< Yesaya 56 >

1 Yehova akuti, “Chitani chilungamo ndi zinthu zabwino, chifukwa chipulumutso changa chili pafupi ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
و خداوند چنین می‌گوید: «انصاف رانگاه داشته، عدالت را جاری نمایید، زیرا که آمدن نجات من و منکشف شدن عدالت من نزدیک است.۱
2 Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi, munthu amene amalimbika kuzichita, amene amasunga Sabata osaliyipitsa, ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”
خوشابحال انسانی که این را بجا آورد و بنی آدمی که به این متمسک گردد، که سبت را نگاه داشته، آن را بی‌حرمت نکند و دست خویش را از هر عمل بد باز‌دارد.»۲
3 Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti, “Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.” Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti, “Ine ndine mtengo wowuma basi.”
پس غریبی که با خداوند مقترن شده باشد تکلم نکند و نگویدکه خداوند مرا از قوم خود جدا نموده است وخصی هم نگوید که اینک من درخت خشک هستم.۳
4 Popeza Yehova akuti, “Wofulidwa amene amasunga masabata anga, nachita zokomera Ine ndi kusunga pangano langa,
زیرا خداوند درباره خصیهایی که سبت های مرا نگاه دارند و آنچه را که من خوش دارم اختیار نمایند و به عهد من متمسک گردند، چنین می‌گوید۴
5 ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake, kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi. Ndidzawapatsa dzina labwino, losatha ndi losayiwalika.”
که «به ایشان در خانه خود و دراندرون دیوارهای خویش یادگاری و اسمی بهتراز پسران و دختران خواهم داد. اسمی جاودانی که منقطع نخواهد شد به ایشان خواهم بخشید.۵
6 Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova, motero kuti amamutumikira Iye, amakonda dzina la Yehova, amamugwirira ntchito, komanso kusunga Sabata osaliyipitsa ndi kusunga bwino pangano langa,
و غریبانی که با خداوند مقترن شده، او راخدمت نمایند و اسم خداوند را دوست داشته، بنده او بشوند. یعنی همه کسانی که سبت را نگاه داشته، آن را بی‌حرمت نسازند و به عهد من متمسک شوند.۶
7 amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika, ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero. Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe. Paja nyumba yanga idzatchedwa nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
ایشان را به کوه قدس خودخواهم آورد و ایشان را در خانه عبادت خودشادمان خواهم ساخت و قربانی های سوختنی وذبایح ایشان بر مذبح من قبول خواهد شد، زیراخانه من به خانه عبادت برای تمامی قوم‌ها مسمی خواهد شد.»۷
8 Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti, “Ndidzasonkhanitsano anthu ena kuwonjezera amene anasonkhana kale.”
و خداوند یهوه که جمع کننده رانده شدگان اسرائیل است می‌گوید که «بعد از این دیگران را با ایشان جمع خواهم کرد علاوه برآنانی که از ایشان جمع شده‌اند.»۸
9 Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo, inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
‌ای تمام حیوانات صحرا و‌ای جمیع حیوانات جنگل بیایید و بخورید!۹
10 Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu, onse ndi opanda nzeru; onse ndi agalu opanda mawu, samatha kuwuwa: amagona pansi nʼkumalota amakonda kugona tulo.
دیده بانان اوکورند، جمیع ایشان معرفت ندارند و همگی ایشان سگان گنگ‌اند که نمی توانند بانگ کنند.۱۰
11 Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu; sakhuta konse. Abusa nawonso samvetsa zinthu; onse amachita monga akufunira, aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
و این سگان حریصند که نمی توانندسیر بشوند و ایشان شبانند که نمی توانندبفهمند. جمیع ایشان به راه خود میل کرده، هریکی بطرف خود طالب سود خویش می‌باشد.۱۱
12 Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo! Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta! Mawa lidzakhala ngati leroli, kapena kuposa lero lino.”
(و می‌گویند) بیایید شراب بیاوریم و ازمسکرات مست شویم و فردا مثل امروز روزعظیم بلکه بسیار زیاده خواهد بود.۱۲

< Yesaya 56 >