< Yesaya 52 >

1 Dzambatuka, dzambatuka iwe Ziyoni, vala zilimbe. Vala zovala zako zokongola, iwe Yerusalemu, mzinda wopatulika. Pakuti kuyambira tsopano anthu osachita mdulidwe ndi odetsedwa sadzalowanso pa zipata zako.
Awake, awake, put on thy strength, O Zion; put on thy beautiful garments, O Jerusalem, thou holy city; for no more shall enter into thee henceforth the uncircumcised and the unclean.
2 Sasa fumbi lako; imirira nukhale pa mpando waufumu, iwe Yerusalemu. Inu omangidwa a ku Ziyoni, masulani maunyolo amene ali mʼkhosi mwanumo.
Shake thyself free from the dust, arise, sit down, O Jerusalem: loosen thyself from the bands of thy neck, O captive, daughter of Zion.
3 Pakuti Yehova akuti, “Sindinalandirepo kanthu pamene ndinakugulitsani, choncho mudzawomboledwa wopanda ndalama.”
For thus hath said the Lord, For naught were you sold, and without silver shall ye be redeemed.
4 Pakuti Ambuye Yehova akuti, “Poyamba paja anthu anga anapita kukakhala ku Igupto; nawonso Asiriya awapondereza popanda chifukwa.”
For thus hath said the Lord Eternal, Into Egypt went my people down aforetimes, to sojourn there, and Asshur hath oppressed it without cause.
5 Tsopano Ine Yehova ndikuti, “Kodi nditani pakuti anthu anga atengedwa ukapolo osaperekapo kanthu, amene amawalamulira amawanyoza,” akutero Yehova. “Ndipo tsiku lonse, akungokhalira kuchita chipongwe dzina langa.
And now what have I here, saith the Lord, since my people hath been taken away for naught? its rulers vaunt aloud, saith the Lord, and continually, all the day, is my name blasphemed.
6 Tsono tsiku limenelo anthu anga adzadziwa dzina langa; kotero adzadziwa kuti ndi Ine amene ndikuyankhula, Indedi, ndine.”
Therefore shall my people know my name, therefore on that day, that I am he that speaketh it: here am I.
7 Ngokongoladi mapazi a amithenga obweretsa nkhani yabwino amene akuyenda pa mapiri. Iwo akukubweretserani nkhani zabwino za mtendere, chisangalalo ndi chipulumutso. Iwo akubwera kudzawuza anthu a ku Ziyoni kuti, “Mulungu wako ndi mfumu!”
How beautiful are upon the mountains the feet of the messenger of good tidings, that publisheth peace, that announceth tidings of happiness, that publisheth salvation, that saith unto Zion, Thy God reigneth.
8 Mverani! Alonda anu akukweza mawu awo; akuyimba pamodzi mwachimwemwe. Popeza akuona chamaso kubwera kwa Yehova ku Yerusalemu.
The voice of thy watchmen, —they raise their voice, together shall they shout; for eye to eye shall they see, when the Lord returneth unto Zion.
9 Imbani pamodzi mofuwula nyimbo zachimwemwe, inu mabwinja a Yerusalemu, pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, wapulumutsa Yerusalemu.
Break forth [in song], shout together, ye ruins of Jerusalem; the Lord hath comforted his people, he hath redeemed Jerusalem.
10 Yehova wagwiritsa ntchito mphamvu zake zopatulika pamaso pa anthu a mitundu yonse, ndipo anthu onse a dziko lapansi adzaona chipulumutso cha Mulungu wathu.
The Lord hath made bare his holy arm before the eyes of all the nations; and all the ends of the earth shall see the salvation of our God.
11 Nyamukani, nyamukani, chokaniko ku Babuloniko! Musakhudze kanthu kodetsedwa! Inu amene mumanyamula ziwiya za Yehova tulukanimo ndipo mudziyeretse.
Depart ye, depart ye, go out from there, touch no unclean thing; go ye out from the midst of it; cleanse yourselves, ye bearers of the vessels of the Lord.
12 Koma simudzachoka mofulumira kapena kuchita chothawa; pakuti Yehova adzayenda patsogolo panu, Mulungu wa Israeli adzakutetezani kumbuyo kwanu.
Not in haste shall ye go out, and not in flight shall ye go; for before you goeth the Lord, and your rereward is the God of Israel.
13 Taonani, mtumiki wanga adzapambana pa ntchito yake adzakwezedwa ndi kulemekezedwa ndipo adzalandira ulemu waukulu kwambiri.
Behold, my servant shall be prosperous, he shall be exalted and extolled, and be placed very high.
14 Anthu ambiri atamuona anadzidzimuka, chifukwa nkhope yake inali itasakazika; sinalinso ngati ya munthu. Ndipo thupi lake linasakazika; silinalinso ngati la munthu.
Just as many were astonished at thee, so greatly was his countenance marred more than any [other] man's, and his form more than [that of] the sons of men, —
15 Momwemonso anthu a mitundu yonse adzadodoma naye, ndipo mafumu adzatseka pakamwa pawo kusowa chonena chifukwa cha iye. Pakuti zinthu zimene iwo sanawuzidwepo, adzaziona, ndipo zimene sanazimvepo, adzazimvetsa.
Thus will he cause many nations to jump up in [astonishment]; at him will kings shut their mouth; for what had not been told unto them shall they see, and what they had never heard shall they understand.

< Yesaya 52 >