< Yesaya 56 >

1 Yehova akuti, “Chitani chilungamo ndi zinthu zabwino, chifukwa chipulumutso changa chili pafupi ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
This is what the Lord says: Follow the law, and do what is right, for my salvation will soon arrive, and my goodness will be revealed.
2 Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi, munthu amene amalimbika kuzichita, amene amasunga Sabata osaliyipitsa, ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”
Blessed is everyone who does this—those who keep to it, who observe the Sabbath without violating it, and who don't do anything wrong.
3 Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti, “Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.” Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti, “Ine ndine mtengo wowuma basi.”
Don't allow foreigners who have dedicated themselves to the Lord say, “The Lord will definitely exclude me from his people.” And don't allow eunuchs to say, “Look at me—I'm as worthless as a dried-up tree because I'm childless.”
4 Popeza Yehova akuti, “Wofulidwa amene amasunga masabata anga, nachita zokomera Ine ndi kusunga pangano langa,
For this is what the Lord says: To the eunuchs who observe my Sabbaths, who choose to do what pleases me, and to keep my agreement,
5 ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake, kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi. Ndidzawapatsa dzina labwino, losatha ndi losayiwalika.”
I will give them, in my house and within my walls, a place to remember them and a reputation better than that of sons and daughters. I will give them an everlasting reputation that will never fade.
6 Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova, motero kuti amamutumikira Iye, amakonda dzina la Yehova, amamugwirira ntchito, komanso kusunga Sabata osaliyipitsa ndi kusunga bwino pangano langa,
About the foreigners who have dedicated themselves to the Lord, who worship him, who love the Lord, and who are his servants, everyone who observes the Sabbath without violating it and who keep to my agreement—
7 amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika, ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero. Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe. Paja nyumba yanga idzatchedwa nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
I will bring these foreigners to my holy mountain and make them happy in my house of prayer. I will accept their burnt offerings and sacrifices, because my Temple will be called a house of prayer for all nations.
8 Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti, “Ndidzasonkhanitsano anthu ena kuwonjezera amene anasonkhana kale.”
This is what the Lord God says, who brought back the scattered people of Israel: I will bring back still others to join you.
9 Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo, inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
Come, wild animals, wild animals of the countryside and forests, come and eat my people!
10 Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu, onse ndi opanda nzeru; onse ndi agalu opanda mawu, samatha kuwuwa: amagona pansi nʼkumalota amakonda kugona tulo.
For all the watchmen are blind. None of them know what's going on. They're all silent—they can't bark. They spend their time lying down, dreaming, loving to sleep.
11 Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu; sakhuta konse. Abusa nawonso samvetsa zinthu; onse amachita monga akufunira, aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
They're greedy dogs that are never satisfied. They're sheepdogs who don't know their job. All of them go their own way, each of them looking out for themselves.
12 Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo! Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta! Mawa lidzakhala ngati leroli, kapena kuposa lero lino.”
“Come on,” they say, “I'll get some wine and let's get drunk! We'll do this today, and tomorrow we'll drink so much more!”

< Yesaya 56 >