< Yesaya 50 >
1 Yehova akuti, “Kalata imene ndinasudzulira amayi anu ili kuti? Kapena mwa anthu amene ndili nawo ngongole, ndinakugulitsani kwa ati? Inu munagulitsidwa ku ukapolo chifukwa cha machimo anu; amayi anu anachotsedwa chifukwa cha kulakwa kwanu.
Ovako govori Jahve: “Gdje je otpusno pismo vaše matere kojim sam je otpustio? Ili tko je od mojih vjerovnika taj komu sam vas prodao? Zbog bezakonja ste svojih prodani, zbog nevjere je mati vaša otpuštena.
2 Nʼchifukwa chiyani pamene ndinabwera kudzakupulumutsani panalibe munthu? Pamene ndinayitana, nʼchifukwa chiyani panalibe wondiyankha? Kodi dzanja langa ndi lalifupi kuti nʼkulephera kukuwombolani? Kodi ndilibe mphamvu zokupulumutsirani? Ndi kudzudzula kokha ndinawumitsa nyanja yayikulu, mitsinje ndinayisandutsa chipululu; nsomba za mʼmenemo zinawola chifukwa chosowa madzi; ndipo zinafa ndi ludzu.
Zašto ne nađoh nikoga kad sam došao? Zašto se ne odazva nitko kad sam zazvao? Zar mi je ruka prekratka da izbavi, ili u meni snage nema da oslobodim? Gle, prijetnjom svojom isušujem more, u pustinje rijeke pretvaram; njihove se ribe raspadaju jer vode nema i od žeđi ugibaju.
3 Ndinaphimba thambo ndi mdima ndipo chiguduli chinakhala chofunda chake.”
Nebesa oblačim u tminu i kostrijet im dajem za pokrivač!”
4 Ambuye Yehova anandiphunzitsa mawu oyenera kuyankhula kudziwa mawu olimbitsa mtima anthu ofowoka. Mmawa mulimonse amandidzutsa, amathwetsa khutu langa kuti ndimve monga amachitira munthu amene akuphunzira.
Gospod Jahve dade mi jezik vješt da znam riječju krijepiti umorne. Svako jutro on mi uho budi da ga slušam kao učenici.
5 Ambuye Yehova wanditsekula makutu anga, ndipo sindinakhale munthu wowukira ndipo sindinabwerere mʼmbuyo.
Gospod Jahve uši mi otvori: ne protivih se niti uzmicah.
6 Ndinapereka msana wanga kwa ondimenya masaya anga ndinawapereka kwa anthu ondizula ndevu; sindinawabisire nkhope yanga anthu ondinyoza ndi ondilavulira.
Leđa podmetnuh onima što me udarahu, a obraze onima što mi bradu čupahu, i lica svojeg ne zaklonih od uvreda ni od pljuvanja.
7 Popeza Ambuye Yehova amandithandiza, sindidzachita manyazi. Tsono ndalimba mtima ngati msangalabwi, chifukwa ndikudziwa kuti sindidzachita manyazi.
Gospod mi Jahve pomaže, zato se neću smesti. Zato učinih svoj obraz k'o kremen i znam da se neću postidjeti.
8 Wondikhalira kumbuyo ali pafupi, ndaninso amene adzandiyimba mlandu? Abwere kuti tionane maso ndi maso! Mdani wanga ndi ndani? Abweretu kuti tilimbane!
Blizu je onaj koji mi pravo daje. Tko će se pravdati sa mnom? Iziđimo zajedno! Tko je protivnik moj u parnici? Nek' mi se približi!
9 Ambuye Yehova ndiye amene amandithandiza. Ndaninso amene adzanditsutsa? Onse adzatha ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
Gle, Gospod mi Jahve pomaže, tko će me osuditi? Svi će se oni k'o haljina izlizati, moljac će ih razjesti.
10 Ndani mwa inu amaopa Yehova ndi kumvera mawu a mtumiki wake? Aliyense woyenda mu mdima, popanda chomuwunikira, iye akhulupirire dzina la Yehova ndi kudalira Mulungu wake.
“Tko god se od vas Jahve boji, nek' posluša glas Sluge njegova! Tko u tmini hodi, bez tračka svjetlosti, nek' se uzda u ime Jahvino, nek' se na Boga svog osloni.
11 Koma tsopano inu nonse amene mumasonkha moto ndi kuyatsa sakali za moto kufuna kuwononga anzanu, lowani mʼmoto wanu womwewo. Pitani mu sakali za moto zimene mwayatsa. Ndipo ine Yehova ndiye amene ndidzakugwetsereni mazunzowo.
Ali svi vi oganj palite, raspirujete žeravicu. Idite u plamenove ognja svojega i u žeravu koju raspiriste. Tako će vam moja učiniti ruka: ležat ćete u mukama.