< Yesaya 54 >

1 “Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
“Sing, barren, you who didn’t give birth; break out into singing, and cry aloud, you who did not travail with child: for the deserted wife will have more children than the children of the married wife,” says Adonai.
2 Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
“Enlarge the place of your tent, and let them stretch out the curtains of your habitations; don’t spare: lengthen your cords, and strengthen your stakes.
3 Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
For you will spread out on the right hand and on the left; and your offspring will possess the nations, and settle in desolate cities.
4 “Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
“Don’t be afraid; for you will not be ashamed. Don’t be confounded; for you will not be disappointed. For you will forget the shame of your youth; and the reproach of your widowhood you shall remember no more.
5 Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
For your Maker is your husband; Adonai Tzva'ot [Yahweh Commander of heaven’s armies] is his name. The haKadosh Isra'el [the Holy One of God prevails] is your Redeemer. He will be called the God of the whole earth.
6 Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
For Adonai has called you as a wife forsaken and grieved in spirit, even a wife of youth, when she is cast off,” says your God.
7 “Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
“For a small moment have I forsaken you; but with great racham ·merciful love· will I gather you.
8 Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
In overflowing wrath I hid my face from you for a moment; but with everlasting cheshed ·loving-kindness· I will have racham ·merciful love· on you,” says Adonai your Redeemer.
9 “Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
“For this is like the waters of Noah [Rest] to me; for as I have sworn that the waters of Noah [Rest] will no more go over the earth, so have I sworn that I will not be angry with you, nor rebuke you.
10 Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
For the mountains may depart, and the hills be removed; but my cheshed ·loving-kindness· will not depart from you, and my covenant ·binding contract between two or more parties· of peace will not be removed,” says Adonai who has mercy on you.
11 “Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
“You afflicted, tossed with storms, and not comforted, behold, I will set your stones in beautiful colors, and lay your foundations with sapphires.
12 Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
I will make your pinnacles of rubies, your gates of sparkling jewels, and all your walls of precious stones.
13 Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
All your children will be taught by Adonai; and your children’s peace will be great.
14 Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
In righteousness you will be established. You will be far from oppression, for you will not be afraid; and far from terror, for it shall not come near you.
15 Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
Behold, they may gather together, but not by me. Whoever gathers together against you will fall because of you.
16 “Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
“Behold, I have created the blacksmith who fans the coals into flame, and forges a weapon for his work; and I have created the destroyer to destroy.
17 palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.
No weapon that is formed against you will prevail; and you will condemn every tongue that rises against you in judgment. This is the heritage of Adonai’s servants, and their righteousness is of me,” says Adonai.

< Yesaya 54 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark