< Yesaya 51 >

1 “Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso ndiponso amene mumafunafuna Yehova: Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;
Listen to me, you who follow what is just and who seek the Lord. Pay attention to the rock from which you have been hewn, and to the walls of the pit from which you have been dug.
2 taganizani za Abrahamu, kholo lanu, ndi Sara, amene anakubalani. Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana, koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.
Pay attention to Abraham, your father, and to Sarah, who bore you. For I called him alone, and I blessed him, and I multiplied him.
3 Yehova adzatonthozadi Ziyoni, ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse; Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni, malo ake owuma ngati munda wa Yehova. Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda ndi kundiyamika.
Therefore, the Lord will console Zion, and he will console all its ruins. And he will turn her desert into a place of delights, and her wilderness into a garden of the Lord. Gladness and rejoicing will be found in her, thanksgiving and a voice of praise.
4 “Mverani Ine, anthu anga: tcherani khutu, inu mtundu wanga: malangizo adzachokera kwa Ine; cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.
Pay attention to me, my people, and listen to me, my tribes. For a law will go forth from me, and my judgment will rest as a light for the nations.
5 Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga. Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga; ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse. Mayiko akutali akundiyembekezera. Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.
My just one is near. My savior has gone forth. And my arms will judge the people. The islands will hope in me, and they will patiently wait for my arm.
6 Kwezani maso anu mlengalenga, yangʼanani pansi pa dziko; mlengalenga udzazimirira ngati utsi, dziko lapansi lidzatha ngati chovala ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe. Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya, chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.
Lift up your eyes to heaven, and look down to the earth below. For the heavens will vanish like smoke, and the earth will be worn away like a garment, and its inhabitants will pass away in like manner. But my salvation will be forever, and my justice will not fail.
7 “Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi, anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu; musaope kudzudzulidwa ndi anthu kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.
Listen to me, you who know what is just, my people who have my law in their heart. Do not be afraid of disgrace among men, and do not dread their blasphemies.
8 Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala; mbozi idzawadya ngati thonje. Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya, chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”
For the worm will consume them like a garment, and the moth will devour them like wool. But my salvation will be forever, and my justice will be from generation to generation.
9 Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe, Inu Yehova; dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana, monga nthawi ya mibado yakale. Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe, amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?
Rise up, Rise up! Clothe yourself in strength, O arm of the Lord! Rise up as in the days of antiquity, as in generations long past. Have you not struck the arrogant one and wounded the dragon?
10 Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu, madzi ozama kwambiri aja? Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama, kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?
Have not you dried up the sea, the waters of the great abyss, and turned the depths of the sea into a road, so that the delivered could cross over it?
11 Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa; chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo. Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe, chisoni ndi kubuwula zidzathawa.
And now, those who have been redeemed by the Lord will return. And they will arrive in Zion, praising. And everlasting rejoicing will be upon their heads. They will take hold of gladness and rejoicing. Anguish and mourning will flee away.
12 Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima. Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa? Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.
It is I, I myself, who will console you. Who are you that you would be afraid of a mortal man, and of a son of man, who will wither like the grass?
13 Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu, amene anayala za mlengalenga ndi kuyika maziko a dziko lapansi. Inu nthawi zonse mumaopsezedwa chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani amene angofuna kukuwonongani. Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?
And have you forgotten the Lord, your Maker, who extended the heavens, and who founded the earth? And have you been in constant dread, all day long, at the face of his fury, of the one who afflicted you and who had prepared to destroy you? Where is the fury of the oppressor now?
14 Amʼndende adzamasulidwa posachedwa; sadzalowa mʼmanda awo, kapena kusowa chakudya.
Advancing quickly, he will arrive to be revealed, and he will not kill unto utter destruction, nor will his bread fail.
15 Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
But I am the Lord, your God, who stirs up the sea, and who makes the waves swell. The Lord of hosts is my name.
16 Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa. Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga, ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi, ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’”
I have placed my words in your mouth, and I have protected you in the shadow of my hand, so that you might plant the heavens, and found the earth, and so that you might say to Zion, “You are my people.”
17 Dzambatuka, dzambatuka! Imirira iwe Yerusalemu. Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo chimene Yehova anakupatsa. Iwe amene unagugudiza chikho chochititsa chizwezwe.
Lift up, Lift up! Arise, O Jerusalem! You drank, from the hand of the Lord, the cup of his wrath. You drank, even to the bottom of the cup of deep sleep. And you were given to drink, all the way to the dregs.
18 Mwa ana onse amene anabereka, panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera; mwa ana onse amene analera, panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.
There is no one who can uphold her, out of all the sons whom she has conceived. And there is no one who would take her by the hand, out of all the sons whom she has raised.
19 Mavuto awiriwa akugwera iwe. Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga. Ndani angakumvere chisoni? Ndani angakutonthoze?
There are two things which have happened to you. Who will be saddened over you? There is devastation and destruction, and famine and sword. Who will console you?
20 Ana ako akomoka; ali lambalamba pa msewu, ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde. Ukali wa Yehova ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.
Your sons have been cast out. They have slept at the head of all the roads, and they have been ensnared like a gazelle. They have been filled by the indignation of the Lord, by the rebuke of your God.
21 Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika, iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.
Therefore, listen to this, O poor little ones, and you who have been inebriated, but not by wine.
22 Ambuye Yehova wanu, Mulungu amene amateteza anthu ake akuti, “Taona, ndachotsa mʼdzanja lako chikho chimene chimakuchititsa kudzandira; sudzamwanso chikho cha ukali wanga.
Thus says your Sovereign, the Lord, and your God, who will fight on behalf of his people: Behold, I have taken the cup of deep sleep from your hand. You shall no longer drink from the bottom of the cup of my indignation.
23 Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza, amene ankakuwuza kuti, ‘gona pansi tikuyende pa msana.’ Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo, ngati msewu woti ayendepo.”
And I will set it in the hand of those who have humiliated you, and who have said to your soul: “Bow down, so that we pass over.” And you placed your body on the ground, as a path for them to pass over.

< Yesaya 51 >