< Yesaya 49 >
1 Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali: Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe, ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.
Poslušajte me, oh otoki in prisluhnite, ve ljudstva od daleč. Gospod me je poklical iz maternice, od notranjosti moje matere je naredil omembo mojega imena.
2 Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa, anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake; Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa ndipo anandibisa mʼchimake.
Moja usta je naredil kakor oster meč; v senco svoje roke me je skril in me naredil zglajeno puščico; v svojem tulu me je skril
3 Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli. Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”
in mi rekel: »Ti si moj služabnik, oh Izrael, v katerem bom proslavljen.«
4 Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe, koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova, ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”
Potem sem rekel: »V prazno sem se trudil, svojo moč sem porabil zaman in v prazno. Vendar je zagotovo moja sodba z Gospodom in moje delo z mojim Bogom.«
5 Yehova anandiwumba ine mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye, choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova, ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.
»In sedaj, « govori Gospod, ki me je oblikoval od maternice, da bi bil njegov služabnik, da Jakoba ponovno privedem k njemu: »Čeprav Izrael ne bi bil zbran, bom vendar veličasten v Gospodovih očeh in moj Bog bo moja moč.«
6 Yehovayo tsono akuti, “Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga, kuti udzutse mafuko a Yakobo ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka. Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira, udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”
Rekel je: »To je lahka stvar, da bi bil moj služabnik, da vzdigneš Jakobove rodove in da obnoviš Izraelove ohranjene. Prav tako te bom dal za svetlobo poganom, da boš lahko moja rešitev duš do konca zemlje.
7 Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula, Woyerayo wa Israeli akunena, amene mitundu ya anthu inamuda, amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti, “Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira. Akalonga nawonso adzagwada pansi. Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”
Tako govori Gospod, Izraelov Odkupitelj in njegov Sveti tistemu, ki ga človek prezira, tistemu, ki ga narod zaničuje, služabniku vladarjev: ›Kralji bodo videli in vstali, tudi princi bodo oboževali zaradi Gospoda, ki je zvest in Svetega Izraelovega in on bo izbral tebe.‹«
8 Yehova akuti, “Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha, ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza; ndinakusunga ndi kukusandutsa kuti ukhale pangano kwa anthu, kuti dziko libwerere mwakale ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.
Tako govori Gospod: »Ob sprejemljivem času sem te uslišal in na dan rešitve duše sem ti pomagal in ohranil te bom in te dal za zavezo ljudstvu, da povzdigneš deželo, da povzročiš, da podedujejo zapuščene dediščine,
9 Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke ndi a mu mdima kuti aonekere poyera. “Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira ndi msipu pa mʼmalo owuma.
da boš lahko ujetnikom rekel: ›Pojdite naprej; ‹ tistim, ki so v temi: ›Pokažite se.‹ Pasli bodo po poteh in njihovi pašniki bodo na vseh visokih krajih.
10 Iwo sadzamva njala kapena ludzu, kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza; chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.
Ne bodo niti lačni niti žejni, niti jih ne bosta udarila, niti vročina, niti sonce, kajti on, ki ima usmiljenje do njih, jih bo vodil, celo pri vodnih izvirih jih bo usmerjal.
11 Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo, ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.
Vse svoje gore bom naredil pot in moje glavne ceste bodo povišane.
12 Taonani, anthu anga adzachokera kutali, ena kumpoto, ena kumadzulo, enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”
Glej, ti bodo prišli od daleč in glej, ti od severa in od zahoda in ti iz dežele Siním.«
13 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga; kondwera, iwe dziko lapansi; imbani nyimbo inu mapiri! Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.
Prepevaj, oh nebo in bodi radostna, oh zemlja in izbruhnite v petje, oh gore. Kajti Gospod je potolažil svoje ljudstvo in usmiljen bo do svojih trpečih.
14 Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya, Ambuye wandiyiwala.”
Toda Sion je rekel: » Gospod me je zapustil in moj Gospod me je pozabil.«
15 “Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni? Ngakhale iye angathe kuyiwala, Ine sindidzakuyiwala iwe!
Mar lahko ženska pozabi svojega doječega otroka, da ne bi imela sočutja do sina svoje maternice? Da, one lahko pozabijo, vendar jaz ne bom pozabil tebe.
16 Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga; makoma ako ndimawaona nthawi zonse.
Glej, vrezal sem te na dlani svojih rok, tvoja obzidja so nenehno pred menoj.
17 Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira, ndipo amene anakupasula akuchokapo.
Tvoji otroci se bodo podvizali, tvoji uničevalci in tisti, ki so te naredili opustošeno, bodo šli od tebe.
18 Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe. Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo, anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’
Dvigni svoje oči naokoli in poglej. Vsi ti se zbirajo skupaj in prihajajo k tebi. Kakor jaz živim, ‹ govori Gospod, ›zanesljivo se boš oblekla z njimi vsemi, kakor z ornamentom in si jih privezala nase, kakor stori nevesta.
19 “Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa ndipo dziko lako ndi kusakazidwa, chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.
Kajti tvoji opustošeni in tvoji zapuščeni kraji in dežela tvojega uničenja bo sedaj torej preozka zaradi prebivalcev in tisti, ki so te pogoltnili, bodo daleč proč.
20 Ana obadwa nthawi yako yachisoni adzanena kuti, ‘Malo ano atichepera, tipatse malo ena woti tikhalemo.’
Otroci, ki jih boš imela, potem ko si izgubila druge, bodo v tvoja ušesa ponovno govorili: ›Kraj je preozek zame. Daj mi prostor, da bom lahko prebival.‹
21 Tsono iwe udzadzifunsa kuti, ‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa? Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena; ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa. Ndani anawalera ana amenewa? Ndinatsala ndekha, nanga awa, achokera kuti?’”
Potem boš v svojem srcu rekla: ›Kdo mi je te rodil, glede na to, da sem izgubila svoje otroke in sem zapuščena, ujetnica in se selim sem ter tja? In kdo je te vzgojil? Glej, sama sem ostala, kje so bili tile?‹«
22 Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi, “Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere. Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere. Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.
Tako govori Gospod Bog: »Glej, svojo roko bom dvignil k poganom in svoj prapor postavil k ljudstvu in tvoje sinove bodo privedli na njihovih rokah in tvoje hčere bodo nošene na njihovih ramah.
23 Mafumu adzakhala abambo wongokulera ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera. Iwo adzagwetsa nkhope zawo pansi. Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova; iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”
Kralji bodo tvoji negovalni očetje in njihove kraljice tvoje negovalne matere. S svojim obrazom se bodo priklonili k tebi proti zemlji in lizali prah tvojih stopal in vedela boš, da jaz sem Gospod, kajti tisti, ki čakajo name, ne bodo osramočeni.
24 Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo, kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?
Mar bo plen vzet od mogočnega, mar bo pravično ujetništvo osvobojeno?«
25 Koma zimene Yehova akunena ndi izi, “Ankhondo adzawalanda amʼndende awo, ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo; ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu, ndipo ndidzapulumutsa ana anu.
Toda tako govori Gospod: »Celo ujetniki mogočnega bodo odvzeti in plen strašnega bo osvobojen, kajti jaz se bom spoprijel s tistim, ki se spoprijema s teboj in jaz bom rešil tvoje otroke.
26 Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe; adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu, Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”
Z njihovim lastnim mesom bom hranil tiste, ki te zatirajo in pijani bodo s svojo lastno krvjo kakor s sladkim vinom in vse meso bo vedelo, da jaz sem Gospod, tvoj Odrešenik in tvoj Odkupitelj, Mogočni Jakobov.‹«