< Yesaya 53 >

1 Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
چه کسی پیام ما را باور کرده، و بازوی توانای خداوند بر چه کسی آشکار شده است!
2 Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
در نظر خدا او مانند درخت سبزی بود که در زمین خشک و شوره‌زار روییده و ریشه دوانده باشد؛ اما در نظر ما او زیبایی و جلوه‌ای نداشت که مشتاقش باشیم.
3 Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
او را خوار شمردیم و رد کردیم، اما او درد و غم ما را تحمل کرد. همهٔ ما از او رو برگردانیدیم. او خوار شد و ما هیچ اهمیت ندادیم.
4 Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
این دردهای ما بود که او به جان گرفته بود، این رنجهای ما بود که او بر خود حمل می‌کرد؛ اما ما گمان کردیم این درد و رنج مجازاتی است که خدا بر او فرستاده است.
5 Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
برای گناهان ما بود که او مجروح شد و برای شرارت ما بود که او را زدند. او تنبیه شد تا ما سلامتی کامل داشته باشیم. از زخمهای او ما شفا یافتیم.
6 Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
ما همچون گوسفندانی که آواره شده باشند، گمراه شده بودیم؛ راه خدا را ترک کرده به راههای خود رفته بودیم. با وجود این، خداوند تقصیرها و گناهان همهٔ ما را به حساب او گذاشت!
7 Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
با او با بی‌رحمی رفتار کردند، اما او تحمل کرد و زبان به شکایت نگشود. همچنانکه بَره را به سوی کشتارگاه می‌برند، او را نیز به کشتارگاه بردند. او مثل گوسفندی که پشمهایش را می‌چینند، لب به اعتراض نگشود.
8 Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
به ناحق او را به مرگ سپردند و کسی از نسل او اعتراض نکرد. زیرا او از دنیای زندگان منقطع شد؛ آری، به سبب عصیان قوم من مجازات شد.
9 Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
هنگامی که خواستند او را همراه خطاکاران دفن کنند، او را در قبر مردی ثروتمند گذاشتند؛ اما هیچ خطایی از او سر نزده بود و هیچ حرف نادرستی از دهانش بیرون نیامده بود.
10 Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
خداوند می‌فرماید: «این خواست من بود که او رنج بکشد و بمیرد. او جانش را قربانی کرد تا آمرزش گناهان را به ارمغان آورد، بنابراین صاحب فرزندان بی‌شمار خواهد شد. او زندگی را از سر خواهد گرفت و ارادهٔ من به دست او اجرا خواهد شد.
11 Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
هنگامی که ببیند عذابی که کشیده چه ثمری به بار آورده، راضی و خشنود خواهد شد. خدمتگزار عادل من بار گناهان بسیاری از مردم را به دوش خواهد گرفت و من به خاطر او آنها را خواهم بخشید.
12 Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.
به او مقامی بزرگ و قدرتی عظیم خواهم داد، زیرا او خود را فدا کرد، از خطاکاران محسوب شد، بار گناهان بسیاری را بر دوش گرفت و برای خطاکاران شفاعت کرد.»

< Yesaya 53 >