< Yesaya 54 >
1 “Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
Fröjda dig, du ofruktsamma, du som intet föder; gläd dig med fröjd och berömmelse, du som intet hafvandes är; ty den ensamma hafver flera barn än den som man hafver, säger Herren.
2 Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
Förvidga din pauluns rum, och utsträck tapeten åt din tjäll; spar icke, förläng din tåg, och befäst dina pålar.
3 Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
Ty du skall brista ut på högra sidon och den venstra, och din säd skall ärfa Hedningarna, och bo uti de förödda städer.
4 “Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
Frukta dig intet; ty du skall icke till skam varda. Var icke blödig; ty du skall icke varda till blygd, utan du skall förgäta dins jungfrudoms blygd, och din enkodoms neso icke mer ihågkomma.
5 Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
Ty den dig gjort hafver, han är din man; Herren Zebaoth är hans Namn; och din förlossare, den Helige i Israel, den alla verldenes Gud kallad varder.
6 Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
Ty Herren hafver låtit dig vara uti det ryktet, att du äst såsom en öfvergifven och af hjertat bedröfvad qvinna, och såsom en ung hustru, den bortdrifven är, säger din Gud.
7 “Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
Jag hafver uti ett litet ögnablick öfvergifvit dig; men med stor barmhertighet vill jag församla dig.
8 Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
Jag hafver, uti vredenes ögnablick, som snarast gömt bort mitt ansigte för dig; men med eviga nåd vill jag förbarma mig öfver dig, säger Herren, din förlossare.
9 “Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
Ty detta skall vara mig såsom Noahs flod; då jag svor, att Noahs flod icke mer skulle gå öfver jordena; alltså hafver jag svorit, att jag icke skall vredgas öfver dig, eller näpsa dig.
10 Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
Ty bergen skola väl vika, och högarna falla; men min nåd skall icke vika ifrå dig, och mins frids förbund skall icke förfalla, säger Herren, din förbarmare.
11 “Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
Du elända, öfver hvilka alle väder gå, och du tröstlösa, si, jag vill lägga dina stenar såsom en prydning, och lägga din grundval med saphirer;
12 Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
Och din fenster göra af christall, och dina portar af rubiner, och alla dina gränsor af utkorada stenar;
13 Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
Och all din barn lärd af Herranom, och stor frid dinom barnom.
14 Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
Du skall genom rättfärdighet beredd varda; du skall vara långt ifrån öfvervåld och orätt, så att du icke skall torfva frukta dig derföre; och ifrå förskräckelse, ty det skall icke nalkas dig.
15 Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
Si, ho vill församla sig emot dig, och öfverfalla dig, då de församla sig utan mig?
16 “Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
Si, jag gör det, att smeden, som uppblås kolen i elden, han gör der ett tyg af, till sitt verk; ty jag gör ock, att förderfvaren förgås.
17 palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.
Ty hvart och ett tyg, som emot dig tillredt varder, thy skall icke väl gå; och hvar och en tunga, som sig uppsätter emot dig, den skall du fördöma i dome. Detta är Herrans tjenares arf, och deras rättfärdighet af mig, säger Herren.