< Yesaya 57 >

1 Anthu olungama amafa, ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake; anthu odzipereka amatengedwa, ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake. Anthu olungama amatengedwa kuti tsoka lisawagwere.
Mapukaw ti nalinteg, ngem awan ti mangikaskaso iti daytoy, ken naipanaw met dagiti tattao ti tulag iti kinapudno, ngem awan ti makaawat a naipanaw dagiti nalinteg manipud iti dakes.
2 Iwo amene amakhala moyo wolungama amafa mwamtendere; amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.
Sumrek isuna iti talna; aginanada kadagiti pagiddaanda, dagiti magna iti kinalintegda.
3 “Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa, inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
Ngem umasidegkayo, dakayo nga annak dagiti manggagamud, annak dagiti mannakikamalala ken ti babai a balangkantis.
4 Kodi inu mukuseka yani? Kodi mukumunena ndani ndi kupotoza pakamwa panu? Kodi inu si ana owukira, zidzukulu za anthu abodza?
Siasino ti lalaisenyo a siraragsak? Siasino ti pangingangangaanyo iti ngiwat ken guyguyabanyo? Saan kadi nga annakdakayo ti panaglabsing, annak ti panangallilaw?
5 Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu, ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri. Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
Pappapudutennyo dagiti bagiyo iti pannakikakaidda iti sirok dagiti lugo, iti sirok ti tunggal nalangto a kayo, dakayo a mangpappapatay kadagiti annakyo iti namaga a karayan, iti sirok dagiti rengngat ti bato.
6 Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu. Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo, ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya. Kodi zimenezi zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
Kadagiti nalamuyot a banbanag iti igid ti karayan ket dagiti banbanag a naited kadakayo. Dagitoy dagiti banbanag a daydayawenyo. Manggibukbukbokkayo iti daton a mainum kadagitoy ken mangitagtag-aykayo iti datonyo a bukel. Kadagitoy a banbanag kadi ti pakaragsakak?
7 Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali. Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
Insaganam ti pagiddaam iti tapaw ti nangato a bantay; simmang-atka pay sadiay tapno mangidaton kadagiti sagut.
8 Mʼnyumba mwanu mwayika mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu. Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu. Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu, ndiye mwazilipira kuti mugone nazo. Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
Iti likudan ti ruangan ken ad-adigi nangikabilka kadagiti pagilasinan; tinallikudannak, naglabuska ket kimmalay-atka; pinalawam ti pagiddaam. Nakitulagka kadakuada; impategmo dagiti pagiddaanda; nakitam dagiti mabagbagida.
9 Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta ndi zonunkhira zochuluka. Munachita kutumiza akazembe anu kutali; inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko! (Sheol h7585)
Napanka iti ari nga addaan iti lana; pinaadom dagiti bangbanglo. Imbaonmo dagiti babaonem iti adayo; bimmabaka iti lubong dagiti natay. (Sheol h7585)
10 Inu mumatopa ndi maulendo anu, koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’ Munapezako kumeneko zokhumba zanu nʼchifukwa chake simunalefuke.
Nabannogka iti adayo a panagdaliasatmo, ngem pulos a saanmo a kinuna, “Awan namnamana.” Nakasarakka iti biag kadagiti imam; ngarud saanka a kimmapoy.
11 “Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa, kotero kuti mwakhala mukundinamiza, ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe, kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine? Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti ndakhala chete nthawi yayitali?
“Siasino ti pagdandanagam? Siasino ti pagbutbutngam iti kasta unay a namagtignay kenka iti inaallilaw, iti kasta unay ket saannakon a malagip wenno mapanunot? Gapu ta naulimekak iti nabayag, saankan nga agbutbuteng kaniak.
12 Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama, ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
Ipakaammok dagiti amin a nalinteg nga aramidmo ken ibagak dagiti amin nga inaramidmo, ngem saandakanto a matulungan.
13 Pamene mufuwula kupempha thandizo, mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni! Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo, mpweya chabe udzawulutsa mafanowo. Koma munthu amene amadalira ine adzalandira dziko lokhalamo. Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”
Inton umasugka, ispalennaka koma ngarud dagiti inurnongmo a didiosen. Ngem ketdi ipanaw ida amin ti angin, ipanaw ida amin ti maysa nga anges. Ngem ti agkamang kaniak ket tawidennanto ti daga ken tagikuaenanto ti nasantoan a bantayko.
14 Ndipo panamveka mawu akuti, “Undani, undani, konzani msewu! Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
Ibagananto, 'Mangaramid, mangaramid! Dalusanyo ti dalan! Ikkatenyo dagiti amin a pakaitibkulan dagiti tattaok!'''
15 Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse, amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo, akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika, koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
Ta kastoy ti kuna ti nangato ken Natan-ok, a sibibiag iti agnanayon, a nasantoan ti naganna, “Agnanaedak iti nangato ken nasantoan a lugar, kasta met kenkuana a napakumbaba ken mangak-aklon nga adda basolna, tapno isublik ti espiritu dagiti napakumbaba, ken tapno papigsaek ti puso dagiti agbabbabawi.
16 Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya kapena kuwapsera mtima nthawi zonse, popeza kuti ndinalenga anthu anga ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
Ta saanakto a mang-usig iti agnanayon, wenno agunget iti agnanayon, ta kumapoy ti espiritu ti tao iti sangoanak, dagiti biag a pinarsuak.
17 Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera; ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya, koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
Gapu iti basol iti kinaranggasna, nagungetak, ket dinusak isuna; inlingedko ti rupak ken nagungetak, ngem nagsubli isuna iti dalan ti pusona.
18 Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa; kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
Nakitak dagiti wagasna, ngem paimbagekto isuna. Idalanko isuna, liwliwaek ken patibkerek dagiti agladladingit gapu kenkuana,
19 anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo. Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,” “Ndipo ndidzawachiritsa.” Akutero Yehova.
ken parsuaek ti bunga dagiti bibig. Kappia, kappia kadagiti adda iti adayo ken kadagiti asideg—kuna ni Yahweh—Paimbagekto ida.
20 Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka, yosatha kukhala bata, mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
Ngem maiyarig dagiti nadangkes iti nadawel a baybay, a saan a mabalin nga aginana, ken mangipurpurruak dagiti danumna iti pitak.
21 “Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.
Awan talna para kadagiti nadangkes—kuna ti Dios.”

< Yesaya 57 >