< Yesaya 54 >
1 “Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
»Zapoj, oh jalova, ti, ki nisi nosila, izbruhni v petje in glasno zavpij, ti, ki se nisi mučila z otrokom, kajti več je otrok zapuščene kakor otrok poročene žene, « govori Gospod.
2 Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
Povečaj kraj svojega šotora in naj razprostrejo zagrinjala tvojih prebivališč. Ne šparaj, podaljšaj svoje vrvi in ojačaj svoje kline,
3 Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
kajti izbruhnila boš na desno roko in na levo in tvoje seme bo podedovalo pogane in naredila boš, da bodo opustela mesta naseljena.
4 “Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
Ne boj se, kajti ne boš osramočena niti ne bodi zbegana, kajti ne prideš v sramoto, kajti pozabila boš sramoto svoje mladosti in ne boš se več spominjala graje svojega vdovstva.
5 Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
Kajti tvoj Stvarnik je tvoj soprog, Gospod nad bojevniki je njegovo ime in tvoj Odkupitelj Sveti Izraelov; imenovali ga bodo Bog celotne zemlje.
6 Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
Kajti Gospod te je poklical kakor žensko, zapuščeno in užaloščeno v duhu in ženo mladosti, ko si bila zavržena, « govori tvoj Bog.
7 “Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
»Kajti za kratek trenutek sem te zapustil, toda z velikimi usmiljenji te bom zbral.
8 Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
Z malce besa sem za trenutek skril svoj obraz pred teboj, toda z večno prijaznostjo bom imel usmiljenje nad teboj, « govori Gospod, tvoj Odkupitelj.
9 “Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
»Kajti to mi je kakor so bile Noetove vode, kajti kakor sem prisegel, da Noetove vode ne bodo več šle preko zemlje, tako sem prisegel, da ne bom ogorčen nad teboj niti te ne bom več oštel.
10 Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
Kajti gore se bodo umaknile in hribi bodo odstranjeni, toda moja prijaznost ne bo odšla od tebe niti zaveza mojega miru ne bo odstranjena, « govori Gospod, ki ima usmiljenje do tebe.
11 “Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
»Oh ti trpeča, premetavana z viharjem in nepotolažena, glej, tvoje kamne bom položil z lepimi barvami in tvoje temelje bom položil s safirji.
12 Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
Tvoja okna bom naredil iz ahata in tvoja velika vrata iz granata in vse tvoje meje iz prijetnih kamnov.
13 Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
Vsi tvoji otroci bodo poučevani od Gospoda in velik bo mir tvojih otrok.
14 Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
V pravičnosti boš utrjena, daleč boš od zatiranja, kajti ne boš se bala in [daleč boš] od strahote, kajti ta se ti ne bo približala.
15 Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
Glej, zagotovo se bodo zbrali skupaj, toda to ni od mene. Kdorkoli se bo skupaj zbral proti tebi, bo padel zaradi tebe.
16 “Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
Glej, jaz sem ustvaril kovača, ki v ognju razpihuje ogorke in ki prinaša orodje za svoje delo in jaz sem ustvaril kvarilca, da uničuje.
17 palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.
Nobeno orožje, ki je oblikovano zoper tebe, ne bo uspelo in vsak jezik, ki se bo na sodbi dvignil zoper tebe, boš obsodila. To je dediščina Gospodovih služabnikov in njihova pravičnost je od mene, « govori Gospod.