< Yesaya 55 >
1 “Bwerani, inu nonse amene muli ndi ludzu, bwerani madzi alipo; ndipo inu amene mulibe ndalama bwerani, mudzagule chakudya kuti mudye! Bwerani mudzagule vinyo ndi mkaka osalipira ndalama, osalipira chilichonse.
Ej, všickni žízniví, poďte k vodám, i vy, kteříž nemáte žádných peněz. Poďte, kupujte a jezte, poďte, pravím, kupujte bez peněz a bez záplaty víno a mléko.
2 Chifukwa chiyani ndalama zanu mukuwonongera zinthu zimene samadya, ndipo mukuwononga malipiro anu pa zinthu zimene sizikhutitsa? Tamverani, mvetsetsani zimene ndikunena kuti mudye zimene zili zabwino; ndipo mudzisangalatse.
Proč vynakládáte peníze ne za chléb, a práci svou za to, což nenasycuje? Poslechněte mne raději, a jezte to, což jest dobrého, a nechť se kochá v tuku duše vaše.
3 Tcherani makutu ndipo mubwere kwa Ine; mvereni Ine, kuti mukhale ndi moyo. Ndidzachita nanu pangano losatha, chikondi changa chija chosasinthika ndi chodalirika ndinalonjeza Davide.
Nakloňte ucha svého, a poďte ke mně, poslechněte, a budeť živa duše vaše; učiním zajisté s vámi smlouvu věčnou, milosrdenství Davidova přepevná.
4 Taonani, ine ndamusankha kuti akhale mboni yanga kwa mitundu ya anthu, kuti akhale mtsogoleri ndi wolamulira mitundu ya anthu.
Aj, za svědka národům dal jsem jej, za vůdce a učitele národům.
5 Ndithu inu mudzayitanitsa mitundu ya anthu imene simuyidziwa, ndipo mitundu ya anthu imene sikudziwani idzabwera ndi liwiro kwa inu. Izi zidzatero chifukwa Yehova Mulungu wanu, Woyerayo wa Israeli, wakuvekani ulemerero.”
Aj, národu, k němužs se neznal, povoláš, a národové, kteříž tě neznali, k tobě se sběhnou, pro Hospodina Boha tvého, a Svatého Izraelského, nebo tě oslaví.
6 Funafunani Yehova pamene Iye akupezeka. Mupemphere kwa Iye pamene ali pafupi.
Hledejte Hospodina, pokudž může nalezen býti; vzývejte ho, pokudž blízko jest.
7 Woyipa asiye makhalidwe ake oyipa, ndipo wosalungama asinthe maganizo ake oyipa. Abwerere kwa Yehova, ndipo adzamuchitira chifundo, ndi kwa Mulungu wathu, pakuti adzamukhululukira koposa.
Opusť bezbožný cestu svou, a člověk nepravý myšlení svá, a nechť se navrátí k Hospodinu, i slitujeť se nad ním, a k Bohu našemu, nebť jest hojný k odpuštění.
8 “Pakuti maganizo anga siwofanana ndi maganizo anu, ngakhale njira zanu si njira zanga,” akutero Yehova.
Nejsouť zajisté myšlení má jako myšlení vaše, ani cesty vaše jako cesty mé, praví Hospodin.
9 “Monga momwe mlengalenga muli kutali ndi dziko lapansi, momwemonso zochita zanga nʼzolekana kutali ndi zochita zanu, ndipo maganizo anga ndi osiyana kutali ndi maganizo anu.
Ale jakož vyšší jsou nebesa než země, tak převyšují cesty mé cesty vaše, a myšlení má myšlení vaše.
10 Monga mvula ndi chisanu chowundana zimatsika kuchokera kumwamba, ndipo sizibwerera komweko koma zimathirira dziko lapansi. Ndipo zimameretsa ndi kukulitsa zomera kenaka nʼkupatsa mlimi mbewu ndi chakudya.
Nebo jakož prší déšť neb sníh s nebe, a zase se tam nenavracuje, ale napájí zemi, a činí ji plodistvou a úrodnou, tak že vydává símě rozsívajícímu, a chléb jedoucímu,
11 Ndi mmenenso amachitira mawu ochokera mʼkamwa mwanga. Sadzabwerera kwa Ine kopanda phindu lake, koma adzachita zonse zimene ndifuna, ndipo adzakwaniritsa cholinga chimene ndinawatumira.
Tak bude slovo mé, kteréž vyjde z úst mých. Nenavrátí se ke mně prázdné, ale učiní to, což mi se líbí, a prospěšně to vykoná, k čemuž je posílám.
12 Inu mudzatuluka mu mzindawo mwachimwemwe ndipo adzakutsogolerani mwamtendere; mapiri ndi zitunda zidzakuyimbirani nyimbo, ndipo mitengo yonse yamʼthengo idzakuwombereni mʼmanja.
A protož s veselím vyjdete, a v pokoji sprovozeni budete. Hory i pahrbkové zvučně naproti vám prozpěvovati budou, a všecko dříví polní rukama plésati bude.
13 Mʼmalo mʼmene tsopano muli mitengo ya minga mudzamera mitengo ya payini, ndipo kumene kuli mkandankhuku kudzamera mchisu. Zimenezi zidzakhala chikumbutso cha Yehova, ngati chizindikiro chamuyaya, chimene sichidzafafanizika konse.”
Místo chrastiny vzejde jedlé, a místo hloží vyroste myrtus, a bude to Hospodinu k slávě, na znamení věčné, kteréž nebude vyhlazeno.