< Yesaya 51 >
1 “Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso ndiponso amene mumafunafuna Yehova: Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;
Hearken to me, ye that pursue righteousness, that seek the Lord: look unto the rock whence ye were hewn, and to the hole of the pit whence ye were dug up.
2 taganizani za Abrahamu, kholo lanu, ndi Sara, amene anakubalani. Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana, koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.
Look unto Abraham your father, and unto Sarah that bore you; for he was one when I called him, and I blessed him, and I increased him.
3 Yehova adzatonthozadi Ziyoni, ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse; Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni, malo ake owuma ngati munda wa Yehova. Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda ndi kundiyamika.
Yea, the Lord hath comforted Zion; he hath comforted all her ruins; and he hath made her wilderness like Eden, and her desert like the garden of the Lord: gladness and joy shall be found therein, thanksgiving, and the voice of song.
4 “Mverani Ine, anthu anga: tcherani khutu, inu mtundu wanga: malangizo adzachokera kwa Ine; cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.
Listen unto me, my people; and O my nation, give ear unto me; for a law shall proceed from me, and my justice will I establish as a light of the people.
5 Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga. Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga; ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse. Mayiko akutali akundiyembekezera. Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.
My righteousness is near; my salvation goeth forth, and my arms shall judge the people: on me the isles shall wait, and for my arm shall they hope.
6 Kwezani maso anu mlengalenga, yangʼanani pansi pa dziko; mlengalenga udzazimirira ngati utsi, dziko lapansi lidzatha ngati chovala ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe. Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya, chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.
Lift up your eyes to the heavens, and look upon the earth beneath; for the heavens shall vanish away like smoke, and the earth shall wear out like a garment, and they that dwell thereon shall die in like manner; but my salvation shall exist for ever, and my righteousness shall not be delayed.
7 “Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi, anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu; musaope kudzudzulidwa ndi anthu kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.
Hearken unto me, ye that know righteousness, O people in whose heart my law is: ye must not fear the reproach of men, and of their revilings shall ye not be in dread.
8 Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala; mbozi idzawadya ngati thonje. Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya, chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”
For like a garment shall the moth eat them up, and like wool shall the worm eat them; but my righteousness shall exist for ever, and my salvation from generation to generation.
9 Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe, Inu Yehova; dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana, monga nthawi ya mibado yakale. Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe, amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
Awake, awake, put on strength, O arm of the Lord: awake, as in the ancient days, in the generations of olden times. Art thou not it that struck down Rahab, that pierced the crocodile?
10 Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu, madzi ozama kwambiri aja? Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama, kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?
Art thou not it that dried up the sea, the waters of the great deep; that rendered the depths of the sea a road for the redeemed to pass through?
11 Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa; chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo. Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe, chisoni ndi kubuwula zidzathawa.
And [so] shall the ransomed of the Lord return, and come to Zion with song, with everlasting joy upon their head; gladness and joy shall they obtain, while sorrow and sighing shall have fled away.
12 Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima. Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa? Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.
I, I am he that comforteth you: who art thou, that thou shouldst be afraid of a mortal that must die, and of a son of man who will wither as the grass?
13 Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu, amene anayala za mlengalenga ndi kuyika maziko a dziko lapansi. Inu nthawi zonse mumaopsezedwa chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani amene angofuna kukuwonongani. Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?
And thou forgettest the Lord, thy Maker, who hath spread out the heavens, and laid the foundations of the earth; and thou dreadest continually, all the day, because of the fury of the oppressor, whenever he aimeth to destroy: and where is [now] the fury of the oppressor?
14 Amʼndende adzamasulidwa posachedwa; sadzalowa mʼmanda awo, kapena kusowa chakudya.
The exile will be speedily set free; and he shall not die in the dungeon, and his bread shall not fail.
15 Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
For I am the Lord thy God, who stirreth up the sea that its waves roar: the Lord of hosts is his name.
16 Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa. Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga, ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi, ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’”
And I have placed my words in thy mouth, and with the shadow of my hand have I covered thee: to plant the heavens, and to lay the foundations of the earth, and to say to Zion, Thou art my people.
17 Dzambatuka, dzambatuka! Imirira iwe Yerusalemu. Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo chimene Yehova anakupatsa. Iwe amene unagugudiza chikho chochititsa chizwezwe.
Rouse up, rouse up, arise, O Jerusalem, thou who hast drunk from the hand of the Lord the cup of his fury: the deep cup of confusion hast thou drunk, hast thou drained.
18 Mwa ana onse amene anabereka, panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera; mwa ana onse amene analera, panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.
There is none to lead her, from all the children whom she hath born; and there is none that taketh her by the hand, from all the children whom she hath brought up.
19 Mavuto awiriwa akugwera iwe. Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga. Ndani angakumvere chisoni? Ndani angakutonthoze?
Two things are these which have befallen thee: who will have compassion for thee? desolation and destruction, and famine and sword—with whom shall I comfort thee?
20 Ana ako akomoka; ali lambalamba pa msewu, ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde. Ukali wa Yehova ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.
Thy children have fainted, they lie at the entrance of all streets, as a wild bull caught in a net, [they are those] who are full of the fury of the Lord, the threatening of thy God.
21 Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika, iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.
Therefore hear now this, O thou afflicted, and drunken, but not with wine.
22 Ambuye Yehova wanu, Mulungu amene amateteza anthu ake akuti, “Taona, ndachotsa mʼdzanja lako chikho chimene chimakuchititsa kudzandira; sudzamwanso chikho cha ukali wanga.
Thus hath said thy Lord, the Eternal, and thy God, who will ever plead for his people, Behold, I have taken out of thy hand the cup of confusion, the deep cup of my fury: thou shalt never more drink it again.
23 Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza, amene ankakuwuza kuti, ‘gona pansi tikuyende pa msana.’ Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo, ngati msewu woti ayendepo.”
And I will place it in the hand of those who have tortured thee, that have said to thy soul, Bend thee down, that we may pass over; and thou madest like the earth thy back, and like the street for those that passed over.