< Yesaya 53 >

1 Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
Ki hitt a mi hírünknek, és az Örökkévaló karja kiben nyilvánult?
2 Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
Felnevekedett előtte mind a csemete, és mint gyökér elszikkadt földből, sem alakja neki, sem dísze; nézzük, de nincs ábrázata, hogy megkedvelnék.
3 Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
Megvetett és az emberek elhagyatottja, fájdalmak embere és betegség meghittje; és mint aki elől elrejtik az arcot, megvetett, és nem tekintettük.
4 Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
De bizony a mi betegségeinket ő viselte és a mi fájdalmainkat ő hordozta, pedig mi őt tekintettük sújtottnak, Istentől vertnek és nyomorgatottnak;
5 Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
megsebzett volt a mi bűntetteinktől, összezúzott a mi bűneinktől, jólétünkre való fenyítés volt rajta és az ő sebei által nekünk lett gyógyulás.
6 Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
Mindannyiunk mint a juhok tévelyegtünk, kiki a maga útjára fordultunk; az Örökkévaló pedig őt illette mindnyájunk bűnével.
7 Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
Szorongattatott, míg ő megalázta magát és nem nyitotta ki száját, mint a bárány, mely levágásra vitetik és mint a juh, mely nyírói előtt elnémul; nem nyitotta ki száját.
8 Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
Elnyomás által és ítélet által elragadtatott, kortársai közt pedig ki gondol arra, hogy kivágatott az élők országából: népem bűntette miatt ő sújtatott?
9 Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
Gonoszok mellé tették a sírját és gazdag mellé halálában, noha nem követett el erőszakot és nem volt álnokság a szájában.
10 Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
De az Örökkévaló akarta őt összezúzni, szenvedtetni: ha lelke bűnáldozattá teszi magát, látni fog magzatot, hosszú életű lesz, és az Örökkévaló akarata sikerül kezében.
11 Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
Lelkének fáradalmából fog látni, jóllakni; megismerésével visz igazságra az igaz, az én szolgám, sokakat és bűneiket ő hordozza.
12 Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.
Ezért kiosztok neki a sokak közt és hatalmasokkal osztja a zsákmányt, azért, hogy odaengedte halálra lelkét és bűnösökhöz számíttatta magát pedig ő sokaknak a vétkét viselte és a bűnösökért közbenjárt.

< Yesaya 53 >