya 58 >

1 “Fuwula kwambiri, usaleke. Mawu ako amveke ngati lipenga. Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo; uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.
Вичи из грла, не устежи се, подигни глас свој као труба, и објави народу мом безакоња његова и дому Јаковљевом грехе њихове,
2 Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine; amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna, kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake. Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.
Премда ме сваки дан траже и ради су знати путеве моје, као народ који твори правду и не оставља суд Бога свог; ишту од мене судове праведне, желе приближити се к Богу.
3 Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala kudya pamene Inu simukulabadirapo? Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa pamene Inu simunasamalepo?’” Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani, ndipo mumazunza antchito anu onse.
Зашто постисмо, веле, а Ти не погледа, мучисмо душе своје, а Ти не хте знати? Гле, кад постите, чините своју вољу и изгоните све шта вам је ко дужан.
4 Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana, mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka. Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.
Ето постите да се прете и свађате и да бијете песницом безбожно. Немојте постити тако као данас, да би се чуо горе глас ваш.
5 Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku, kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi? Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo? Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko, tsiku lokondweretsa Yehova?
Такав ли је пост који изабрах да човек мучи душу своју један дан? Да савија главу своју као сита и да стере пода се кострет и пепео? То ли ћеш звати пост и дан угодан Господу?
6 “Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna: Kumasula maunyolo ozunzizira anthu ndi kumasula zingwe za goli, kupereka ufulu kwa oponderezedwa ndi kuphwanya goli lililonse?
А није ли ово пост што изабрах: да развежеш свезе безбожности, да разрешиш ремење од бремена, да отпустиш потлачене, и да изломите сваки јарам?
7 Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu? Osowa ndi ongoyendayenda, kodi mwawapatsa malo ogona? Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?
Није ли да преламаш хлеб свој гладноме, и сиромахе прогнане да уведеш у кућу? Кад видиш голог, да га оденеш, и да се не кријеш од свог тела?
8 Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha, ndipo mabala anu adzachira msangamsanga; chilungamo chanu chidzakutsogolerani ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.
Тада ће синути видело твоје као зора, и здравље ће твоје брзо процвасти, и пред тобом ће ићи правда твоја, слава Господња биће ти задња стража.
9 Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani; mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano. “Ngati muleka kuzunza anzanu, ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.
Тада ћеш призивати, и Господ ће те чути; викаћеш, и рећи ће: Ево ме. Ако избациш између себе јарам и престанеш пружати прст и говорити зло;
10 Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala, ndi kuthandiza anthu oponderezedwa, pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima, ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.
И ако отвориш душу своју гладноме, и наситиш душу невољну; тада ће засјати у мраку видело твоје и тама ће твоја бити као подне.
11 Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse; adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa ndipo adzalimbitsa matupi anu. Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri, ngati kasupe amene madzi ake saphwa.
Јер ће те Господ водити вазда, и ситиће душу твоју на суши, и кости твоје крепиће, и бићеш као врт заливен и као извор коме вода не пресише.
12 Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali, ndipo adzamanganso pa maziko akalekale; inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka. Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.
И твоји ће сазидати старе пустолине, и подигнућеш темеље који ће стајати од колена до колена, и прозваћеш се: Који сазида развалине и оправи путеве за насеље.
13 “Muzisunga osaphwanya Sabata; musamachite zimene mukufuna pa masiku anga opatulika, tsiku la Sabata lizikhala tsiku lachisangalalo. Tsiku lopatulika la Yehova muzililemekeza posayenda mʼnjira zanu, kapena kuchita zimene mukufuna ndi kuyankhula zopandapake,
Ако одвратиш ногу своју од суботе да не чиниш шта је теби драго на мој свети дан, и ако прозовеш суботу милином, свети дан Господњи славним, и будеш га славио не идући својим путевима и не чинећи шта је теби драго, ни говорећи речи,
14 mukatero mudzapeza chimwemwe mwa Yehova, ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi. Mudzadyerera dziko limene ndinapatsa Yakobo kholo lanu.” Yehova wayankhula ndi pakamwa pake.
Тада ћеш се веселити у Господу, и извешћу те на висине земаљске, и даћу ти да једеш наследство Јакова оца свог; јер уста Господња рекоше.

< Yesaya 58 >