< Yesaya 53 >

1 Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
Hvo troede det, vi have hørt? og for hvem er Herrens Arm aabenbaret?
2 Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
Thi han skød frem som en Kvist for hans Ansigt og som et Rodskud af tør Jord, han havde ingen Skikkelse eller Herlighed; og vi saa ham, men der var ikke Anseelse, at vi kunde have Lyst til ham.
3 Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
Han var foragtet og ikke at regne iblandt Mænd, en Mand fuld af Pine og forsøgt i Sygdom; og som en, for hvem man skjuler Ansigtet, foragtet, og vi agtede ham for intet.
4 Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
Visselig, han har taget vore Sygdomme paa sig og baaret vore Smerter; men vi agtede ham for plaget, slagen af Gud og gjort elendig.
5 Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
Men han er saaret for vore Overtrædelser og knust for vore Misgerninger; Straffen er lagt paa ham, at vi skulle have Fred, og vi have faaet Lægedom ved hans Saar.
6 Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
Vi fore alle vild som Faar, vi vendte os hver sin Vej; men Herren lod al vor Misgerning komme over ham.
7 Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
Han blev trængt, og han blev gjort elendig, men han oplod ikke sin Mund, som et Lam, der føres hen at slagtes, og som et Faar, der er stumt over for dem, som klippe det; og han oplod ikke sin Mund.
8 Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
Fra Trængsel og fra Dom er han borttagen, og hvo kan tale om hans Slægt? thi han er bortreven fra de levendes Land, han havde Plage for mit Folks Overtrædelses Skyld.
9 Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
Og man gav ham hans Grav hos de ugudelige, og hos den rige i hans Død, uagtet han ikke havde gjort Uret, og der ikke var Svig i hans Mund.
10 Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
Men Herren havde Behag i at knuse ham med Sygdom; naar hans Sjæl har fuldbragt et Skyldoffer, skal han se Sæd og forlænge sine Dage; og Herrens Villie skal lykkes ved hans Haand.
11 Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
Fordi hans Sjæl har haft Møje, skal han se det, hvorved han skal mættes; naar han kendes, skal min retfærdige Tjener retfærdiggøre de mange; og han skal bære deres Misgerninger.
12 Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.
Derfor vil jeg give ham Del i de mange, og han skal dele de stærke som et Bytte, fordi han udtømte sin Sjæl til Døden og blev regnet iblandt Overtrædere; ja han har baaret manges Synd, og han skal bede for Overtrædere.

< Yesaya 53 >