< Yesaya 54 >

1 “Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
Riemuitse, sinä hedelmätön, joka et ole synnyttänyt, huuda ilosta ja riemahda, sinä, joka et ole synnytyskivuissa ollut. Sillä hyljätyllä on lapsia enemmän kuin aviovaimolla, sanoo Herra.
2 Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
Tee avaraksi telttasi sija, levennettäköön sinun majojesi seinien kangas. Älä säästele! Pidennä telttaköytesi ja vahvista vaarnasi.
3 Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
Sillä sinä olet leviävä oikealle ja vasemmalle, sinun jälkeläisesi ottavat omiksensa kansat ja tekevät autiot kaupungit asutuiksi.
4 “Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
Älä pelkää, sillä et sinä häpeään joudu; älä ole häpeissäsi, sillä et sinä ole pettyvä. Nuoruutesi häpeän sinä olet unhottava, leskeytesi pilkkaa et ole enää muistava.
5 Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
Sillä hän, joka sinut teki, on sinun aviomiehesi, Herra Sebaot on hänen nimensä, sinun lunastajasi on Israelin Pyhä, hän joka kaiken maan Jumalaksi kutsutaan.
6 Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
Sillä niinkuin hyljätyn, syvästi murheellisen vaimon on Herra sinut kutsunut-nuoruuden vaimon, joka on ollut halveksittu, sanoo sinun Jumalasi.
7 “Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
Vähäksi silmänräpäykseksi minä hylkäsin sinut, mutta minä kokoan sinut jälleen suurella laupeudella.
8 Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
Ylitsevuotavassa vihassani minä peitin sinulta kasvoni silmänräpäykseksi, mutta minä armahdan sinut iankaikkisella armolla, sanoo Herra, sinun lunastajasi.
9 “Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
Sillä tämä on minulle, niinkuin olivat Nooan vedet: niinkuin minä vannoin, etteivät Nooan vedet enää tulvi maan ylitse, niin minä vannon, etten enää vihastu sinuun enkä sinua nuhtele.
10 Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
Sillä vuoret väistykööt ja kukkulat horjukoot, mutta minun armoni ei sinusta väisty, eikä minun rauhanliittoni horju, sanoo Herra, sinun armahtajasi.
11 “Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
Sinä kurja, myrskyn raastama, sinä lohduton! Katso, minä muuraan sinun kivesi kiiltokivellä, panen sinun perustuksesi safiireista,
12 Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
minä teen sinun harjasi rubiineista ja sinun porttisi kristalleista ja koko sinun ympärysmuurisi jalokivistä.
13 Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
Sinun lapsesi ovat kaikki Herran opetuslapsia, ja suuri rauha on sinun lapsillasi oleva.
14 Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
Sinut vahvistetaan vanhurskaudella; sinä olet oleva kaukana väkivallasta, sillä ei sinulla ole pelkäämistä, ja kaukana hävityksestä, sillä ei se sinua lähesty.
15 Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
Jos sinun kimppuusi karataan, ei se ole minusta; joka kimppuusi karkaa, se eteesi kaatuu.
16 “Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
Katso, minä olen luonut sepän, joka lietsoo hiilivalkeata ja kuonnuttaa aseen käytäntöönsä; mutta minä olen myös luonut tuhontuottajan hävittämään sen.
17 palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.
Jokainen ase, joka valmistetaan sinun varallesi, on oleva tehoton; ja jokaisen kielen, joka nousee käymään sinun kanssasi oikeutta, sinä osoitat vääräksi. Tämä on Herran palvelijain perintöosa, tämä heidän vanhurskautensa, minulta saatu, sanoo Herra.

< Yesaya 54 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark