< Yesaya 54 >

1 “Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
Agkantaka, sika a lupes a babai; sika a saan a nagpasngay; agkantaka a sirarag-o ken agsangitka iti napigsa, sika a saan pay pulos a nagpasikal. Ta dagiti annak ti nabaybay-an a babai ket ad-adunto ngem kadagiti annak ti naasawaan a babai,” kuna ni Yahweh.
2 Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
Palawaem ti toldam ken iyukradmo dagiti kurtina ti toldam; paatidogem dagiti talim ken palagdaem dagiti pasokmo.
3 Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
Ta maiyukradkanto iti makanawan ken iti makanigid, ken parmekento dagiti kaputotam dagiti nasion ken agnaeddanto manen kadagiti langalang a siudad.
4 “Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
Saanka nga agbuteng ta saankanton a mabainan, wenno maupay ta saankanto a maibabain; malipatamto ti pannakaibabain ti kinaagtutubom ken ti pannakaibabain ti pannakabaybay-am.
5 Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
Ta ti Nangparsua kenka ket isu ti asawam; ni Yahweh a Mannakabalin-amin ti naganna. Ti Nasantoan ti Israel ket isu ti Mannubotmo; maawagan isuna a Dios ti sangalubongan.
6 Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
Ta inayabannaka manen ni Yahweh kas asawa a nabaybay-an ken agladladingit iti espiritu, kas iti babai nga ubing a nakiasawa ken nailaksid, kuna ti Diosmo.
7 “Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
“Binaybay-anka iti apagbiit a tiempo, ngem babaen iti dakkel nga asi alaenkanto.
8 Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
Iti nakaro a pungtotko inlingedko ti rupak kenka iti apagkanito; ngem babaen iti agnanayon a kinapudnok iti tulagko kaasiankanto-kuna ni Yahweh, a mangisalakan mo.
9 “Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
Ta daytoy ket kas kadagiti dandanum ni Noe kaniak: kas iti panangisapatak a saanen a layusen ti dandanum ni Noe ti daga, kasta met ti panangisapatak a saankanton nga ungtan wenno tubngaren.
10 Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
Ta uray no matuang dagiti bantay ken magungon dagiti turod, ngem saanto a maisina kenka ti kinapudno ti tulagko, wenno saanto a magungon ti tulagko a pannakikappia- kuna ni Yahweh, a naasi kenka.
11 “Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
Sika a nagsagaba, a kasla pinarparigat iti bagyo ken saan a naliwliwa, kitaem, bangonekto manen ti siudadmo babaen kadagiti agkakapateg a batbato, ken ikabilkonto dagiti pundasionmo babaen iti bato a sapiro.
12 Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
Aramidekto dagiti torrem babaen iti bato a rubi ken rumimrimat a batbato dagiti ruangam, ken napipintas a batbato dagiti akinruar a padermo.
13 Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
Ket suruanto ni Yahweh dagiti amin nga annakmo; ket dakkelto ti talna dagiti annakmo.
14 Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
Bangonenkanto manen iti kinalinteg. Saanmonto a pulos a mapadas ti pannakaidaddanes, ta saankanton a mabuteng, ken awanto iti nakabutbuteng nga umasideg kenka.
15 Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
Kitaem, no adda ti mangpataud iti riribuk, saanto daytoy a nagtaud kaniak; siasinoman a mangpataud iti riribuk kenka ket maparmekto.
16 “Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
Kitaem, pinarsuak ti mammanday, a mangpasged kadagiti beggang ket agpanday kadagiti armas a kas trabahona, ken pinarsuak ti manangdadael tapno mangdadael.
17 palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.
Awan ti naaramid nga armas nga agballigi a maibusor kenka; ket kedngamto iti pannakadusa ti siasinoman a mangakusar kenka. Daytoy ti tawid dagiti adipen ni Yahweh, ken ti pannangikalintegak kadakuada —kastoy ti pakaammo ni Yahweh.”

< Yesaya 54 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark