< Yesaya 52 >

1 Dzambatuka, dzambatuka iwe Ziyoni, vala zilimbe. Vala zovala zako zokongola, iwe Yerusalemu, mzinda wopatulika. Pakuti kuyambira tsopano anthu osachita mdulidwe ndi odetsedwa sadzalowanso pa zipata zako.
Трезеште-те, трезеште-те! Ымбракэ-те ын подоаба та, Сиоане! Пуне-ць хайнеле де сэрбэтоаре, Иерусалиме, четате сфынтэ! Кэч ну ва май интра ын тине ничун ом нетэят ымпрежур сау некурат.
2 Sasa fumbi lako; imirira nukhale pa mpando waufumu, iwe Yerusalemu. Inu omangidwa a ku Ziyoni, masulani maunyolo amene ali mʼkhosi mwanumo.
Скутурэ-ць цэрына де пе тине, скоалэ-те ши шезь ын капул оаселор, Иерусалиме! Дезлягэ-ць легэтуриле де ла гыт, фийкэ, роабэ а Сионулуй!
3 Pakuti Yehova akuti, “Sindinalandirepo kanthu pamene ndinakugulitsani, choncho mudzawomboledwa wopanda ndalama.”
Кэч аша ворбеште Домнул: „Фэрэ платэ аць фост вындуць ши ну вець фи рэскумпэраць ку прец де арӂинт.”
4 Pakuti Ambuye Yehova akuti, “Poyamba paja anthu anga anapita kukakhala ku Igupto; nawonso Asiriya awapondereza popanda chifukwa.”
Кэч аша ворбеште Домнул Думнезеу: „Одиниоарэ, попорул Меу с-а коборыт сэ локуяскэ пентру о време ын Еӂипт, апой асириянул л-а асуприт фэрэ темей.
5 Tsopano Ine Yehova ndikuti, “Kodi nditani pakuti anthu anga atengedwa ukapolo osaperekapo kanthu, amene amawalamulira amawanyoza,” akutero Yehova. “Ndipo tsiku lonse, akungokhalira kuchita chipongwe dzina langa.
Ши акум, че ам сэ фак аич”, зиче Домнул, „кынд попорул Меу а фост луат пе нимик? Асуприторий луй стригэ де букурие”, зиче Домнул, „ши кыт е зиулика де маре есте батжокорит Нумеле Меу.
6 Tsono tsiku limenelo anthu anga adzadziwa dzina langa; kotero adzadziwa kuti ndi Ine amene ndikuyankhula, Indedi, ndine.”
Де ачея, попорул Меу ва куноаште Нумеле Меу, де ачея ва шти, ын зиуа ачея, кэ Еу ворбеск ши зик: ‘Ятэ-Мэ!’”
7 Ngokongoladi mapazi a amithenga obweretsa nkhani yabwino amene akuyenda pa mapiri. Iwo akukubweretserani nkhani zabwino za mtendere, chisangalalo ndi chipulumutso. Iwo akubwera kudzawuza anthu a ku Ziyoni kuti, “Mulungu wako ndi mfumu!”
Че фрумоасе сунт пе мунць пичоареле челуй че адуче вешть буне, каре вестеште пачя, пичоареле челуй че адуче вешть буне, каре вестеште мынтуиря, пичоареле челуй че зиче Сионулуй: „Думнезеул тэу ымпэрэцеште!”
8 Mverani! Alonda anu akukweza mawu awo; akuyimba pamodzi mwachimwemwe. Popeza akuona chamaso kubwera kwa Yehova ku Yerusalemu.
Ятэ, гласул стрэжерилор тэй рэсунэ; ей ыналцэ гласул ши стригэ тоць де веселие, кэч вэд ку окий лор кум Се ынтоарче Домнул ын Сион.
9 Imbani pamodzi mofuwula nyimbo zachimwemwe, inu mabwinja a Yerusalemu, pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, wapulumutsa Yerusalemu.
Избукниць ку тоате ын стригэте де букурие, дэрымэтурь але Иерусалимулуй! Кэч Домнул мынгые пе попорул Сэу ши рэскумпэрэ Иерусалимул.
10 Yehova wagwiritsa ntchito mphamvu zake zopatulika pamaso pa anthu a mitundu yonse, ndipo anthu onse a dziko lapansi adzaona chipulumutso cha Mulungu wathu.
Домнул Ышь дескоперэ брацул Сэу чел сфынт ынаинтя тутурор нямурилор ши тоате марӂиниле пэмынтулуй вор ведя мынтуиря Думнезеулуй ностру.
11 Nyamukani, nyamukani, chokaniko ku Babuloniko! Musakhudze kanthu kodetsedwa! Inu amene mumanyamula ziwiya za Yehova tulukanimo ndipo mudziyeretse.
Плекаць, плекаць, ешиць дин Бабилон! Ну вэ атинӂець де нимик некурат! Ешиць дин мижлокул луй! Курэцици-вэ, чей че пуртаць васеле Домнулуй!
12 Koma simudzachoka mofulumira kapena kuchita chothawa; pakuti Yehova adzayenda patsogolo panu, Mulungu wa Israeli adzakutetezani kumbuyo kwanu.
Ну ешиць ку грабэ, ну плекаць ын фугэ, кэч Домнул вэ ва еши ынаинте ши Думнезеул луй Исраел вэ ва тэя каля!
13 Taonani, mtumiki wanga adzapambana pa ntchito yake adzakwezedwa ndi kulemekezedwa ndipo adzalandira ulemu waukulu kwambiri.
„Ятэ, Робул Меу ва пропэши; Се ва суи, Се ва ридика, Се ва ынэлца фоарте сус.
14 Anthu ambiri atamuona anadzidzimuka, chifukwa nkhope yake inali itasakazika; sinalinso ngati ya munthu. Ndipo thupi lake linasakazika; silinalinso ngati la munthu.
Дупэ кум пентру мулць а фост о причинэ де гроазэ – атыт де скимоноситэ Ый ера фаца ши атыт де мулт се деосебя ынфэцишаря Луй де а фиилор оаменилор –,
15 Momwemonso anthu a mitundu yonse adzadodoma naye, ndipo mafumu adzatseka pakamwa pawo kusowa chonena chifukwa cha iye. Pakuti zinthu zimene iwo sanawuzidwepo, adzaziona, ndipo zimene sanazimvepo, adzazimvetsa.
тот аша, пентру мулте попоаре ва фи о причинэ де букурие; ынаинтя Луй, ымпэраций вор ынкиде гура, кэч вор ведя че ну ли се май историсисе ши вор аузи че ну май аузисерэ.”

< Yesaya 52 >