< Yesaya 50 >

1 Yehova akuti, “Kalata imene ndinasudzulira amayi anu ili kuti? Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole, ndinakugulitsani kwa ati? Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu; amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.
Thus - he says Yahweh where? this [is] [the] document of [the] divorce of mother your which I sent away her or who? [is one] of creditors my whom I sold you to him here! for iniquities your you were sold and for transgressions your she was sent away mother your.
2 Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu? Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha? Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani? Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani? Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu, mitsinje ndinayisandutsa chipululu; nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi; ndipo zinafa ndi ludzu.
Why? did I come and there not [was] anyone did I call? and there not [was one who] answered ¿ really was it [too] short hand my for ransom and or? [was] there not in me strength to deliver here! by rebuke my I dry up [the] sea I make rivers a wilderness it will stink fish their from not water and it will die by thirst.
3 Ndinaphimba thambo ndi mdima ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”
I clothe [the] heavens darkness and sackcloth I make covering their.
4 Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka. Mmawa mulimonse amandidzutsa, amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.
[the] Lord Yahweh he has given to me a tongue of disciples to know to help [the] weary a word he awakens - in the morning in the morning he awakens of me ear to hear like disciples.
5 Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga, ndipo sindinakhale munthu wowukira ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.
[the] Lord Yahweh he has opened of me ear and I not I have been rebellious backwards not I have turned back.
6 Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu; sindinawabisire nkhope yanga anthu ondinyoza ndi ondilavulira.
Back my I gave to [those who] struck [it] and cheeks my to [those who] made [them] bare face my not I hid from insults and spittle.
7 Popeza Ambuye Yehova amandithandiza, sindidzachita manyazi. Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi, chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.
And [the] Lord Yahweh he helps me there-fore not I have been humiliated there-fore I have made face my like flint and I have perceived that not I will be put to shame.
8 Wondikhalira kumbuyo ali pafupi, ndaninso amene adzandiyimba mlandu? Abwere kuti tionane maso ndi maso! Mdani wanga ndi ndani? Abweretu kuti tilimbane!
[is] near [the one who] justifies Me who? will he contend with me let us stand together who? [is] [the] master of case my let him draw near to me.
9 Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza. Ndaninso amene adzanditsutsa? Onse adzatha ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
Here! [the] Lord Yahweh he helps me who? he will he condemn as guilty me there! all of them like garment they will wear out moth it will eat them.
10 Ndani mwa inu amaopa Yehova ndi kumvera mawu a mtumiki wake? Aliyense woyenda mu mdima, popanda chomuwunikira, iye akhulupirire dzina la Yehova ndi kudalira Mulungu wake.
Who? among you [is] fearing Yahweh [is] listening to [the] voice of servant his [the one] who - he has walked darkness and not brightness [belongs] to him let him trust in [the] name of Yahweh and let him depend on God his.
11 Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu, lowani mʼmoto wanu womwewo. Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa. Ndipo ine Yehova ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.
Here! O all of you [who] kindle a fire [who] gird on firebrands walk - by [the] light of fire your and with [the] firebrands [which] you have kindled from hand my it will belong this to you to pain you will lie down!

< Yesaya 50 >