< Yesaya 54 >

1 “Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
to sing barren not to beget to break out cry and to cry out not to twist: writh in pain for many son: child be desolate: destroyed from son: child rule: to marry to say LORD
2 Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
to enlarge place tent your and curtain tabernacle your to stretch not to withhold to prolong cord your and peg your to strengthen: strengthen
3 Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
for right and left to break through and seed: children your nation to possess: take and city be desolate: destroyed to dwell
4 “Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
not to fear for not be ashamed and not be humiliated for not be ashamed for shame youth your to forget and reproach widowhood your not to remember still
5 Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
for rule: to marry you to make you LORD Hosts name his and to redeem: redeem your holy Israel God all [the] land: country/planet to call: call by
6 Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
for like/as woman: wife to leave: forsake and to hurt spirit to call: call to you LORD and woman: wife youth for to reject to say God your
7 “Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
in/on/with moment small to leave: forsake you and in/on/with compassion great: large to gather you
8 Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
in/on/with overflowing wrath to hide face my moment from you and in/on/with kindness forever: enduring to have compassion you to say to redeem: redeem your LORD
9 “Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
for water Noah this to/for me which to swear from to pass water Noah still upon [the] land: country/planet so to swear from be angry upon you and from to rebuke in/on/with you
10 Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
for [the] mountain: mount to remove and [the] hill to shake and kindness my from with you not to remove and covenant peace my not to shake to say to have compassion you LORD
11 “Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
afflicted to rage not to be sorry: comfort behold I to stretch in/on/with color stone your and to found you in/on/with sapphire
12 Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
and to set: make ruby sun your and gate your to/for stone carbuncle and all border: boundary your to/for stone pleasure
13 Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
and all son: child your disciple LORD and many peace son: child your
14 Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
in/on/with righteousness to establish: establish to remove from oppression for not to fear and from terror for not to present: come to(wards) you
15 Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
look! to quarrel to quarrel end from [obj] me who? to quarrel with you upon you to fall: fall
16 “Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
(behold *Q(K)*) I to create artificer to breathe in/on/with fire coal and to come out: produce article/utensil to/for deed: work his and I to create to ruin to/for to destroy
17 palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.
all article/utensil to form: formed upon you not to prosper and all tongue to arise: attack with you to/for justice: judgement be wicked this inheritance servant/slave LORD and righteousness their from with me utterance LORD

< Yesaya 54 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark