< Yesaya 54 >

1 “Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
Весели се, нероткињо која не рађаш, запевај и покликни ти, која не трпиш муке од порођаја, јер пуста има више деце него ли она која има мужа, вели Господ.
2 Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
Рашири место шатора свог, и завесе стана твог нека се разастру, не брани, продужи ужа своја, коље своје утврди.
3 Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
Јер ћеш се надесно и налево распространити, и семе ће твоје наследити народе, и пусте ће градове населити.
4 “Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
Не бој се, јер се нећеш осрамотити, и немој се стидети, јер нећеш бити прекорна, него ћеш заборавити срамоту младости своје, и прекора удовиштва свог нећеш се више сећати.
5 Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
Јер ти је муж Творац твој, име Му је Господ над војскама, и Избавитељ ти је Светац Израиљев, Бог свој земљи зваће се.
6 Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
Јер као жену остављену и у духу ожалошћену дозва те Господ, и као младу жену пуштену, говори Господ.
7 “Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
Замало оставих те, али с великом милошћу прибраћу те.
8 Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
У малом гневу сакрих за час лице своје од тебе, али ћу те вечном милошћу помиловати, вели Избавитељ твој Господ.
9 “Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
Јер ми је то као потоп Нојев: јер као што се заклех да потоп Нојев неће више доћи на земљу, тако се заклех да се нећу разгневити на те нити ћу те карати.
10 Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
Ако ће се и горе помакнути и хумови се поколебати, опет милост моја неће се одмакнути од тебе, и завет мира мог неће се поколебати, вели Господ, који ти је милостив.
11 “Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
Невољнице, коју ветар размеће, која си без утехе, ево ја ћу наместити камење твоје на мрамору порфирном, и основаћу те на сафирима.
12 Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
И начинићу ти прозоре од кристала, и врата од камена рубина, и све међе твоје од драгог камења.
13 Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
А синови ће твоји сви бити научени од Господа, и обилан мир имаће синови твоји.
14 Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
Правдом ћеш се утврдити, далеко ћеш бити од насиља, те се нећеш бојати, и од страхоте, јер ти се неће приближити.
15 Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
Гле, биће их који ће се сабирати на те, али неће бити од мене; који се год саберу на те, пашће.
16 “Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
Гле, ја сам створио ковача који распаљује угљевље и вади оруђе за свој посао, ја сам створио и крвника да убија.
17 palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.
Никакво оружје начињено против тебе неће бити срећно, и сваки језик који се подигне на те на суду сапрећеш. То је наследство слуга Господњих и правда њихова од мене, вели Господ.

< Yesaya 54 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark