< Yesaya 51 >

1 “Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso ndiponso amene mumafunafuna Yehova: Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;
Hörer mig, I som efter rättfärdighet faren, I som Herran söken; ser uppå klippona, dädan I afhuggne ären, och uppå brunnsgropena, dädan I utgrafne ären.
2 taganizani za Abrahamu, kholo lanu, ndi Sara, amene anakubalani. Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana, koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.
Ser uppå Abraham, edar fader, och Sara, den eder födt hafver; ty jag kallade honom, då han ännu ensam var, och välsignade honom, och förmerade honom.
3 Yehova adzatonthozadi Ziyoni, ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse; Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni, malo ake owuma ngati munda wa Yehova. Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda ndi kundiyamika.
Ty Herren hugsvalar Zion, han tröster all dess öde, och gör dess öde såsom lustgårdar, och dess hedmark såsom en Herrans örtegård; glädje och fröjd skall man finna derinne, tack och lofsång.
4 “Mverani Ine, anthu anga: tcherani khutu, inu mtundu wanga: malangizo adzachokera kwa Ine; cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.
Gifver akt uppå mig, mitt folk, och hörer mig, min allmoge; ty af mig skall utgå en lag, och min rätt vill jag sätta folkom till ljus.
5 Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga. Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga; ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse. Mayiko akutali akundiyembekezera. Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.
Ty min rättfärdighet är när; min salighet drager ut, och mina armar skola döma folken; öarna förbida mig, och vakta uppå min arm.
6 Kwezani maso anu mlengalenga, yangʼanani pansi pa dziko; mlengalenga udzazimirira ngati utsi, dziko lapansi lidzatha ngati chovala ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe. Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya, chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.
Lyfter edor ögon upp till himmelen, och skåder neder uppå jordena; ty himmelen skall förgås såsom en rök, och jorden föråldras såsom ett kläde, och de som bo deruppå skola dö bort, såsom detta; men min salighet blifver evinnerliga, och min rättfärdighet skall icke återvända.
7 “Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi, anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu; musaope kudzudzulidwa ndi anthu kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.
Hörer mig, I som kännen rättfärdighetena, du folk i hvilkets hjerta min lag är; frukter eder intet, när menniskorna försmäda eder, och gifver eder icke, när de förhäda eder.
8 Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala; mbozi idzawadya ngati thonje. Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya, chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”
Ty mal skall uppäta dem såsom ett kläde, och matkar skola äta dem såsom ull; men min rättfärdighet blifver evinnerliga, och min salighet förutan ända.
9 Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe, Inu Yehova; dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana, monga nthawi ya mibado yakale. Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe, amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
Upp, upp, kläd dig i starkhet, du Herrans arm; upp, såsom i förtiden af ålder. Äst icke du den som de högmodiga slagit, och drakan sargat hafver?
10 Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu, madzi ozama kwambiri aja? Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama, kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?
Äst icke du den som uttorkade hafvet, det djupa vattnet; den som gjorde hafsbottnen till en väg, så att de förlossade gingo derigenom?
11 Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa; chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo. Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe, chisoni ndi kubuwula zidzathawa.
Alltså; skola Herrans förlossade vända om, och komma till Zion med fröjd, och evig glädje skall vara på deras hufvud; glädje och fröjd skall fatta dem, sorg och suckan skall ifrå dem fly.
12 Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima. Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa? Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.
Jag, Jag är edar tröstare. Ho äst du då, att du fruktar dig för menniskor, de dock dö, och för menniskobarn, hvilke såsom hö förtärde varda;
13 Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu, amene anayala za mlengalenga ndi kuyika maziko a dziko lapansi. Inu nthawi zonse mumaopsezedwa chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani amene angofuna kukuwonongani. Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?
Och förgäter Herran, den dig gjort hafver, den der himmelen utsträcker, och jordena grundar? Men du fruktar dig alltid hela dagen för plågarens grymhet, då han tager till att förderfva. Hvar blef plågarens grymhet,
14 Amʼndende adzamasulidwa posachedwa; sadzalowa mʼmanda awo, kapena kusowa chakudya.
Då han måste hasta sig och löpa omkring, att han skulle lös gifva, och de icke döde blefvo i förderfvelsen, ej heller någon brist på bröd hade?
15 Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Ty jag är Herren din Gud, den der hafvet rörer, så att dess böljor fräsa. Hans Namn heter Herren Zebaoth.
16 Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa. Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga, ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi, ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’”
Jag sätter min ord uti din mun, och öfvertäcker dig under mina händers skugga, på det jag skall plantera himmelen och grunda jordena, och säga till Zion: Du äst mitt folk.
17 Dzambatuka, dzambatuka! Imirira iwe Yerusalemu. Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo chimene Yehova anakupatsa. Iwe amene unagugudiza chikho chochititsa chizwezwe.
Vaka upp, vaka, upp, statt upp, Jerusalem, du som af Herrans hand hans grymhets kalk druckit hafver; dräggen af dvalakalken hafver du utdruckit, och uppslekt dropparna.
18 Mwa ana onse amene anabereka, panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera; mwa ana onse amene analera, panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.
Det var ingen af all de barn, som hon födt hade, som henne ledde; ingen af all de barn, de hon uppfödt hade, som henne vid handena tog.
19 Mavuto awiriwa akugwera iwe. Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga. Ndani angakumvere chisoni? Ndani angakutonthoze?
Desse tu stycke äro dig påkomne; ho ömkade sig öfver dig? Förstöring, skade, hunger och svärd var der; ho skulle hugsvala dig?
20 Ana ako akomoka; ali lambalamba pa msewu, ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde. Ukali wa Yehova ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.
Din barn voro försmäktade, de lågo på alla gator, såsom en besnärd skogsoxe; fulle med vrede af Herranom, och med straff af dinom Gud.
21 Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika, iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.
Derföre hör detta, du elända, och druckna utan vin.
22 Ambuye Yehova wanu, Mulungu amene amateteza anthu ake akuti, “Taona, ndachotsa mʼdzanja lako chikho chimene chimakuchititsa kudzandira; sudzamwanso chikho cha ukali wanga.
Så säger den som råder öfver dig, Herren, och din Gud, den sitt folk hämnas: Si, jag tager den dvalakalken utu dine hand, samt med dräggene af mine vredes kalk, du skall icke mer dricka honom;
23 Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza, amene ankakuwuza kuti, ‘gona pansi tikuyende pa msana.’ Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo, ngati msewu woti ayendepo.”
Utan jag skall få honom dina plågare i handena, de som till dina själ sade: Bocka dig, att vi måge gå öfver dig, och lägg din rygg på jordena, och som ena gato, att man må löpa deröfver.

< Yesaya 51 >