< Yesaya 51 >

1 “Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso ndiponso amene mumafunafuna Yehova: Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;
“Escúchame, tú que sigues la justicia, vosotros que buscáis a Yahvé. Mira a la roca de la que fuiste cortado, y a la cantera de la que fuiste excavado.
2 taganizani za Abrahamu, kholo lanu, ndi Sara, amene anakubalani. Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana, koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.
Mira a Abraham, tu padre, y a Sarah que te parió; ya que cuando no era más que uno le llamé, Lo bendije, y le hizo muchos.
3 Yehova adzatonthozadi Ziyoni, ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse; Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni, malo ake owuma ngati munda wa Yehova. Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda ndi kundiyamika.
Porque Yahvé ha consolado a Sión. Él ha reconfortado todos sus lugares de desecho, y ha hecho que su desierto sea como el Edén, y su desierto como el jardín de Yahvé. La alegría y el gozo se encontrarán en ellos, acción de gracias, y la voz de la melodía.
4 “Mverani Ine, anthu anga: tcherani khutu, inu mtundu wanga: malangizo adzachokera kwa Ine; cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.
“Escuchadme, pueblo mío; y escuchadme, nación mía, porque una ley saldrá de mí, y estableceré mi justicia para luz de los pueblos.
5 Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga. Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga; ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse. Mayiko akutali akundiyembekezera. Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.
Mi justicia está cerca. Mi salvación se ha apagado, y mis brazos juzgarán a los pueblos. Las islas me esperarán, y confiarán en mi brazo.
6 Kwezani maso anu mlengalenga, yangʼanani pansi pa dziko; mlengalenga udzazimirira ngati utsi, dziko lapansi lidzatha ngati chovala ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe. Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya, chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.
Alza tus ojos al cielo, y mira la tierra que hay debajo; porque los cielos se desvanecerán como el humo, y la tierra se desgastará como un vestido. Sus habitantes morirán de la misma manera, pero mi salvación será para siempre, y mi justicia no será abolida.
7 “Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi, anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu; musaope kudzudzulidwa ndi anthu kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.
“Escúchame, tú que conoces la justicia, el pueblo en cuyo corazón está mi ley. No temas el reproche de los hombres, y no te desanimes por sus insultos.
8 Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala; mbozi idzawadya ngati thonje. Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya, chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”
Porque la polilla se los comerá como un vestido, y el gusano los comerá como si fueran lana; pero mi justicia será para siempre, y mi salvación para todas las generaciones”.
9 Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe, Inu Yehova; dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana, monga nthawi ya mibado yakale. Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe, amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
¡Despierta, despierta, ponte fuerte, brazo de Yahvé! Despierta, como en los viejos tiempos, las generaciones de la antigüedad. ¿No fuiste tú quien cortó en pedazos a Rahab? ¿quién perforó al monstruo?
10 Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu, madzi ozama kwambiri aja? Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama, kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?
¿No fuiste tú quien secó el mar? las aguas de las grandes profundidades; ¿quién hizo de las profundidades del mar un camino para que pasaran los redimidos?
11 Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa; chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo. Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe, chisoni ndi kubuwula zidzathawa.
Los rescatados por Yahvé volverán, y venir con el canto a Sión. La alegría eterna estará sobre sus cabezas. Obtendrán alegría y gozo. La pena y el suspiro huirán.
12 Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima. Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa? Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.
“Yo, yo mismo, soy el que te consuela. ¿Quiénes sois vosotros, que tenéis miedo del hombre que va a morir? y del hijo del hombre que será hecho como hierba?
13 Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu, amene anayala za mlengalenga ndi kuyika maziko a dziko lapansi. Inu nthawi zonse mumaopsezedwa chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani amene angofuna kukuwonongani. Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?
¿Has olvidado a Yahvé, tu Hacedor? que extendió los cielos, y puso los cimientos de la tierra? ¿Vives continuamente con miedo por la furia del opresor? cuando se prepara para destruir? ¿Dónde está la furia del opresor?
14 Amʼndende adzamasulidwa posachedwa; sadzalowa mʼmanda awo, kapena kusowa chakudya.
El exiliado cautivo será liberado rápidamente. No morirá y bajará a la fosa. Su pan no fallará.
15 Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Porque yo soy Yahvé, tu Dios, que agita el mar de modo que sus olas rugen. Yahvé de los Ejércitos es su nombre.
16 Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa. Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga, ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi, ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’”
He puesto mis palabras en tu boca y te he cubierto con la sombra de mi mano, para plantar los cielos, y poner los cimientos de la tierra, y dile a Sión: ‘Tú eres mi pueblo’”.
17 Dzambatuka, dzambatuka! Imirira iwe Yerusalemu. Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo chimene Yehova anakupatsa. Iwe amene unagugudiza chikho chochititsa chizwezwe.
¡Despierta, despierta! Levántate, Jerusalén, tú que has bebido de la mano de Yahvé el cáliz de su ira. Te has bebido el cuenco de la copa del tambaleo, y lo escurrió.
18 Mwa ana onse amene anabereka, panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera; mwa ana onse amene analera, panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.
No hay nadie que la guíe entre todos los hijos que ha dado a luz; y no hay nadie que la tome de la mano entre todos los hijos que ha criado.
19 Mavuto awiriwa akugwera iwe. Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga. Ndani angakumvere chisoni? Ndani angakutonthoze?
Estas dos cosas te han sucedido... ¿quién se afligirá contigo? desolación y destrucción, y el hambre y la espada. ¿Cómo puedo consolarte?
20 Ana ako akomoka; ali lambalamba pa msewu, ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde. Ukali wa Yehova ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.
Tus hijos se han desmayado. Están a la cabeza de todas las calles, como un antílope en una red. Están llenos de la ira de Yahvé, la reprimenda de tu Dios.
21 Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika, iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.
Por lo tanto, escuchad ahora esto, afligidos, y borracho, pero no con vino:
22 Ambuye Yehova wanu, Mulungu amene amateteza anthu ake akuti, “Taona, ndachotsa mʼdzanja lako chikho chimene chimakuchititsa kudzandira; sudzamwanso chikho cha ukali wanga.
Tu Señor Yahvé, tu Dios que defiende la causa de su pueblo, dice, “He aquí que he quitado de tu mano el cáliz del tambaleo, hasta el cuenco de la copa de mi ira. No lo beberás más.
23 Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza, amene ankakuwuza kuti, ‘gona pansi tikuyende pa msana.’ Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo, ngati msewu woti ayendepo.”
La pondré en manos de los que te afligen, que han dicho a tu alma: “Inclínate, para que caminemos sobre ti”. y has puesto tu espalda como el suelo, como una calle para los que pasan por encima”.

< Yesaya 51 >