< Yesaya 58 >

1 “Fuwula kwambiri, usaleke. Mawu ako amveke ngati lipenga. Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo; uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.
آواز خود را بلند کن و دریغ مدار و آوازخود را مثل کرنا بلند کرده، به قوم من تقصیر ایشان را و به خاندان یعقوب گناهان ایشان را اعلام نما.۱
2 Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine; amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna, kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake. Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.
و ایشان هر روز مرا می‌طلبند و ازدانستن طریق های من مسرور می‌باشند. مثل امتی که عدالت را بجا آورده، حکم خدای خود را ترک ننمودند. احکام عدالت را از من سوال نموده، ازتقرب جستن به خدا مسرور می‌شوند۲
3 Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala kudya pamene Inu simukulabadirapo? Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa pamene Inu simunasamalepo?’” Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani, ndipo mumazunza antchito anu onse.
(ومی گویند): چرا روزه داشتیم و ندیدی و جانهای خویش را رنجانیدیم و ندانستی. اینک شما درروز روزه خویش خوشی خود را می‌یابید و برعمله های خود ظلم می‌نمایید.۳
4 Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana, mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka. Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.
اینک به جهت نزاع و مخاصمه روزه می‌گیرید و به لطمه شرارت می‌زنید. «امروز روزه نمی گیرید که آواز خود رادر اعلی علیین بشنوانید.۴
5 Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku, kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi? Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo? Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko, tsiku lokondweretsa Yehova?
آیا روزه‌ای که من می‌پسندم مثل این است، روزی که آدمی جان خود را برنجاند و سر خود را مثل نی خم ساخته، پلاس و خاکستر زیر خود بگستراند؟ آیا این راروزه و روز مقبول خداوند می‌خوانی؟۵
6 “Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna: Kumasula maunyolo ozunzizira anthu ndi kumasula zingwe za goli, kupereka ufulu kwa oponderezedwa ndi kuphwanya goli lililonse?
«مگر روزه‌ای که من می‌پسندم این نیست که بندهای شرارت را بگشایید و گره های یوغ را بازکنید و مظلومان را آزاد سازید و هر یوغ رابشکنید؟۶
7 Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu? Osowa ndi ongoyendayenda, kodi mwawapatsa malo ogona? Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?
مگر این نیست که نان خود را به گرسنگان تقسیم نمایی و فقیران رانده شده را به خانه خود بیاوری و چون برهنه را ببینی او رابپوشانی و خود را از آنانی که از گوشت تومی باشند مخفی نسازی؟۷
8 Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha, ndipo mabala anu adzachira msangamsanga; chilungamo chanu chidzakutsogolerani ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.
آنگاه نور تو مثل فجرطالع خواهد شد و صحت تو بزودی خواهدرویید و عدالت تو پیش تو خواهد خرامید وجلال خداوند ساقه تو خواهد بود.۸
9 Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani; mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano. “Ngati muleka kuzunza anzanu, ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.
آنگاه دعاخواهی کرد و خداوند تو را اجابت خواهد فرمودو استغاثه خواهی نمود و او خواهد گفت که اینک حاضر هستم. اگر یوغ و اشاره کردن به انگشت وگفتن ناحق را از میان خود دور کنی،۹
10 Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala, ndi kuthandiza anthu oponderezedwa, pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima, ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.
و آرزوی جان خود را به گرسنگان ببخشی و جان ذلیلان راسیر کنی، آنگاه نور تو در تاریکی خواهددرخشید و تاریکی غلیظ تو مثل ظهر خواهد بود.۱۰
11 Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse; adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa ndipo adzalimbitsa matupi anu. Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri, ngati kasupe amene madzi ake saphwa.
و خداوند تو را همیشه هدایت نموده، جان تورا در مکان های خشک سیر خواهد کرد واستخوانهایت را قوی خواهد ساخت و تو مثل باغ سیرآب و مانند چشمه آب که آبش کم نشودخواهی بود.۱۱
12 Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali, ndipo adzamanganso pa maziko akalekale; inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka. Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.
و کسان تو خرابه های قدیم را بناخواهند نمود و تو اساسهای دوره های بسیار رابرپا خواهی داشت و تو را عمارت کننده رخنه هاو مرمت کننده کوچه‌ها برای سکونت خواهندخواند.۱۲
13 “Muzisunga osaphwanya Sabata; musamachite zimene mukufuna pa masiku anga opatulika, tsiku la Sabata lizikhala tsiku lachisangalalo. Tsiku lopatulika la Yehova muzililemekeza posayenda mʼnjira zanu, kapena kuchita zimene mukufuna ndi kuyankhula zopandapake,
«اگر پای خود را از سبت نگاه داری وخوشی خود را در روز مقدس من بجا نیاوری وسبت را خوشی و مقدس خداوند و محترم بخوانی و آن را محترم داشته، به راههای خودرفتار ننمایی و خوشی خود را نجویی و سخنان خود را نگویی،۱۳
14 mukatero mudzapeza chimwemwe mwa Yehova, ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi. Mudzadyerera dziko limene ndinapatsa Yakobo kholo lanu.” Yehova wayankhula ndi pakamwa pake.
آنگاه در خداوند متلذذخواهی شد و تو را بر مکان های بلند زمین سوارخواهم کرد. و نصیب پدرت یعقوب را به توخواهم خورانید» زیرا که دهان خداوند این راگفته است.۱۴

< Yesaya 58 >