< Yesaya 50 >
1 Yehova akuti, “Kalata imene ndinasudzulira amayi anu ili kuti? Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole, ndinakugulitsani kwa ati? Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu; amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.
Kastoy ti kuna ni Yahweh, “Sadino ti ayan ti kasuratan ti panagsina a mangipakita nga insinak ti inayo? Ken siasino kadagiti nakautangak ti nangilakoak kadakayo? Kitaenyo, nailakokayo gapu kadagiti basbasolyo, ken gapu iti kinasukiryo, napatalaw ti inayo.
2 Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu? Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha? Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani? Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani? Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu, mitsinje ndinayisandutsa chipululu; nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi; ndipo zinafa ndi ludzu.
Apay nga awan tao idi immayak dita? Apay nga awan simmungbat idi immawagak? Ababa kadi unay ti imak a mangsubbot kenka? Awan kadi iti pannakabalinko a mangispal kadakayo? Kitaenyo, babaen iti panagsaok, matianan ti baybay; pagbalinek a disierto dagiti karayan; matay ken mabuyok dagiti lames kadagitoy gapu iti kinaawan ti danum.
3 Ndinaphimba thambo ndi mdima ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”
Kawesak iti kinasipnget ti tangatang; kalubak daytoy iti nakersang a lupot.”
4 Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka. Mmawa mulimonse amandidzutsa, amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.
Inikkannak ni Yahweh nga Apo iti dila a kas maysa kadagiti nasuroan, tapno agsaoak iti makaited pigsa kadagiti nabannog; ririingennak iti binigat; ririingenna dagiti lapayagko a dumngeg a kas kadagiti nasurroan.
5 Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga, ndipo sindinakhale munthu wowukira ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.
Ti Apo a Yahweh ti nanglukat kadagiti lapayagko, ken saanak a nagsukir, saanak a timmalikud.
6 Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu; sindinawabisire nkhope yanga anthu ondinyoza ndi ondilavulira.
Intayak ti bukotko kadagiti mangsapsaplit kaniak, ken dagiti pingpingko kadagiti mangparut kadagiti barbasko; saanko nga inlinged ti rupak manipud iti pannakaibabain ken pannakatuptupra.
7 Popeza Ambuye Yehova amandithandiza, sindidzachita manyazi. Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi, chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.
Ta tulongannakto ni Yahweh nga Apo; saanak ngarud a naibabain, pinagbalinko a kasla bato ti rupak, ta ammok a saanakto a maibabain.
8 Wondikhalira kumbuyo ali pafupi, ndaninso amene adzandiyimba mlandu? Abwere kuti tionane maso ndi maso! Mdani wanga ndi ndani? Abweretu kuti tilimbane!
Adda iti asideg ti mangipaduyakyak nga awan basolko. Siasino ti sumupiat kaniak? Tumakdertayo ket agsasangotayo. Siasino ti mangakusar kaniak? Umasideg koma ngarud kaniak.
9 Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza. Ndaninso amene adzanditsutsa? Onse adzatha ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
Kitaenyo, tulongannakto ni Yahweh nga Apo. Siasino ti mangibaga a nagbasolak? Kitaenyo, rumukopdanto amin a kasla lupot; kanento ida ti buot.
10 Ndani mwa inu amaopa Yehova ndi kumvera mawu a mtumiki wake? Aliyense woyenda mu mdima, popanda chomuwunikira, iye akhulupirire dzina la Yehova ndi kudalira Mulungu wake.
Siasino kadakayo ti agbutbuteng kenni Yahweh? Siasino ti agtultulnog iti timek ti adipenna? Siasino ti magmagna iti kasipngetan nga awan ti silawna? Rumbeng nga agtalek isuna iti nagan ni Yahweh ken agtalek iti Diosna.
11 Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu, lowani mʼmoto wanu womwewo. Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa. Ndipo ine Yehova ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.
Kitaenyo, dakayo amin a agpasged iti apuy, a kanayon nga adda awitna a pagsilawan: magnakayo iti lawag dagiti apuyyo ken kadagiti gil-ayab ti pinasgedanyo. Daytoy ti naawatyo kaniak; agiddakayonto iti disso iti ut-ot.