< Yesaya 50 >

1 Yehova akuti, “Kalata imene ndinasudzulira amayi anu ili kuti? Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole, ndinakugulitsani kwa ati? Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu; amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.
Овако вели Господ: Где је распусна књига матере ваше којом је пустих? Или који је између рукодавалаца мојих коме вас продадох? Гле, за безакоња своја продадосте се и за ваше преступе би пуштена мати ваша.
2 Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu? Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha? Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani? Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani? Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu, mitsinje ndinayisandutsa chipululu; nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi; ndipo zinafa ndi ludzu.
Зашто кад дођох не би никога? Кад звах, нико се не одазва? Да није како год окраћала рука моја, те не може искупити? Или нема у мене снаге да избавим? Гле, претњом својом исушујем море; обраћам реке у пустињу да се усмрде рибе њихове зато што нестане воде, и мру од жеђи.
3 Ndinaphimba thambo ndi mdima ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”
Облачим небеса у мрак, и кострет им дајем за покривач.
4 Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka. Mmawa mulimonse amandidzutsa, amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.
Господ Господ даде ми језик учен да умем проговорити згодну реч уморном; буди свако јутро, буди ми уши, да слушам као ученици.
5 Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga, ndipo sindinakhale munthu wowukira ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.
Господ Господ отвори ми уши, и ја се не противих, не одступих натраг.
6 Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu; sindinawabisire nkhope yanga anthu ondinyoza ndi ondilavulira.
Леђа своја подметах онима који ме бијаху и образе своје онима који ме чупаху; не заклоних лице своје од руга ни од запљувања.
7 Popeza Ambuye Yehova amandithandiza, sindidzachita manyazi. Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi, chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.
Јер ми Господ Господ помаже, зато се не осрамотих, зато ставих чело своје као кремен, и знам да се нећу постидети.
8 Wondikhalira kumbuyo ali pafupi, ndaninso amene adzandiyimba mlandu? Abwere kuti tionane maso ndi maso! Mdani wanga ndi ndani? Abweretu kuti tilimbane!
Близу је Онај који ме правда; ко ће се прети са мном? Станимо заједно; ко је супарник мој? Нека приступи к мени.
9 Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza. Ndaninso amene adzanditsutsa? Onse adzatha ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
Гле, Господ Господ помагаће ми: ко ће ме осудити? Гле, сви ће они као хаљина оветшати, мољац ће их изјести.
10 Ndani mwa inu amaopa Yehova ndi kumvera mawu a mtumiki wake? Aliyense woyenda mu mdima, popanda chomuwunikira, iye akhulupirire dzina la Yehova ndi kudalira Mulungu wake.
Ко се међу вама боји Господа и слуша глас слуге Његовог? Ко ходи по мраку и нема видела, нека се узда у име Господње и нека се ослања на Бога свог.
11 Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu, lowani mʼmoto wanu womwewo. Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa. Ndipo ine Yehova ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.
Гле, сви који ложите огањ и опасујете се искрама, идите у светлости огња свог и у искрама које распалисте. То вам је из моје руке, у мукама ћете лежати.

< Yesaya 50 >