< Yesaya 56 >

1 Yehova akuti, “Chitani chilungamo ndi zinthu zabwino, chifukwa chipulumutso changa chili pafupi ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
Овако вели Господ: Пазите на суд, и творите правду, јер ће скоро доћи спасење моје, и правда ће се моја објавити.
2 Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi, munthu amene amalimbika kuzichita, amene amasunga Sabata osaliyipitsa, ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”
Благо човеку који тако чини, и сину човечјем који се држи тога чувајући суботу да се не оскврни, чувајући руку своју да не учини зло.
3 Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti, “Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.” Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti, “Ine ndine mtengo wowuma basi.”
И нека не говори туђин који пристане уз Господа: Господ ме је одлучио од свог народа; и нека не говори ушкопљеник: Гле, ја сам суво дрво.
4 Popeza Yehova akuti, “Wofulidwa amene amasunga masabata anga, nachita zokomera Ine ndi kusunga pangano langa,
Јер овако вели Господ за ушкопљенике: Који држе суботе моје и избирају шта је мени угодно, и држе завет мој,
5 ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake, kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi. Ndidzawapatsa dzina labwino, losatha ndi losayiwalika.”
Њима ћу дати у дому свом и међу зидовима својим место и име боље него синова и кћери, име вечно даћу свакоме од њих, које се неће затрти.
6 Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova, motero kuti amamutumikira Iye, amakonda dzina la Yehova, amamugwirira ntchito, komanso kusunga Sabata osaliyipitsa ndi kusunga bwino pangano langa,
А туђине који пристану уз Господа да Му служе и да љубе име Господње, да Му буду слуге, који год држе суботу да је не оскврне и држе завет мој,
7 amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika, ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero. Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe. Paja nyumba yanga idzatchedwa nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
Њих ћу довести на свету гору своју и развеселићу их у дому свом молитвеном; жртве њихове паљенице и друге жртве биће угодне на олтару мом, јер ће се дом мој звати дом молитве свим народима.
8 Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti, “Ndidzasonkhanitsano anthu ena kuwonjezera amene anasonkhana kale.”
Господ Господ говори, који сабира прогнанике Израиљеве: Још ћу му сабрати осим оних који су сабрани.
9 Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo, inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
Све звери пољске, ходите да једете, све звери шумске.
10 Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu, onse ndi opanda nzeru; onse ndi agalu opanda mawu, samatha kuwuwa: amagona pansi nʼkumalota amakonda kugona tulo.
Сви су му стражари слепи, ништа не знају, сви су пси неми, не могу лајати, сањиви су, леже, мио им је дремеж.
11 Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu; sakhuta konse. Abusa nawonso samvetsa zinthu; onse amachita monga akufunira, aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
И пси су прождрљиви, који не знају за ситост; и пастири су који не знају за разум, сваки се окреће својим путем, сваки за својом коришћу са свог краја.
12 Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo! Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta! Mawa lidzakhala ngati leroli, kapena kuposa lero lino.”
Ходите, узећу вина и напићемо се силовитог пића, и сутра ће бити као данас, и још много више.

< Yesaya 56 >