< Yesaya 56 >

1 Yehova akuti, “Chitani chilungamo ndi zinthu zabwino, chifukwa chipulumutso changa chili pafupi ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
Toto praví Hospodin: Ostříhejte soudu, a čiňte spravedlnost; nebo brzo spasení mé přijde, a spravedlnost má zjevena bude.
2 Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi, munthu amene amalimbika kuzichita, amene amasunga Sabata osaliyipitsa, ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”
Blahoslavený člověk, kterýž činí to, a syn člověka, kterýž se přídrží toho, ostříhaje soboty, aby jí nepoškvrňoval, a ostříhaje ruky své, aby nic zlého neučinila.
3 Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti, “Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.” Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti, “Ine ndine mtengo wowuma basi.”
Nechť tedy nemluví cizozemec, kterýž se připojuje k Hospodinu, říkaje: Jistě odloučil mne Hospodin od lidu svého. Též ať neříká kleštěnec: Aj, já jsem dřevo suché.
4 Popeza Yehova akuti, “Wofulidwa amene amasunga masabata anga, nachita zokomera Ine ndi kusunga pangano langa,
Nebo toto praví Hospodin o kleštěncích, kteříž by ostříhali sobot mých, a zvolili to, což mi se líbí, a drželi smlouvu mou:
5 ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake, kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi. Ndidzawapatsa dzina labwino, losatha ndi losayiwalika.”
Že dám jim v domě svém a mezi zdmi svými místo, a jméno lepší nežli synů a dcer. Jméno věčné dám jim, kteréž nebude vyhlazeno.
6 Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova, motero kuti amamutumikira Iye, amakonda dzina la Yehova, amamugwirira ntchito, komanso kusunga Sabata osaliyipitsa ndi kusunga bwino pangano langa,
Cizozemce pak, kteříž by se připojili k Hospodinu, aby sloužili jemu, a milovali jméno Hospodinovo, jsouce u něho za služebníky, všecky ostříhající soboty, aby jí nepoškvrňovali, a držící smlouvu mou,
7 amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika, ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero. Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe. Paja nyumba yanga idzatchedwa nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
Ty přivedu k hoře svatosti své, a obveselím je v domě svém modlitebném. Zápalové jejich a oběti jejich příjemné mi budou na oltáři mém; nebo dům můj dům modlitby slouti bude u všech národů.
8 Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti, “Ndidzasonkhanitsano anthu ena kuwonjezera amene anasonkhana kale.”
Pravíť Panovník Hospodin, kterýž shromažďuje rozehnané Izraelovy: Ještěť shromáždím k němu a k shromážděným jeho.
9 Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo, inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
Všecka zvířata polní poďte žráti, i všecka zvířata lesní.
10 Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu, onse ndi opanda nzeru; onse ndi agalu opanda mawu, samatha kuwuwa: amagona pansi nʼkumalota amakonda kugona tulo.
Strážní jeho jsou slepí, všickni napořád nic neznají, všickni jsou psi němí, aniž mohou štěkati; jsou ospalci, leží, milujíce dřímotu.
11 Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu; sakhuta konse. Abusa nawonso samvetsa zinthu; onse amachita monga akufunira, aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
Nadto jsou psi obžerní, nevědí, kdy jsou syti; pročež sami se pasou. Neumějí učiti, všickni k cestám svým patří, jeden každý k zisku svému po své straně.
12 Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo! Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta! Mawa lidzakhala ngati leroli, kapena kuposa lero lino.”
Poďte, naberu vína, a opojíme se nápojem opojným, a bude rovně zítřejší jako dnešní den, nýbrž větší a mnohem hojnější.

< Yesaya 56 >