< Yesaya 52 >
1 Dzambatuka, dzambatuka iwe Ziyoni, vala zilimbe. Vala zovala zako zokongola, iwe Yerusalemu, mzinda wopatulika. Pakuti kuyambira tsopano anthu osachita mdulidwe ndi odetsedwa sadzalowanso pa zipata zako.
Despertai, despertai! Ponha suas forças, Zion. Vista suas belas vestes, Jerusalém, a cidade santa, pois de agora em diante os incircuncisos e os impuros não mais entrarão em você.
2 Sasa fumbi lako; imirira nukhale pa mpando waufumu, iwe Yerusalemu. Inu omangidwa a ku Ziyoni, masulani maunyolo amene ali mʼkhosi mwanumo.
Sacuda-se do pó! Levante-se, sente-se, Jerusalém! Liberte-se dos laços de seu pescoço, filha cativa de Zion!
3 Pakuti Yehova akuti, “Sindinalandirepo kanthu pamene ndinakugulitsani, choncho mudzawomboledwa wopanda ndalama.”
Para Yahweh diz: “Você foi vendido por nada; e você será resgatado sem dinheiro”.
4 Pakuti Ambuye Yehova akuti, “Poyamba paja anthu anga anapita kukakhala ku Igupto; nawonso Asiriya awapondereza popanda chifukwa.”
Para o Senhor Yahweh diz: “Meu povo desceu pela primeira vez ao Egito para viver lá; e o assírio os oprimiu sem causa.
5 Tsopano Ine Yehova ndikuti, “Kodi nditani pakuti anthu anga atengedwa ukapolo osaperekapo kanthu, amene amawalamulira amawanyoza,” akutero Yehova. “Ndipo tsiku lonse, akungokhalira kuchita chipongwe dzina langa.
“Agora, portanto, o que eu faço aqui”, diz Yahweh, “vendo que meu povo é levado para nada? Aqueles que governam sobre eles zombam”, diz Yahweh, “e meu nome é blasfemado continuamente durante todo o dia”.
6 Tsono tsiku limenelo anthu anga adzadziwa dzina langa; kotero adzadziwa kuti ndi Ine amene ndikuyankhula, Indedi, ndine.”
Portanto, meu povo deve saber meu nome. Portanto, eles saberão naquele dia que eu sou aquele que fala. Eis que sou eu”.
7 Ngokongoladi mapazi a amithenga obweretsa nkhani yabwino amene akuyenda pa mapiri. Iwo akukubweretserani nkhani zabwino za mtendere, chisangalalo ndi chipulumutso. Iwo akubwera kudzawuza anthu a ku Ziyoni kuti, “Mulungu wako ndi mfumu!”
Como são bonitos nas montanhas os pés daquele que traz boas notícias, que publica a paz, que traz boas notícias, que proclama a salvação, que diz a Sião: “Seu Deus reina!”
8 Mverani! Alonda anu akukweza mawu awo; akuyimba pamodzi mwachimwemwe. Popeza akuona chamaso kubwera kwa Yehova ku Yerusalemu.
Seus vigilantes levantam sua voz. Juntos eles cantam; pois eles estarão de acordo quando Yahweh retornar a Zion.
9 Imbani pamodzi mofuwula nyimbo zachimwemwe, inu mabwinja a Yerusalemu, pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, wapulumutsa Yerusalemu.
Entre na alegria! Cantem juntos, vocês desperdiçam lugares de Jerusalém; pois Yahweh tem confortado seu povo. Ele resgatou Jerusalém.
10 Yehova wagwiritsa ntchito mphamvu zake zopatulika pamaso pa anthu a mitundu yonse, ndipo anthu onse a dziko lapansi adzaona chipulumutso cha Mulungu wathu.
Yahweh fez seu braço sagrado ficar nu aos olhos de todas as nações. Todos os confins da Terra viram a salvação de nosso Deus.
11 Nyamukani, nyamukani, chokaniko ku Babuloniko! Musakhudze kanthu kodetsedwa! Inu amene mumanyamula ziwiya za Yehova tulukanimo ndipo mudziyeretse.
Partida! Partida! Saia de lá! Não toque em nada impuro! Saia do meio dela! Limpem-se, vocês que carregam as embarcações de Yahweh.
12 Koma simudzachoka mofulumira kapena kuchita chothawa; pakuti Yehova adzayenda patsogolo panu, Mulungu wa Israeli adzakutetezani kumbuyo kwanu.
Para você não deve sair à pressa, também não deve ir de avião; para Yahweh irá antes de você, e o Deus de Israel será sua retaguarda.
13 Taonani, mtumiki wanga adzapambana pa ntchito yake adzakwezedwa ndi kulemekezedwa ndipo adzalandira ulemu waukulu kwambiri.
Eis que meu servo tratará sabiamente. Ele será exaltado e erguido, e será muito alto.
14 Anthu ambiri atamuona anadzidzimuka, chifukwa nkhope yake inali itasakazika; sinalinso ngati ya munthu. Ndipo thupi lake linasakazika; silinalinso ngati la munthu.
Muitos também ficaram surpresos com você. sua aparência foi prejudicada mais do que qualquer homem, e sua forma mais do que os filhos dos homens...
15 Momwemonso anthu a mitundu yonse adzadodoma naye, ndipo mafumu adzatseka pakamwa pawo kusowa chonena chifukwa cha iye. Pakuti zinthu zimene iwo sanawuzidwepo, adzaziona, ndipo zimene sanazimvepo, adzazimvetsa.
para que ele limpe muitas nações. Os reis vão fechar a boca para ele; pois eles verão o que não lhes havia sido dito, e eles entenderão o que não tinham ouvido.