< Yesaya 58 >
1 “Fuwula kwambiri, usaleke. Mawu ako amveke ngati lipenga. Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo; uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.
« Criez à haute voix! N'épargnez pas! Élevez votre voix comme une trompette! Déclarez à mon peuple sa désobéissance, et à la maison de Jacob leurs péchés.
2 Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine; amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna, kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake. Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.
Mais ils me cherchent chaque jour, et se réjouissent de connaître mes voies. Comme une nation qui a fait le bien, et n'ont pas abandonné l'ordonnance de leur Dieu, ils me demandent des jugements justes. Ils se plaisent à s'approcher de Dieu.
3 Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala kudya pamene Inu simukulabadirapo? Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa pamene Inu simunasamalepo?’” Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani, ndipo mumazunza antchito anu onse.
Pourquoi avons-nous jeûné, disent-ils, et ne voyez-vous pas? Pourquoi avons-nous affligé notre âme, et vous ne vous en apercevez pas? ». « Voici qu'au jour de ton jeûne tu trouves du plaisir, et opprimez tous vos ouvriers.
4 Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana, mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka. Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.
Voici, vous jeûnez pour des querelles et des disputes, et de frapper avec le poing de la méchanceté. Vous ne jeûnez pas aujourd'hui pour faire entendre votre voix en haut lieu.
5 Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku, kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi? Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo? Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko, tsiku lokondweretsa Yehova?
Est-ce le jeûne que j'ai choisi? Un jour où un homme doit humilier son âme? Est-ce de baisser sa tête comme un roseau, et de se couvrir de sacs et de cendres? Vous appelez ça un jeûne, et un jour agréable pour Yahvé?
6 “Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna: Kumasula maunyolo ozunzizira anthu ndi kumasula zingwe za goli, kupereka ufulu kwa oponderezedwa ndi kuphwanya goli lililonse?
« N'est-ce pas là le jeûne que j'ai choisi: pour libérer les liens de la méchanceté, pour défaire les sangles de l'étrier, pour laisser les opprimés libres, et que vous brisez tout joug?
7 Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu? Osowa ndi ongoyendayenda, kodi mwawapatsa malo ogona? Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?
N'est-ce pas distribuer son pain à celui qui a faim, et que tu amènes les pauvres qui sont chassés dans ta maison? Quand tu vois le nu, que tu le couvres; et que tu ne te caches pas de ta propre chair?
8 Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha, ndipo mabala anu adzachira msangamsanga; chilungamo chanu chidzakutsogolerani ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.
Alors ta lumière éclatera comme l'aurore, et votre guérison apparaîtra rapidement; alors ta justice marchera devant toi, et la gloire de Yahvé sera votre arrière-garde.
9 Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani; mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano. “Ngati muleka kuzunza anzanu, ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.
Alors tu appelleras, et Yahvé répondra. Tu crieras à l'aide, et il dira: « Je suis là. « Si vous enlevez du milieu de vous le joug, le fait de pointer du doigt, et de parler méchamment;
10 Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala, ndi kuthandiza anthu oponderezedwa, pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima, ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.
et si vous répandez votre âme à ceux qui ont faim, et satisfaire l'âme affligée, alors ta lumière se lèvera dans les ténèbres, et ton obscurité sera comme le jour de midi;
11 Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse; adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa ndipo adzalimbitsa matupi anu. Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri, ngati kasupe amene madzi ake saphwa.
et Yahvé te guidera sans cesse, satisfaire votre âme dans les lieux arides, et rendre vos os forts. Vous serez comme un jardin arrosé, et comme une source d'eau dont les eaux ne faiblissent pas.
12 Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali, ndipo adzamanganso pa maziko akalekale; inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka. Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.
Ceux qui seront de vous rebâtiront les anciennes ruines. Tu relèveras les fondations de nombreuses générations. Tu seras appelé Réparateur de la Brèche, Restaurateur de chemins avec des habitations.
13 “Muzisunga osaphwanya Sabata; musamachite zimene mukufuna pa masiku anga opatulika, tsiku la Sabata lizikhala tsiku lachisangalalo. Tsiku lopatulika la Yehova muzililemekeza posayenda mʼnjira zanu, kapena kuchita zimene mukufuna ndi kuyankhula zopandapake,
« Si tu détournes ton pied du sabbat, de faire ton plaisir le jour de ma fête, et appeler le sabbat un délice, et le saint de Yahvé, honorable, et l'honorer, de ne pas faire à ta façon, ni de trouver son propre plaisir, ni de parler avec vos propres mots,
14 mukatero mudzapeza chimwemwe mwa Yehova, ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi. Mudzadyerera dziko limene ndinapatsa Yakobo kholo lanu.” Yehova wayankhula ndi pakamwa pake.
alors tu feras tes délices de Yahvé, et je vous ferai monter sur les hauteurs de la terre, et je te nourrirai de l'héritage de Jacob, ton père ». car la bouche de Yahvé l'a dit.