< Yesaya 53 >
1 Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
Чине а крезут ын чея че ни се вестисе? Чине а куноскут брацул Домнулуй?
2 Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
Ел а крескут ынаинтя Луй ка о одраслэ слабэ, ка ун Лэстар каре есе динтр-ун пэмынт ускат. Н-авя нич фрумусеце, нич стрэлучире ка сэ не атрагэ привириле ши ынфэцишаря Луй н-авя нимик каре сэ не плакэ.
3 Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
Диспрецуит ши пэрэсит де оамень, ом ал дурерий ши обишнуит ку суферинца, ера аша де диспрецуит, кэ ыць ынторчяй фаца де ла Ел, ши ной ну Л-ам бэгат ын сямэ.
4 Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
Тотушь Ел суферинцеле ноастре ле-а пуртат ши дурериле ноастре ле-а луат асупра Луй, ши ной ам крезут кэ есте педепсит, ловит де Думнезеу ши смерит.
5 Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
Дар Ел ера стрэпунс пентру пэкателе ноастре, здробит пентру фэрэделеӂиле ноастре. Педяпса каре не дэ пачя а кэзут песте Ел, ши прин рэниле Луй сунтем тэмэдуиць.
6 Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
Ной рэтэчям ку тоций ка ниште ой, фиекаре ышь ведя де друмул луй, дар Домнул а фэкут сэ кадэ асупра Луй нелеӂюиря ноастрэ, а тутурор.
7 Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
Кынд а фост кинуит ши асуприт, н-а дескис гура делок, ка ун мел пе каре-л дучь ла мэчелэрие ши ка о оае мутэ ынаинтя челор че о тунд: н-а дескис гура.
8 Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
Ел а фост луат прин апэсаре ши жудекатэ, дар чине дин чей де пе время Луй а крезут кэ Ел фусесе штерс де пе пэмынтул челор вий ши ловит де моарте пентру пэкателе попорулуй меу?
9 Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
Гроапа Луй а фост пусэ ынтре чей рэй, ши мормынтул Луй, ла ун лок ку чел богат, мэкар кэ ну сэвыршисе ничо нелеӂюире ши ну се гэсисе ничун виклешуг ын гура Луй.
10 Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
Домнул а гэсит ку кале сэ-Л здробяскэ прин суферинцэ… Дар, дупэ че Ышь ва да вяца ка жертфэ пентру пэкат, ва ведя о сэмынцэ де урмашь, ва трэи мулте зиле ши лукраря Домнулуй ва пропэши ын мыниле Луй.
11 Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
„Ва ведя родул мунчий суфлетулуй Луй ши Се ва ынвиора. Прин куноштинца Луй, Робул Меу чел неприхэнит ва пуне пе мулць оамень ынтр-о старе дупэ воя луй Думнезеу ши ва луа асупра Луй повара нелеӂюирилор лор.
12 Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.
Де ачея Ый вой да партя Луй ла ун лок ку чей марь ши ва ымпэрци прада ку чей путерничь, пентру кэ С-а дат пе Сине Ынсушь ла моарте ши а фост пус ын нумэрул челор фэрэделеӂе, пентру кэ а пуртат пэкателе мултора ши С-а ругат пентру чей виноваць.”