< Yesaya 49 >
1 Mverani Ine, inu anthu a pa zilumba tcherani khutu, inu anthu a mayiko akutali: Yehova anandiyitana ine ndisanabadwe, ananditchula dzina ndili mʼmimba ya amayi anga.
Écoutez-moi, îles. Écoutez, vous, peuples, de loin: Yahvé m'a appelé depuis le ventre de ma mère; de l'intérieur de ma mère, il a mentionné mon nom.
2 Iye anasandutsa pakamwa panga kukhala ngati lupanga lakuthwa, anandibisa mu mthunzi wa dzanja lake; Iye anandisandutsa ngati muvi wakuthwa ndipo anandibisa mʼchimake.
Il a rendu ma bouche semblable à une épée tranchante. Il m'a caché dans l'ombre de sa main. Il m'a fait une tige polie. Il m'a gardé près de lui dans son carquois.
3 Iye anati kwa ine, “Ndiwe mtumiki wanga, Israeli. Anthu adzanditamanda chifukwa cha iwe.”
Il m'a dit: « Tu es mon serviteur, Israël, en qui je serai glorifié. »
4 Koma Ine ndinati, “Ine ndinkaganiza kuti ndinagwira ntchito ndi kuwononga mphamvu zanga pachabe, koma ayi, zondiyenera zili mʼmanja a Yehova, ndipo mphotho yanga ili mʼmanja mwa Mulungu wanga.”
Mais j'ai dit: « C'est en vain que j'ai travaillé. J'ai dépensé mes forces en vain pour rien; mais c'est à Yahvé que revient la justice qui m'est due, et ma récompense auprès de mon Dieu. »
5 Yehova anandiwumba ine mʼmimba mwa amayi anga kuti ndikhale mtumiki wake kuti ndibweze fuko la Yakobo kwa Iye ndi kusonkhanitsa Israeli kwa Iye, choncho ndimalemekezeka mʼmaso mwa Yehova, ndipo ndimapeza mphamvu mwa Mulungu wanga.
Or, Yahvé, celui qui m'a formé dès le ventre de ma mère pour être son serviteur, dit de lui ramener Jacob, et de rassembler Israël auprès de lui, car je suis honorable aux yeux de Yahvé, et mon Dieu est devenu ma force.
6 Yehovayo tsono akuti, “Nʼchinthu chochepa kwambiri kwa iwe kuti ukhale mtumiki wanga, kuti udzutse mafuko a Yakobo ndi kuwabweretsa kwawo Aisraeli amene anapulumuka. Choncho iwe udzakhala ngati chowunikira, udzafikitsa uthenga wa chipulumutso changa ku mathero a dziko lapansi.”
En effet, il dit: « C'est une chose trop légère que tu sois mon serviteur pour relever les tribus de Jacob, et de restaurer les préservés d'Israël. Je te donnerai aussi comme lumière aux nations, afin que tu sois mon salut jusqu'au bout du monde. »
7 Yehova Mpulumutsi ndi Woyerayo wa Israeli akuyankhula, Woyerayo wa Israeli akunena, amene mitundu ya anthu inamuda, amenenso anali kapolo wa mafumu ankhanza uja kuti, “Mafumu adzaona ntchito ya chipulumutso changa ndipo adzayimirira. Akalonga nawonso adzagwada pansi. Zimenezi zidzachitika chifukwa cha Yehova amene ndi wokhulupirika ndi Woyerayo wa Israeli amene wakusankha iwe.”
Yahvé, le Rédempteur d'Israël, et son Saint, dit à celui que l'homme méprise, à celui que la nation abhorre, à un serviteur des chefs: « Les rois verront et se lèveront, les princes, et ils se prosterneront, à cause de Yahvé qui est fidèle, le Saint d'Israël, qui t'a choisi. »
8 Yehova akuti, “Pa nthawi imene ndinakukomera mtima ndinakuyankha, ndipo pa tsiku lachipulumutso ndinakuthandiza; ndinakusunga ndi kukusandutsa kuti ukhale pangano kwa anthu, kuti dziko libwerere mwakale ndi kuti cholowa changa chowonongeka chija ndichigawegawenso.
Yahvé dit: « Je t'ai répondu au bon moment. Je vous ai aidé au jour du salut. Je te garderai et te donnerai comme alliance du peuple, pour relever le pays, pour leur faire hériter de l'héritage dévasté,
9 Ndidzawuza a mʼndende kuti atuluke ndi a mu mdima kuti aonekere poyera. “Adzapeza chakudya mʼmphepete mwa njira ndi msipu pa mʼmalo owuma.
en disant à ceux qui sont liés: « Sortez! »; à ceux qui sont dans les ténèbres: « Montrez-vous! « Ils se nourriront le long des chemins, et leur pâturage sera sur toutes les hauteurs sans arbres.
10 Iwo sadzamva njala kapena ludzu, kutentha kwa mʼchipululu kapena dzuwa silidzawapsereza; chifukwa Iye amene amawachitira chifundo adzawatsogolera ndi kuwaperekeza ku akasupe a madzi.
Ils n'auront ni faim ni soif; ni la chaleur ni le soleil ne les frapperont, car celui qui a pitié d'eux les conduira. Il les guidera vers des sources d'eau.
11 Mapiri anga onse ndidzawasandutsa njira yoyendamo, ndipo misewu yanga yayikulu ndidzayikweza.
Je ferai de toutes mes montagnes une route, et mes autoroutes seront exaltées.
12 Taonani, anthu anga adzachokera kutali, ena kumpoto, ena kumadzulo, enanso adzachokera ku chigawo cha Asuwani.”
Voici, ils viennent de loin, et voici ceux du nord et de l'ouest, et ceux-ci du pays de Sinim. »
13 Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga; kondwera, iwe dziko lapansi; imbani nyimbo inu mapiri! Pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, ndipo wachitira chifundo anthu ake ovutika.
