< Yesaya 49 >

1 Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali: Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe, ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.
Ecoutez, îles, et soyez attentifs, peuples éloignés: le Seigneur dès le sein m’a appelé, dès les entrailles de ma mère il s’est souvenu de mon nom.
2 Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa, anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake; Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa ndipo anandibisa mʼchimake.
Il a disposé ma bouche comme un glaive aigu; à l’ombre de sa main il m’a protégé, et il m’a disposé comme une flèche choisie; il m’a caché dans son carquois.
3 Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli. Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”
Et il m’a dit: Mon serviteur, c’est toi, Israël, parce qu’en toi je me glorifierai.
4 Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe, koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova, ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”
Et moi j’ai dit: C’est dans le vide que j’ai travaillé, c’est sans motif et vainement que j’ai consumé ma force; ainsi mon jugement est au pouvoir du Seigneur, et mon travail au pouvoir de Dieu.
5 Yehova anandiwumba ine mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye, choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova, ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.
Et maintenant, dit le Seigneur, qui m’a formé dès le sein de ma mère pour le servir, afin que je ramène Jacob à lui, et Israël ne sera pas rassemblé, et j’ai été glorifié aux yeux du Seigneur, et mon Dieu est devenu ma force.
6 Yehovayo tsono akuti, “Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga, kuti udzutse mafuko a Yakobo ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka. Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira, udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”
Il a donc dit: C’est peu que tu me serves à relever les tribus de Jacob, et à convertir les restes d’Israël. Voici que je t’ai posé en lumière des nations, afin que tu sois mon salut jusqu’à l’extrémité de la terre.
7 Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula, Woyerayo wa Israeli akunena, amene mitundu ya anthu inamuda, amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti, “Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira. Akalonga nawonso adzagwada pansi. Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”
Voici ce que dit le Seigneur, le rédempteur d’Israël, son saint, à une âme méprisable, à une nation détestée, à l’esclave de ceux qui le dominent: Les rois te verront, et les princes se lèveront, et ils l’adoreront à cause du Seigneur, parce qu’il est fidèle, et à cause du saint d’Israël qui t’a choisi.
8 Yehova akuti, “Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha, ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza; ndinakusunga ndi kukusandutsa kuti ukhale pangano kwa anthu, kuti dziko libwerere mwakale ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.
Voici ce que dit le Seigneur: En un temps favorable je t’ai exaucé, et en un jour de salut je t’ai secouru, je t’ai conservé, et je t’ai établi pour faire alliance avec un peuple, afin que tu rétablisses une terre, et que tu possèdes des héritages dissipés;
9 Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke ndi a mu mdima kuti aonekere poyera. “Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira ndi msipu pa mʼmalo owuma.
Afin que tu dises à ceux qui étaient dans les fers: Sortez; et à ceux qui étaient dans les ténèbres: Venez à la lumière. Sur les chemins, ils trouveront à paître, et dans toutes les plaines seront leurs pâturages.
10 Iwo sadzamva njala kapena ludzu, kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza; chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.
Ils n’auront pas faim, ni soif; la chaleur ne les atteindra pas, ni le soleil; parce que celui qui a pitié d’eux les conduira, et à des sources d’eaux il les fera boire.
11 Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo, ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.
Et je disposerai toutes mes montagnes en une voie, et mes sentiers seront élevés.
12 Taonani, anthu anga adzachokera kutali, ena kumpoto, ena kumadzulo, enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”
Voici que ceux-ci viendront de loin, et voici que ceux-là viendront de l’aquilon et de la mer, et ceux-ci de la terre du midi.
13 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga; kondwera, iwe dziko lapansi; imbani nyimbo inu mapiri! Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.
Louez, cieux; exulte, terre; montagnes, faites retentir la louange, parce que le Seigneur a consolé son peuple, et qu’il aura pitié de ses pauvres.
14 Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya, Ambuye wandiyiwala.”
Et Sion a dit: Le Seigneur m’a abandonnée, et le Seigneur m’a oubliée.
15 “Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni? Ngakhale iye angathe kuyiwala, Ine sindidzakuyiwala iwe!
Est-ce qu’une mère peut oublier son enfant, de sorte qu’elle n’ait pas pitié du fils de son sein? mais quand même elle l’oublierait, pour moi, je ne l’oublierai point.
16 Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga; makoma ako ndimawaona nthawi zonse.
Voici que je t’ai gravée dans mes mains; tes murs sont devant mes yeux sans cesse.
17 Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira, ndipo amene anakupasula akuchokapo.
Ils sont venus, tes constructeurs; ceux qui te détruisaient et te dissipaient, sortiront de ton enceinte.
18 Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe. Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo, anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’
Lève tes yeux tout autour et vois; tous ceux-ci se sont rassemblés, et ils sont venus à toi, Je vis, moi, dit le Seigneur: de tous ceux-ci, comme d’un ornement, tu seras revêtue, et tu t’en pareras comme une épouse.
19 “Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa ndipo dziko lako ndi kusakazidwa, chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.
Tes déserts et tes solitudes, et ta terre ruinée seront maintenant étroits eu égard aux habitants, et ils seront mis en fuite au loin, ceux qui te dévoraient.
20 Ana obadwa nthawi yako yachisoni adzanena kuti, ‘Malo ano atichepera, tipatse malo ena woti tikhalemo.’
Ils te diront encore à tes oreilles, les fils de ta stérilité: Le lieu est étroit; fais-moi de l’espace, afin que j’habite.
21 Tsono iwe udzadzifunsa kuti, ‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa? Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena; ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa. Ndani anawalera ana amenewa? Ndinatsala ndekha, nanga awa, achokera kuti?’”
Et tu diras dans ton cœur: Qui m’a engendré ceux-ci? j’étais stérile, et je n’enfantais pas; exilée et captive; et ceux-ci, qui les a nourris? j’étais abandonnée et seule, et ceux-ci, où étaient-ils?
22 Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi, “Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere. Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere. Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.
Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Voici que vers des nations j’élèverai ma main, et devant des peuples je hausserai mon étendard; et ils apporteront tes fils entre leurs bras, et tes filles, ils les porteront sur leurs épaules.
23 Mafumu adzakhala abambo wongokulera ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera. Iwo adzagwetsa nkhope zawo pansi. Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova; iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”
Et les rois seront tes nourriciers, et les reines tes nourrices; la face contre terre, ils se prosterneront devant toi, et ils lécheront la poussière de tes pieds. Et tu sauras que je suis le Seigneur, dans lequel ne seront pas confondus ceux qui l’attendent.
24 Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo, kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?
Est-ce qu’on ôtera à un homme fort sa proie? ou ce qui a été pris par un homme robuste, pourra-t-il être sauvé?
25 Koma zimene Yehova akunena ndi izi, “Ankhondo adzawalanda amʼndende awo, ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo; ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu, ndipo ndidzapulumutsa ana anu.
Parce que voici ce que dit le Seigneur: Certainement et les captifs seront ôtés à un homme fort, et ce qui aura été enlevé par un homme robuste sera sauvé. Or ceux qui t’ont jugée, moi je les jugerai, et tes fils, moi je les sauverai.
26 Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe; adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu, Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”
Et je nourrirai tes ennemis de leurs propres chairs, et comme d’un vin nouveau je les enivrerai de leur sang; et toute chair saura que c’est moi le Seigneur qui te sauve, et que ton rédempteur est le fort de Jacob.

< Yesaya 49 >