< Yesaya 55 >

1 “Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu, bwerani madzi alipo; ndipo inu amene mulibe ndalama bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye! Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
We lina lonke elomileyo, wozani emanzini, laye ongelamali, wozani, lithenge, lidle; yebo, wozani lithenge ngaphandle kwemali langaphandle kwentengo, iwayini lochago.
2 Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya, ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa? Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino; ndipo mudzisangalatse.
Kungani lichitha imali kokungeyisikho kudla, lomtshikatshika wenu kokungenelisiyo? Ngilalelani lokungilalela, lidle okuhle, lomphefumulo wenu kawuzithokozise kokunonileyo.
3 Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine; mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo. Ndidzachita nanu pangano losatha, chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
Thobani indlebe yenu, lize kimi, zwanini, njalo umphefumulo wenu uzaphila; njalo ngizakwenza isivumelwano esilaphakade lani, izisa eziqinisekileyo zikaDavida.
4 Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu, kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
Khangela, ngimnike waba ngumfakazi ebantwini, umkhokheli lomlawuli ebantwini.
5 Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa, ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu. Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu, Woyerayo wa Israeli, wakuvekani ulemerero.”
Khangela, uzabiza isizwe ongasaziyo, lezizwe ebezingakwazi zizagijimela kuwe, ngenxa yeNkosi, uNkulunkulu wakho, langoNgcwele kaIsrayeli, ngoba ekudumisile.
6 Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka. Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
Dingani iNkosi iselokutholwa, ibizeni iseseduze.
7 Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa, ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa. Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo, ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
Omubi katshiye indlela yakhe, lomuntu ongalunganga imicabango yakhe; kabuyele eNkosini, njalo izakuba lomusa kuye, lakuNkulunkulu wethu, ngoba uzathethelela ngokukhulu.
8 “Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu, ngakhale njira zanu si njira zanga,” akutero Yehova.
Ngoba imicabango yami kayisiyo imicabango yenu, lendlela zenu kayisizo izindlela zami, itsho iNkosi.
9 “Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
Ngoba njengoba amazulu ephakeme kulomhlaba, ngokunjalo indlela zami ziphakeme kulendlela zenu, lemicabango yami kulemicabango yenu.
10 Monga mvula ndi chisanu chowundana zimatsika kuchokera kumwamba, ndipo sizibwerera komweko koma zimathirira dziko lapansi. Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
Ngoba njengalokhu izulu lisehla, leliqhwa elikhithikileyo kuvela emazulwini, kungabuyeli khona, kodwa kuthelela umhlaba, kuwenze ukuthi uthele uhlume, ukuze unike inhlanyelo kumhlanyeli, lokudla kodlayo,
11 Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
lizakuba njalo ilizwi lami eliphuma emlonyeni wami; kaliyikubuyela kimi lize, kodwa lizakwenza lokho engikufisayo, liphumelele kulokhu engilithumele khona.
12 Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe ndipo adzakutsogolerani mwamtendere; mapiri ndi zitunda zidzakuyimbirani nyimbo, ndipo mitengo yonse yamʼthengo idzakuwombereni mʼmanja.
Ngoba lizaphuma ngentokozo, njalo likhokhelwe ngokuthula; izintaba lamaqaqa kuzaqhamuka ngokuhlabela phambi kwenu, lezihlahla zonke zeganga zitshaye izandla.
13 Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini, ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu. Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova, ngati chizindikiro chamuyaya, chimene sichidzafafanizika konse.”
Endaweni yameva kuzamila ifiri, lendaweni yokhula oluhlabayo kumile imiteli; kuzakuba seNkosini libizo, kube yisibonakaliso esilaphakade esingayikuqunywa.

< Yesaya 55 >