< Yesaya 56 >

1 Yehova akuti, “Chitani chilungamo ndi zinthu zabwino, chifukwa chipulumutso changa chili pafupi ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
The Lord seith these thingis, Kepe ye doom, and do ye riytfulnesse, for whi myn helthe is niy, that it come, and my riytfulnesse, that it be schewid.
2 Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi, munthu amene amalimbika kuzichita, amene amasunga Sabata osaliyipitsa, ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”
Blessid is the man, that doith this, and the sone of man, that schal take this; kepynge the sabat, that he defoule not it, kepynge hise hondis, that he do not ony yuel.
3 Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti, “Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.” Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti, “Ine ndine mtengo wowuma basi.”
And seie not the sone of a comelyng, that cleueth faste to the Lord, seiynge, Bi departyng the Lord schal departe me fro his puple; and a geldyng, ether a chast man, seie not, Lo! Y am a drie tree.
4 Popeza Yehova akuti, “Wofulidwa amene amasunga masabata anga, nachita zokomera Ine ndi kusunga pangano langa,
For the Lord seith these thingis to geldingis, that kepen my sabatis, and chesen what thingis Y wolde, and holden my boond of pees.
5 ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake, kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi. Ndidzawapatsa dzina labwino, losatha ndi losayiwalika.”
Y schal yyue to hem a place in myn hous, and in my wallis, and the beste name of sones and douytris; Y schal yyue to hem a name euerlastynge, that schal not perische.
6 Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova, motero kuti amamutumikira Iye, amakonda dzina la Yehova, amamugwirira ntchito, komanso kusunga Sabata osaliyipitsa ndi kusunga bwino pangano langa,
And Y schal brynge in to blis the sones of a comelyng, that cleuen faste to the Lord, that thei worschipe hym, and loue his name, that thei be to hym in to seruauntis; ech man kepynge the sabat, that he defoule it not, and holdynge my boond of pees;
7 amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika, ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero. Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe. Paja nyumba yanga idzatchedwa nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
Y schal brynge hem in to myn hooli hil, and Y schal make hem glad in the hous of my preier; her brent sacrifices and her slayn sacrifices schulen plese me on my auter; for whi myn hous schal be clepid an hous of preier to alle puplis,
8 Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti, “Ndidzasonkhanitsano anthu ena kuwonjezera amene anasonkhana kale.”
seith the Lord God, that gaderith togidere the scaterid men of Israel. Yit Y schal gadere togidere to hym alle the gaderid men therof.
9 Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo, inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
Alle beestis of the feeld, come ye to deuoure, alle beestis of the forest.
10 Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu, onse ndi opanda nzeru; onse ndi agalu opanda mawu, samatha kuwuwa: amagona pansi nʼkumalota amakonda kugona tulo.
Alle the biholderis therof ben blinde, alle thei knewen not; doumbe doggis, that moun not berke, seynge veyn thingis, slepynge, and louynge dremes;
11 Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu; sakhuta konse. Abusa nawonso samvetsa zinthu; onse amachita monga akufunira, aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
and moost vnschamefast doggis knewen not fulnesse. Tho scheepherdis knewen not vndurstondyng; alle thei bowyden in to her weie, ech man to his aueryce, fro the hiyeste `til to the laste.
12 Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo! Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta! Mawa lidzakhala ngati leroli, kapena kuposa lero lino.”
Come ye, take we wyn, and be we fillid of drunkenesse; and it schal be as to dai, so and to morewe, and myche more.

< Yesaya 56 >