Chantez, cieux, et soyez joyeux, terre! Laissez-vous aller à chanter, montagnes! Car Yahvé a réconforté son peuple, et aura de la compassion pour ses affligés.
14 Koma Ziyoni anati, “Yehova wandisiya, Ambuye wandiyiwala.”
Mais Sion dit: « Yahvé m'a abandonné, et le Seigneur m'a oublié. »
15 “Kodi amayi angathe kuyiwala mwana wawo wakubere ndi kusachitira chifundo mwana amene anabereka iwo eni? Ngakhale iye angathe kuyiwala, Ine sindidzakuyiwala iwe!
« Une femme peut-elle oublier son enfant qu'elle allaite, pour qu'elle n'ait pas de compassion pour le fils de ses entrailles? Oui, ils peuvent oublier, mais je ne vous oublierai pas!
16 Taona, ndakulemba iwe mʼzikhantho zanga; makoma ako ndimawaona nthawi zonse.
Voici, je vous ai gravés sur les paumes de mes mains. Vos murs sont continuellement devant moi.
17 Amisiri odzakumanganso akubwerera mofulumira, ndipo amene anakupasula akuchokapo.
Vos enfants se dépêchent. Vos destructeurs et ceux qui vous ont dévasté vous quitteront.
18 Kweza maso ako ndipo uyangʼaneyangʼane ana ako onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe. Yehova akuti, ‘Ine Yehova wamoyo, anthu ako adzakhala ngati chinthu chodzikongoletsa chimene mkwatibwi wavala pa mkono pake.’
Lève les yeux tout autour, et regarde: tous ceux-là se rassemblent et viennent à toi. Je suis vivant, dit Yahvé, et tu t'en revêtiras comme d'une parure, et habille-toi avec, comme une mariée.
19 “Ngakhale unasanduka bwinja ndi kuwonongedwa ndipo dziko lako ndi kusakazidwa, chifukwa cha kuchuluka kwa anthu malo okhalamo adzakhala operewera ndipo amene anakuwononga iwe aja adzakhala kutali.
« En effet, pour ce qui est de tes déchets et de tes lieux désolés, et votre terre qui a été détruite, Il est certain que maintenant cette terre sera trop petite pour les habitants, et ceux qui t'ont englouti seront loin.
20 Ana obadwa nthawi yako yachisoni adzanena kuti, ‘Malo ano atichepera, tipatse malo ena woti tikhalemo.’
Les enfants de ton deuil diront à tes oreilles, Cet endroit est trop petit pour moi. Donnez-moi un endroit où vivre.
21 Tsono iwe udzadzifunsa kuti, ‘Kodi ndani anandiberekera ana amenewa? Ana anga onse anamwalira ndipo sindinathenso kukhala ndi ana ena; ndinapita ku ukapolo ndipo ndinachotsedwa. Ndani anawalera ana amenewa? Ndinatsala ndekha, nanga awa, achokera kuti?’”
Alors tu diras dans ton cœur: « Qui les a conçus pour moi, puisque je suis privé de mes enfants? et que je suis seul, exilé, et que j'erre de long en large? Qui les a évoqués? Voici, j'ai été laissé seul. Où étaient-ils? »
22 Zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi, “Taonani, Ine ndidzakodola Anthu a mitundu ina kuti abwere. Ndidzawakwezera anthu a mitundu ina mbendera yanga kuti abwere. Tsono adzabwera ndi ana ako aamuna atawanyamula mʼmanja mwawo ndipo adzanyamula ana ako aakazi pa mapewa awo.
Le Seigneur Yahvé dit: « Voici que je lève ma main vers les nations, et je lèverai ma bannière vers les peuples. Ils porteront vos fils dans leur sein, et vos filles seront portées sur leurs épaules.
23 Mafumu adzakhala abambo wongokulera ndipo akazi a mafumu adzakhala amayi wongokulera. Iwo adzagwetsa nkhope zawo pansi. Ndiye inu mudzazindikira kuti Ine ndine Yehova; iwo amene amadalira Ine sadzakhumudwa.”
Les rois seront vos pères nourriciers, et leurs reines vos mères nourricières. Ils se prosterneront devant toi, le visage tourné vers la terre, et lécher la poussière de vos pieds. Alors vous saurez que je suis Yahvé; et ceux qui m'attendent ne seront pas déçus. »
24 Kodi mungathe kulanda anthu ankhondo zofunkha zawo, kapena kupulumutsa anthu ogwidwa mʼdzanja la munthu wankhanza?
Le butin sera pris aux puissants, ou que les captifs légitimes soient délivrés?
25 Koma zimene Yehova akunena ndi izi, “Ankhondo adzawalanda amʼndende awo, ndipo munthu woopsa adzamulanda zofunkha zawo; ndidzalimbana ndi amene amalimbana nanu, ndipo ndidzapulumutsa ana anu.
Mais Yahvé dit: « Même les captifs des puissants seront emmenés, et le butin récupéré sur le féroce, car je me battrai avec celui qui se battra avec vous. et je sauverai vos enfants.
26 Anthu amene anakuponderezani adzadya mnofu wawo omwe; adzamwa magazi awo omwe ngati aledzera ndi vinyo. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wanu, Momboli wanu, Wamphamvu wa Yakobo.”
Je nourrirai de leur propre chair ceux qui vous oppriment; et ils s'enivreront de leur propre sang, comme d'un vin doux. Alors toute chair saura que moi, Yahvé, je suis votre Sauveur. et ton rédempteur, le Puissant de Jacob. »