< Yesaya 51 >

1 “Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso ndiponso amene mumafunafuna Yehova: Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;
“Ouçam-me, vocês que seguem a retidão, você que procura Yahweh. Olhe para a rocha de onde você foi cortado, e para a pedreira de onde você foi escavado.
2 taganizani za Abrahamu, kholo lanu, ndi Sara, amene anakubalani. Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana, koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.
Olhe para Abraham, seu pai, e a Sarah, que o aborreceu; para quando ele era apenas um, eu o chamei, Eu o abençoei, e fez dele muitos.
3 Yehova adzatonthozadi Ziyoni, ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse; Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni, malo ake owuma ngati munda wa Yehova. Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda ndi kundiyamika.
Pois Yahweh tem confortado Zion. Ele tem confortado todos os seus lugares de desperdício, e fez dela um lugar selvagem como o Éden, e seu deserto como o jardim de Yahweh. Alegria e alegria serão encontradas neles, ação de graças, e a voz da melodia.
4 “Mverani Ine, anthu anga: tcherani khutu, inu mtundu wanga: malangizo adzachokera kwa Ine; cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.
“Ouçam-me, meu povo; e me ouçam, minha nação, por uma lei sairá de mim, e estabelecerei minha justiça por uma luz para os povos.
5 Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga. Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga; ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse. Mayiko akutali akundiyembekezera. Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.
Minha retidão está próxima. Minha salvação se apagou, e meus braços irão julgar os povos. As ilhas me aguardarão, e eles vão confiar em meu braço.
6 Kwezani maso anu mlengalenga, yangʼanani pansi pa dziko; mlengalenga udzazimirira ngati utsi, dziko lapansi lidzatha ngati chovala ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe. Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya, chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.
Levantem seus olhos para o céu, e olhe para a terra por baixo; pois os céus desaparecerão como fumaça, e a terra vai se desgastar como uma peça de vestuário. Seus habitantes morrerão da mesma forma, mas minha salvação será para sempre, e minha retidão não será abolida.
7 “Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi, anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu; musaope kudzudzulidwa ndi anthu kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.
“Ouçam-me, vocês que conhecem a retidão, as pessoas em cujo coração está minha lei. Não tenha medo da reprovação dos homens, e não fiquem consternados com seus insultos.
8 Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala; mbozi idzawadya ngati thonje. Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya, chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”
Pois a traça vai comê-los como uma peça de vestuário, e a minhoca os comerá como lã; mas minha retidão será para sempre, e minha salvação para todas as gerações”.
9 Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe, Inu Yehova; dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana, monga nthawi ya mibado yakale. Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe, amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
Desperta, desperta, coloca força, braço de Yahweh! Desperta, como nos velhos tempos, as gerações dos tempos antigos. Não foi você quem cortou a Rahab em pedaços? quem furou o monstro?
10 Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu, madzi ozama kwambiri aja? Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama, kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?
Não foi você quem secou o mar, as águas das grandes profundezas; quem fez das profundezas do mar uma forma de passar os redimidos?
11 Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa; chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo. Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe, chisoni ndi kubuwula zidzathawa.
Os resgatados por Iavé voltarão, e vêm com cânticos para Zion. A alegria eterna estará em suas cabeças. Eles obterão alegria e alegria. A dor e o suspiro devem fugir.
12 Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima. Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa? Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.
“Eu, até mesmo eu, sou aquele que vos conforta. Quem é você, que tem medo do homem que deve morrer, e do filho do homem que será feito de grama?
13 Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu, amene anayala za mlengalenga ndi kuyika maziko a dziko lapansi. Inu nthawi zonse mumaopsezedwa chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani amene angofuna kukuwonongani. Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?
Você esqueceu Yahweh, seu Criador, que estendia os céus, e lançou os alicerces da terra? Você vive com medo continuamente o dia todo por causa da fúria do opressor, quando ele se prepara para destruir? Onde está a fúria do opressor?
14 Amʼndende adzamasulidwa posachedwa; sadzalowa mʼmanda awo, kapena kusowa chakudya.
O exílio cativo será rapidamente libertado. Ele não morrerá e descerá para o poço. Seu pão não falhará.
15 Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Pois eu sou Yahweh, vosso Deus, que agita o mar para que suas ondas rugam. Yahweh dos Exércitos é seu nome.
16 Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa. Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga, ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi, ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’”
Coloquei minhas palavras em sua boca e o cobri na sombra da minha mão, que eu possa plantar os céus, e lançar os alicerces da terra, e dizer a Zion, 'Vocês são meu povo'”.
17 Dzambatuka, dzambatuka! Imirira iwe Yerusalemu. Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo chimene Yehova anakupatsa. Iwe amene unagugudiza chikho chochititsa chizwezwe.
Despertai, despertai! Levante-se, Jerusalém, você que bebeu da mão de Yahweh o cálice de sua ira. Você bebeu a taça do copo de cambaleio, e o drenou.
18 Mwa ana onse amene anabereka, panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera; mwa ana onse amene analera, panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.
Não há ninguém que a guie entre todos os filhos aos quais ela deu à luz; e não há ninguém que a pegue pela mão entre todos os filhos que ela educou.
19 Mavuto awiriwa akugwera iwe. Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga. Ndani angakumvere chisoni? Ndani angakutonthoze?
Estas duas coisas aconteceram com você... quem vai sofrer com você... desolação e destruição, e a fome e a espada. Como posso confortá-lo?
20 Ana ako akomoka; ali lambalamba pa msewu, ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde. Ukali wa Yehova ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.
Seus filhos desmaiaram. Eles estão à frente de todas as ruas, como um antílope em uma rede. Eles estão cheios da ira de Yahweh, a repreensão de seu Deus.
21 Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika, iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.
Portanto, agora ouçam isto, vocês afligiram, e embriagado, mas não com vinho:
22 Ambuye Yehova wanu, Mulungu amene amateteza anthu ake akuti, “Taona, ndachotsa mʼdzanja lako chikho chimene chimakuchititsa kudzandira; sudzamwanso chikho cha ukali wanga.
Vossa Senhoria Yahweh, seu Deus que pleiteia a causa de seu povo, diz, “Eis que eu tirei de sua mão o cálice do cambaleio”, até mesmo a taça da taça da minha ira. Você não vai beber mais.
23 Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza, amene ankakuwuza kuti, ‘gona pansi tikuyende pa msana.’ Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo, ngati msewu woti ayendepo.”
Vou colocá-lo na mão daqueles que o afligem, que disseram à sua alma: “Curve-se, para que possamos caminhar sobre você; e você se deitou de costas como o chão, como uma rua para aqueles que passam por cima”.

< Yesaya 51 >