< Yesaya 50 >

1 Yehova akuti, “Kalata imene ndinasudzulira amayi anu ili kuti? Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole, ndinakugulitsani kwa ati? Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu; amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.
thus to say LORD where? this scroll: document divorce mother your which to send: divorce her or who? from to lend me which to sell [obj] you to/for him look! in/on/with iniquity: crime your to sell and in/on/with transgression your to send: divorce mother your
2 Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu? Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha? Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani? Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani? Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu, mitsinje ndinayisandutsa chipululu; nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi; ndipo zinafa ndi ludzu.
why? to come (in): come and nothing man: anyone to call: call to and nothing to answer be short be short hand: power my from redemption and if: surely no nothing in/on/with me strength to/for to rescue look! in/on/with rebuke my to dry sea to set: make river wilderness to stink fish their from nothing water and to die in/on/with thirst
3 Ndinaphimba thambo ndi mdima ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”
to clothe heaven darkness and sackcloth to set: make covering their
4 Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka. Mmawa mulimonse amandidzutsa, amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.
Lord YHWH/God to give: give to/for me tongue disciple to/for to know to/for to help [obj] weary word to rouse in/on/with morning in/on/with morning to rouse to/for me ear to/for to hear: hear like/as disciple
5 Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga, ndipo sindinakhale munthu wowukira ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.
Lord YHWH/God to open to/for me ear and I not to rebel back not to turn
6 Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu; sindinawabisire nkhope yanga anthu ondinyoza ndi ondilavulira.
back my to give: give to/for to smite and jaw my to/for to smooth face my not to hide from shame and spittle
7 Popeza Ambuye Yehova amandithandiza, sindidzachita manyazi. Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi, chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.
and Lord YHWH/God to help to/for me upon so not be humiliated upon so to set: make face my like/as flint and to know for not be ashamed
8 Wondikhalira kumbuyo ali pafupi, ndaninso amene adzandiyimba mlandu? Abwere kuti tionane maso ndi maso! Mdani wanga ndi ndani? Abweretu kuti tilimbane!
near to justify me who? to contend with me to stand: stand unitedness who? master: [master of] justice: judgement my to approach: approach to(wards) me
9 Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza. Ndaninso amene adzanditsutsa? Onse adzatha ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
look! Lord YHWH/God to help to/for me who? he/she/it be wicked me look! all their like/as garment to become old moth to eat them
10 Ndani mwa inu amaopa Yehova ndi kumvera mawu a mtumiki wake? Aliyense woyenda mu mdima, popanda chomuwunikira, iye akhulupirire dzina la Yehova ndi kudalira Mulungu wake.
who? in/on/with you afraid LORD to hear: obey in/on/with voice servant/slave his which to go: walk darkness and nothing brightness to/for him to trust in/on/with name LORD and to lean in/on/with God his
11 Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu, lowani mʼmoto wanu womwewo. Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa. Ndipo ine Yehova ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.
look! all your to kindle fire to gird missile to go: walk in/on/with flame fire your and in/on/with missile to burn: burn from hand my to be this to/for you to/for torment to lie down: lay down [emph?]

< Yesaya 50 >