< Yesaya 53 >
1 Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
Ko wai i whakapono ki ta matou korero; i whakaaturia ranei ki a wai te ringaringa o Ihowa?
2 Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
Ka tupu ake hoki ia ki tona aroaro, ano he rakau wana, me te pakiaka hoki i te oneone maroke, kahore ona ahuareka, kahore hoki he pai; a ka titiro tatou ki a ia, te ai he ataahua e minamina ai tatou ki a ia.
3 Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
I whakahengia, i whakakahoretia ia e te tangata; he tangata pouri, kua mohio hoki ki te tangi: a, i ahua huna nga kanohi ki a ia; i whakakahoretia, kihai hoki tatou i whakaaro ki a ia.
4 Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
He pono, nana o tatou mate i pikau, nana hoki i waha o tatou pouri: ko tatou ia i mea, i tukitukia, i patua ia e te Atua, i whakawhiua.
5 Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
Kahore, i werohia ia mo o tatou he, i kurua mo o tatou kino: nona te whiunga i mau ai to tatou rongo, kei ona karawarawa hoki he rongoa mo tatou.
6 Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
Ko tatou katoa, ano he hipi, kua marara ke, kua anga atu tatou ki tona ara, ki tona ara; na Ihowa ia i mea kia tau iho ki a ia te kino o tatou katoa.
7 Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
I tukinotia ia, i whakawhiua; heoi kihai i kuihi tona mangai: ano he reme i arahina ia kia patua, me te hipi hoki i te aroaro o ona kaikutikuti e wahangu ana, kihai i kuihi tona waha.
8 Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
Na te tukino, na te whakawa, tangohia atu ana ia; tena ko tona whakatupuranga, ko wai o ratou i whakaaro kua wehea atu ia i te ao ora? he mahi he hoki na taku iwi i patua ai ia.
9 Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
A ka whakaritea hei te hunga kino he urupa mona; i te tangata taonga ia i tona matenga; ahakoa kahore ana mahi tutu, kahore ano he tinihanga i tona mangai.
10 Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
Otiia i pai hoki a Ihowa kia kurua ia; nana ia i mea kia mamae. Ina meinga e koe tona wairua hei whakahere mo te he, ka kite ia i tona uri, ka whakaroa i ona ra, a ko ta Ihowa i pai ai ka ata oti i a ia.
11 Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
Ka kite ia i ta tona wairua i uaua ai, a tatu ana te ngakau: ma te mohio ki a ia ka whakatikaia ai te tini e taku pononga tika; mana hoki o ratou kino e waha.
12 Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.
Mo reira ka hoatu e ahau he wahi mona i roto i o te hunga nui, a ka tu ngatahi ia me te hunga kaha i te taonga: mo tona wairua i ringihia e ia ki te mate, a i taua ngatahitia me nga poka ke; nana hoki nga hara o te tini i waha, nana i wawao nga poka ke.