< Yesaya 53 >

1 Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
Who has believed what they heard from us, and to whom has the arm of Yahweh been revealed?
2 Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
For he grew up before Yahweh like a sapling, and like a sprout out of parched earth; he had no remarkable appearance or splendor; when we saw him, there was no beauty to attract us.
3 Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
He was despised and rejected by people; a man of sorrows, and one familiar with pain. Like one from whom men hide their faces, he was despised; and we considered him insignificant.
4 Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
But surely he has borne our sicknesses and carried our sorrows; yet we thought he was being punished by God, struck by God, and afflicted.
5 Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
But he was pierced because of our rebellious deeds; he was crushed because of our sins. The punishment for our peace was on him, and with his wounds we are healed.
6 Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
We all like sheep have gone astray; we have each turned to his own way, and Yahweh has placed on him the iniquity of us all.
7 Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
He was oppressed; yet when he humbled himself, he did not open his mouth; as a lamb that is led to the slaughter, and as a sheep that before its shearers is silent, so he did not open his mouth.
8 Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
By coercion and judgment he was condemned; who from that generation thought anymore about him? But he was cut off from the land of the living; because of the offenses of my people the penalty was put on him.
9 Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
They placed his grave with the criminals, with a rich man in his death, although he had done no violence, nor had there been any deceit in his mouth.
10 Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
Yet it was Yahweh's will to crush him and make him ill. When he makes his life an offering for sin, he will see his offspring, he will prolong his days, and Yahweh's purpose will be accomplished through him.
11 Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
After the suffering of his life, he will see light and be satisfied by his knowledge. My righteous servant will justify many; he will bear their iniquities.
12 Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.
Therefore will I give him his portion among the multitudes, and he will divide the spoils with the many, because he exposed himself to death and was numbered with the transgressors. He bore the sin of many and made intercession for the transgressors.

< Yesaya 53 >