< Yesaya 57 >
1 Anthu olungama amafa, ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake; anthu odzipereka amatengedwa, ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake. Anthu olungama amatengedwa kuti tsoka lisawagwere.
The righteous perish, but no one considers it, and the people of covenant faithfulness are gathered away, but no one understands that the righteous is gathered away from the evil.
2 Iwo amene amakhala moyo wolungama amafa mwamtendere; amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.
He enters into peace; they rest in their beds, those who walk in their uprightness.
3 “Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa, inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
But come here, you sons of the sorceress, children of the adulterer and the woman who has prostituted herself.
4 Kodi inu mukuseka yani? Kodi mukumunena ndani ndi kupotoza pakamwa panu? Kodi inu si ana owukira, zidzukulu za anthu abodza?
Whom are you merrily mocking? Against whom are you opening the mouth and sticking out the tongue? Are you not children of rebellion, children of deceit?
5 Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu, ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri. Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
You heat yourselves up sleeping together under the oaks, under every green tree, you who kill your children in the dry riverbeds, under the rocky overhangs.
6 Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu. Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo, ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya. Kodi zimenezi zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
Among the smooth things of the river valley are the things that have been assigned to you. They are the object of your devotion. You pour out your drink offering to them and raise up a grain offering. In these things should I take pleasure?
7 Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali. Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
You prepared your bed on a high mountain; you also went up there to offer sacrifices.
8 Mʼnyumba mwanu mwayika mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu. Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu. Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu, ndiye mwazilipira kuti mugone nazo. Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
Behind the door and the doorposts you set up your symbols; you deserted me, made yourselves naked, and went up; you made your bed wide. You made a covenant with them; you loved their beds; you saw their private parts.
9 Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta ndi zonunkhira zochuluka. Munachita kutumiza akazembe anu kutali; inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko! (Sheol )
You went to Molech with oil; you multiplied perfumes. You send your ambassadors far away; you went down to Sheol. (Sheol )
10 Inu mumatopa ndi maulendo anu, koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’ Munapezako kumeneko zokhumba zanu nʼchifukwa chake simunalefuke.
You were tired from your long journey, but you never said, “It is hopeless.” You found life in your hand; therefore you did not weaken.
11 “Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa, kotero kuti mwakhala mukundinamiza, ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe, kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine? Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti ndakhala chete nthawi yayitali?
“Whom are you worried about? Whom do you fear so much that has caused you to act so deceitfully, so much that you would not remember me or think about me? Because I was silent for so long, you are no longer afraid of me.
12 Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama, ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
I will proclaim all your righteous acts and tell all that you have done, but they will not help you.
13 Pamene mufuwula kupempha thandizo, mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni! Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo, mpweya chabe udzawulutsa mafanowo. Koma munthu amene amadalira ine adzalandira dziko lokhalamo. Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”
When you cry out, let your collection of idols rescue you. Instead the wind will carry them all away, a breath will carry them all away. Yet he who takes refuge in me will inherit the land and will take possession of my holy mountain.
14 Ndipo panamveka mawu akuti, “Undani, undani, konzani msewu! Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
He will say, 'Build, build! Clear a way! Remove all the stumbling blocks from the path of my people!'”
15 Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse, amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo, akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika, koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
For this is what the high and elevated One says, who lives eternally, whose name is holy, “I live in the exalted and holy place, with him also that is of a crushed and humble spirit, to revive the spirit of the humble ones, and to revive the heart of the contrite ones.
16 Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya kapena kuwapsera mtima nthawi zonse, popeza kuti ndinalenga anthu anga ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
For I will not accuse forever, nor will I be angry forever, for then man's spirit would faint before me, the lives that I have made.
17 Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera; ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya, koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
Because of the sin of his violent gain, I was angry, and I punished him; I hid my face and was angry, but he went backward in the way of his heart.
18 Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa; kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
I have seen his ways, but I will heal him. I will lead him and comfort and console those who mourn for him,
19 anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo. Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,” “Ndipo ndidzawachiritsa.” Akutero Yehova.
and I create the fruit of the lips. Peace, peace, to those who are far off and to those who are near—says Yahweh—I will heal them.
20 Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka, yosatha kukhala bata, mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
But the wicked are like the tossing sea, which cannot rest, and its waters churn up mire and mud.
21 “Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.
There is no peace for the wicked one—says God.”