< Yesaya 52 >
1 Dzambatuka, dzambatuka iwe Ziyoni, vala zilimbe. Vala zovala zako zokongola, iwe Yerusalemu, mzinda wopatulika. Pakuti kuyambira tsopano anthu osachita mdulidwe ndi odetsedwa sadzalowanso pa zipata zako.
Uyan, ey Siyon, uyan, kudretini kuşan. Ey Yeruşalim, kutsal kent, güzel giysilerini giy. Çünkü sünnetsizlerle murdarlar Kapılarından asla içeri girmeyecek artık.
2 Sasa fumbi lako; imirira nukhale pa mpando waufumu, iwe Yerusalemu. Inu omangidwa a ku Ziyoni, masulani maunyolo amene ali mʼkhosi mwanumo.
Üzerindeki tozu silk! Kalk, ey Yeruşalim, tahtına otur, Boynundaki zinciri çöz, Ey Siyon, tutsak kız.
3 Pakuti Yehova akuti, “Sindinalandirepo kanthu pamene ndinakugulitsani, choncho mudzawomboledwa wopanda ndalama.”
RAB diyor ki, “Karşılıksız satılmıştınız, Parasız kurtulacaksınız.”
4 Pakuti Ambuye Yehova akuti, “Poyamba paja anthu anga anapita kukakhala ku Igupto; nawonso Asiriya awapondereza popanda chifukwa.”
Egemen RAB diyor ki, “Halkım gurbette yaşamak için önce Mısır'a inmişti. Şimdi de Asurlular onları ezdi.
5 Tsopano Ine Yehova ndikuti, “Kodi nditani pakuti anthu anga atengedwa ukapolo osaperekapo kanthu, amene amawalamulira amawanyoza,” akutero Yehova. “Ndipo tsiku lonse, akungokhalira kuchita chipongwe dzina langa.
Halkım boş yere alınıp götürüldü, Benim burayla ne ilgim kaldı?” diyor RAB, “Yöneticileri feryat ediyor, Adıma günboyu sövülüyor” diyor RAB.
6 Tsono tsiku limenelo anthu anga adzadziwa dzina langa; kotero adzadziwa kuti ndi Ine amene ndikuyankhula, Indedi, ndine.”
“Bundan ötürü halkım adımı bilecek, O gün, ‘İşte ben’ diyenin ben olduğumu anlayacak.”
7 Ngokongoladi mapazi a amithenga obweretsa nkhani yabwino amene akuyenda pa mapiri. Iwo akukubweretserani nkhani zabwino za mtendere, chisangalalo ndi chipulumutso. Iwo akubwera kudzawuza anthu a ku Ziyoni kuti, “Mulungu wako ndi mfumu!”
Dağları aşıp gelen müjdecinin ayakları ne güzeldir! O müjdeci ki, esenlik duyuruyor. İyilik müjdesi getiriyor, kurtuluş haberi veriyor. Siyon halkına, “Tanrınız egemenlik sürüyor!” diye ilan ediyor.
8 Mverani! Alonda anu akukweza mawu awo; akuyimba pamodzi mwachimwemwe. Popeza akuona chamaso kubwera kwa Yehova ku Yerusalemu.
Dinleyin! Bekçileriniz seslerini yükseltiyor, Hep birlikte sevinçle haykırıyorlar. Çünkü RAB'bin Siyon'a dönüşünü gözleriyle görmekteler!
9 Imbani pamodzi mofuwula nyimbo zachimwemwe, inu mabwinja a Yerusalemu, pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, wapulumutsa Yerusalemu.
Ey Yeruşalim yıkıntıları, Hep birlikte sevinçle haykırıp bağırın! Çünkü RAB halkını avuttu, Yeruşalim'i kurtardı.
10 Yehova wagwiritsa ntchito mphamvu zake zopatulika pamaso pa anthu a mitundu yonse, ndipo anthu onse a dziko lapansi adzaona chipulumutso cha Mulungu wathu.
Bütün ulusların gözü önünde Kutsal kolunu sıvadı, Dünyanın dört bucağı Tanrımız'ın kurtarışını görecek.
11 Nyamukani, nyamukani, chokaniko ku Babuloniko! Musakhudze kanthu kodetsedwa! Inu amene mumanyamula ziwiya za Yehova tulukanimo ndipo mudziyeretse.
Çekilin, çekilin, oradan çıkın, Murdara dokunmayın. Oradan çıkıp temizlenin, Ey RAB'be tapınma araçlarını taşıyan sizler!
12 Koma simudzachoka mofulumira kapena kuchita chothawa; pakuti Yehova adzayenda patsogolo panu, Mulungu wa Israeli adzakutetezani kumbuyo kwanu.
Aceleyle çıkmayacak, Kaçıp gitmeyeceksiniz; Çünkü RAB önünüzden gidecek, İsrail'in Tanrısı artçınız olacak.
13 Taonani, mtumiki wanga adzapambana pa ntchito yake adzakwezedwa ndi kulemekezedwa ndipo adzalandira ulemu waukulu kwambiri.
Bakın, kulum başarılı olacak; Üstün olacak, el üstünde tutulup alabildiğine yüceltilecek.
14 Anthu ambiri atamuona anadzidzimuka, chifukwa nkhope yake inali itasakazika; sinalinso ngati ya munthu. Ndipo thupi lake linasakazika; silinalinso ngati la munthu.
Birçokları onun karşısında dehşete düşüyor; Biçimi, görünüşü öyle bozuldu ki, İnsana benzer yanı kalmadı;
15 Momwemonso anthu a mitundu yonse adzadodoma naye, ndipo mafumu adzatseka pakamwa pawo kusowa chonena chifukwa cha iye. Pakuti zinthu zimene iwo sanawuzidwepo, adzaziona, ndipo zimene sanazimvepo, adzazimvetsa.
Pek çok ulus ona şaşacak, Onun önünde kralların ağızları kapanacak. Çünkü kendilerine anlatılmamış olanı görecek, Duymadıklarını anlayacaklar.